< Job 31 >

1 Pepigi fœdus cum oculis meis ut ne cogitarem quidem de virgine.
“Ndinachita pangano ndi maso anga kuti sindidzapenya namwali momusirira.
2 Quam enim partem haberet in me Deus desuper, et hereditatem Omnipotens de excelsis?
Kodi Mulungu kumwambako wandisungira zotani? Kodi cholowa changa chochokera kwa Wamphamvuzonse kumwambako nʼchotani?
3 Numquid non perditio est iniquo, et alienatio operantibus iniustitiam?
Kodi si chiwonongeko kwa anthu oyipa, tsoka kwa iwo amene amachita zolakwa?
4 Nonne ipse considerat vias meas, et cunctos gressus meos dinumerat?
Kodi Mulungu saona zochita zanga, ndi kudziwa mayendedwe anga?
5 Si ambulavi in vanitate, et festinavit in dolo pes meus:
“Ngati ndachita zinthu mwachiphamaso, kapena kufulumira kukachita zachinyengo,
6 Appendat me in statera iusta, et sciat Deus simplicitatem meam.
Mulungu andiyeze ndi muyeso wake wolungama ndipo Iye adzadziwa kuti ine ndine wosalakwa,
7 Si declinavit gressus meus de via, et si secutum est oculos meos cor meum, et si manibus meis adhæsit macula:
ngati mayendedwe anga asempha njira, ngati mtima wanga wakhumbira zimene maso anga aona, kapena ngati ndachita choyipa chilichonse.
8 Seram, et alium comedat: et progenies mea eradicetur.
Pamenepo ena adye zimene ndinadzala, ndipo zomera zanga zizulidwe.
9 Si deceptum est cor meum super muliere, et si ad ostium amici mei insidiatus sum:
“Ngati mtima wanga unakopekapo ndi mkazi, ndipo ngati ndinalakalaka mkazi wa mnansi wanga,
10 Scortum alterius sit uxor mea, et super illam incurventur alii.
pamenepo mkazi wanga aphikire mwamuna wina chakudya, ndipo amuna ena azigona naye.
11 Hoc enim nefas est, et iniquitas maxima.
Pakuti zimenezo zikanakhala zochititsa manyazi, tchimo loyenera kulangidwa nalo.
12 Ignis est usque ad perditionem devorans, et omnia eradicans genimina.
Ndi moto umene umayaka mpaka chiwonongeko; ukanapsereza zokolola zanga.
13 Si contempsi subire iudicium cum servo meo, et ancilla mea, cum disceptarent adversum me:
“Ngati ndinkapondereza mlandu wa akapolo anga aamuna kapena aakazi, pamene ankabwera kwa ine ndi milandu yawo,
14 Quid enim faciam cum surrexerit ad iudicandum Deus? et cum quæsierit, quid respondebo illi?
ndidzatani pamene Mulungu adzanditsutsa? Nanga ndidzayankha chiyani akadzandifunsa?
15 Numquid non in utero fecit me qui et illum operatus est: et formavit me in vulva unus?
Kodi amene anapanga ine mʼmimba mwa amayi anga si yemwe anapanganso iwo? Kodi si mmodzi yemweyo amene anatipanga tonsefe mʼmimba mwa amayi athu?
16 Si negavi, quod volebant, pauperibus, et oculos viduæ expectare feci:
“Ngati ndinawamana aumphawi zinthu zimene ankazikhumba, kapena kuwagwiritsa fuwa lamoto akazi amasiye amene amafuna thandizo kwa ine,
17 Si comedi buccellam meam solus, et non comedit pupillus ex ea:
ngati chakudya changa ndinadya ndekha, wosagawirako mwana wamasiye,
18 (Quia ab infantia mea crevit mecum miseratio: et de utero matris meæ egressa est mecum.)
chonsechotu kuyambira unyamata wanga ndinamulera monga abambo ake, ndipo moyo wanga wonse ndakhala ndikusamalira akazi amasiye,
19 Si despexi pereuntem, eo quod non habuerit indumentum, et absque operimento pauperem:
ngati ndinaona wina aliyense akuzunzika ndi usiwa, kapena munthu wosauka alibe chofunda,
20 Si non benedixerunt mihi latera eius, et de velleribus ovium mearum calefactus est:
ndipo ngati iyeyo sananditamandepo chifukwa chomufunditsa ndi nsalu ya ubweya wankhosa,
21 Si levavi super pupillum manum meam, etiam cum viderem me in porta superiorem:
ngati ndinaopsezapo mwana wamasiye, poganiza kuti ndinali ndi mphamvu mʼbwalo la milandu,
22 Humerus meus a iunctura sua cadat, et brachium meum cum suis ossibus confringatur.
pamenepo phewa langa lipokonyeke, mkono wanga ukonyoke polumikizira pake.
23 Semper enim quasi tumentes super me fluctus timui Deum, et pondus eius ferre non potui.
Popeza ine ndinaopa kwambiri chiwonongeko chochokera kwa Mulungu, ndinachitanso mantha ndi ulemerero wake, sindikanatha kuchita zinthu zimenezi.
24 Si putavi aurum robur meum, et obrizo dixi: Fiducia mea.
“Ngati ndinayika mtima wanga pa chuma kapena kunena kwa golide wabwino kwambiri kuti, ‘Iwe ndiye chitetezo changa,’
25 Si lætatus sum super multis divitiis meis, et quia plurima reperit manus mea.
ngati ndinakondwera chifukwa choti chuma changa chinali chambiri, zinthu zimene manja anga anazipeza,
26 Si vidi solem cum fulgeret, et lunam incedentem clare:
ngati pamene ndinaona dzuwa likuwala, kapena mwezi ukuyenda mwa ulemerero wake,
27 Et lætatum est in abscondito cor meum, et osculatus sum manum meam ore meo.
ndipo kuti mtima wanga unakopeka nazo nʼkuyika dzanja langa pakamwa mozilemekeza,
28 Quæ est iniquitas maxima, et negatio contra Deum altissimum.
pamenepo zimenezinso zikanakhala machimo oti ndilangidwe nawo, chifukwa ndikanakhala wosakhulupirika kwa Mulungu wakumwamba.
29 Si gavisus sum ad ruinam eius, qui me oderat, et exultavi quod invenisset eum malum.
“Ngati ndinasangalala ndi kuwonongeka kwa mdani wanga, kapena kusekera mavuto pamene mavuto anamugwera,
30 Non enim dedi ad peccandum guttur meum, ut expeterem maledicens animam eius.
ine sindinachimwe ndi pakamwa panga potulutsa matemberero a mdani wanga kuti awonongeke,
31 Si non dixerunt viri tabernaculi mei: Quis det de carnibus eius ut saturemur:
ngati anthu amene ndimakhala nawo mʼnyumba mwanga sananenepo kuti, ‘Kodi ndani amene sakhuta ndi chakudya cha Yobu?’
32 Foris non mansit peregrinus, ostium meum viatori patuit.
Komatu mlendo sindinamusiye pa msewu usiku wonse, pakuti khomo langa linali lotsekuka nthawi zonse kwa alendo,
33 Si abscondi quasi homo peccatum meum, et celavi in sinu meo iniquitatem meam.
ngati ndinabisa tchimo langa monga amachitira anthu ena, kubisa kulakwa mu mtima mwanga
34 Si expavi ad multitudinem nimiam, et despectio propinquorum terruit me: et non magis tacui, nec egressus sum ostium.
chifukwa choopa gulu la anthu, ndi kuchita mantha ndi mnyozo wa mafuko kotero ndinakhala chete ndipo sindinatuluke panja.
35 Quis mihi tribuat auditorem, ut desiderium meum audiat Omnipotens: et librum scribat ipse qui iudicat.
“Aa, pakanakhala wina wondimva! Tsopano ndikutsiriza mawu anga odzitetezera. Wamphamvuzonse andiyankhe; mdani wanga achite kulemba pa kalata mawu ake ondineneza.
36 Ut in humero meo portem illum, et circumdem illum quasi coronam mihi?
Ndithu ine ndikanakoleka kalatayo pa phewa langa, ndikanayivala kumutu ngati chipewa chaufumu.
37 Per singulos gradus meos pronunciabo illum, et quasi principi offeram eum.
Ndikanamufotokozera zonse zimene ndinachita; ndikanafika pamaso pake ngati kalonga.
38 Si adversum me terra mea clamat, et cum ipsa sulci eius deflent:
“Ngati minda yanga ikulira monditsutsa ine ndipo malo ake onse osalimidwa anyowa ndi misozi,
39 Si fructus eius comedi absque pecunia, et animam agricolarum eius afflixi:
ngati ndinadya za mʼminda mwake osapereka ndalama kapena kukhumudwitsa anthu olima mʼmindamo,
40 Pro frumento oriatur mihi tribulus, et pro hordeo spina. (Finita sunt verba Iob.)
pamenepo mʼmindamo mumere namsongole mʼmalo mwa tirigu ndi udzu mʼmalo mwa barele.” Mawu a Yobu athera pano.

< Job 31 >