< Psalmorum 105 >

1 Alleluja. [Confitemini Domino, et invocate nomen ejus; annuntiate inter gentes opera ejus.
Yamikani Yehova, itanani dzina lake; lalikirani pakati pa anthu a mitundu ina zimene Iye wachita.
2 Cantate ei, et psallite ei; narrate omnia mirabilia ejus.
Imbirani Iye, imbani matamando kwa Iyeyo; fotokozani za machitidwe ake onse odabwitsa.
3 Laudamini in nomine sancto ejus; lætetur cor quærentium Dominum.
Munyadire dzina lake loyera; mitima ya iwo amene amafunafuna Yehova ikondwere.
4 Quærite Dominum, et confirmamini; quærite faciem ejus semper.
Dalirani Yehova ndi mphamvu zake; funafunani nkhope yake nthawi yonse.
5 Mementote mirabilium ejus quæ fecit; prodigia ejus, et judicia oris ejus:
Kumbukirani zodabwitsa zimene Iye anazichita, zozizwitsa zake ndi maweruzo amene anapereka,
6 semen Abraham servi ejus; filii Jacob electi ejus.
inu zidzukulu za Abrahamu mtumiki wake, inu ana a Yakobo, osankhika ake.
7 Ipse Dominus Deus noster; in universa terra judicia ejus.
Iye ndiye Yehova Mulungu wathu; maweruzo ake ali pa dziko lonse lapansi.
8 Memor fuit in sæculum testamenti sui; verbi quod mandavit in mille generationes:
Iyeyo amakumbukira pangano lake kwamuyaya, mawu amene analamula kwa mibado yonse,
9 quod disposuit ad Abraham, et juramenti sui ad Isaac:
pangano limene Iye anapanga ndi Abrahamu, lumbiro limene analumbira kwa Isake.
10 et statuit illud Jacob in præceptum, et Israël in testamentum æternum,
Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga zophunzitsa, kwa Israeli monga pangano lamuyaya:
11 dicens: Tibi dabo terram Chanaan, funiculum hæreditatis vestræ:
“Ndidzapereka kwa iwe dziko la Kanaani ngati gawo la cholowa chako.”
12 cum essent numero brevi, paucissimi, et incolæ ejus.
Pamene iwo anali ngati anthu ochepa mʼchiwerengero, ochepa ndithu, ndiponso alendo mʼdzikolo,
13 Et pertransierunt de gente in gentem, et de regno ad populum alterum.
ankayendayenda kuchoka ku mtundu wina wa anthu ndi kupita ku mtundu wina, kuchoka mu ufumu wina kupita ku wina.
14 Non reliquit hominem nocere eis: et corripuit pro eis reges.
Iye sanalole wina aliyense kuwapondereza; anadzudzula mafumu chifukwa cha iwo:
15 Nolite tangere christos meos, et in prophetis meis nolite malignari.
“Musakhudze odzozedwa anga; musachitire choyipa aneneri anga.”
16 Et vocavit famem super terram, et omne firmamentum panis contrivit.
Iye anabweretsa njala pa dziko ndipo anawononga chakudya chonse;
17 Misit ante eos virum: in servum venundatus est, Joseph.
Iyeyo anatumiza munthu patsogolo pawo, Yosefe anagulitsidwa ngati kapolo.
18 Humiliaverunt in compedibus pedes ejus; ferrum pertransiit animam ejus:
Iwo anavulaza mapazi ake ndi matangadza, khosi lake analiyika mʼzitsulo,
19 donec veniret verbum ejus. Eloquium Domini inflammavit eum.
mpaka zimene Iye ananeneratu zitakwaniritsidwa, mpaka mawu a Yehova ataonetsa kuti Iye ananena zoona.
20 Misit rex, et solvit eum; princeps populorum, et dimisit eum.
Mfumu inatuma munthu kukamumasula, wolamulira wa mitundu ya anthu anamasula iyeyo.
21 Constituit eum dominum domus suæ, et principem omnis possessionis suæ:
Anamuyika kukhala wolamulira nyumba yake, wolamulira zonse zimene iye anali nazo,
22 ut erudiret principes ejus sicut semetipsum, et senes ejus prudentiam doceret.
kulangiza ana a mfumu monga ankafunira ndi kuphunzitsa nzeru akuluakulu.
23 Et intravit Israël in Ægyptum, et Jacob accola fuit in terra Cham.
Tsono Israeli analowa mu Igupto; Yakobo anakhala monga mlendo mʼdziko la Hamu.
24 Et auxit populum suum vehementer, et firmavit eum super inimicos ejus.
Yehova anachulukitsa anthu ake; ndipo anachititsa kuti akhale ochuluka kwambiri kuposa adani awo;
25 Convertit cor eorum, ut odirent populum ejus, et dolum facerent in servos ejus.
amene mitima yawo anayitembenuza kuti idane ndi anthu ake, kukonzera chiwembu atumiki ake.
26 Misit Moysen servum suum; Aaron quem elegit ipsum.
Yehova anatuma Mose mtumiki wake, ndi Aaroni amene Iye anamusankha.
27 Posuit in eis verba signorum suorum, et prodigiorum in terra Cham.
Iwo anachita zizindikiro zozizwitsa pakati pawo, zodabwitsa zake mʼdziko la Hamu.
28 Misit tenebras, et obscuravit; et non exacerbavit sermones suos.
Yehova anatumiza mdima nasandutsa dziko kuti likhale la mdima. Koma anthuwo anakaniratu mawu a Yehova.
29 Convertit aquas eorum in sanguinem, et occidit pisces eorum.
Yehova anasandutsa madzi awo kukhala magazi, kuchititsa kuti nsomba zawo zife.
30 Edidit terra eorum ranas in penetralibus regum ipsorum.
Dziko lawo linadzaza ndi achule amene analowa mʼzipinda zogona za olamulira awo.
31 Dixit, et venit cœnomyia et ciniphes in omnibus finibus eorum.
Iye anayankhula, ndipo kunabwera ntchentche zochuluka ndi nsabwe mʼdziko lawo lonse.
32 Posuit pluvias eorum grandinem: ignem comburentem in terra ipsorum.
Iyeyo anatembenuza mvula yawo kukhala matalala, ndi zingʼaningʼani mʼdziko lawo lonse;
33 Et percussit vineas eorum, et ficulneas eorum, et contrivit lignum finium eorum.
Anagwetsa mitengo yawo ya mpesa ndi mitengo yawo ya mkuyu, nawononganso mitengo ina ya mʼdziko lawolo.
34 Dixit, et venit locusta, et bruchus cujus non erat numerus:
Iye anayankhula, ndipo dzombe linabwera, ziwala zosawerengeka;
35 et comedit omne fœnum in terra eorum, et comedit omnem fructum terræ eorum.
zinadya chilichonse chobiriwira cha mʼdziko lawo, zinadya zonse zotuluka mʼnthaka yawo.
36 Et percussit omne primogenitum in terra eorum, primitias omnis laboris eorum.
Kenaka anakantha ana onse oyamba kubadwa a mʼdziko lawo, zipatso zoyamba za umunthu wawo wonse.
37 Et eduxit eos cum argento et auro, et non erat in tribubus eorum infirmus.
Yehova anatulutsa Israeli, atatenga siliva ndi golide wambiri, ndipo pakati pa mafuko awo palibe mmodzi amene anafowoka.
38 Lætata est Ægyptus in profectione eorum, quia incubuit timor eorum super eos.
Dziko la Igupto linakondwa pamene iwo anachoka, pakuti kuopsa kwa Israeli kunawagwera iwo.
39 Expandit nubem in protectionem eorum, et ignem ut luceret eis per noctem.
Iye anatambasula mitambo ngati chofunda chawo, ndi moto owawunikira usiku.
40 Petierunt, et venit coturnix, et pane cæli saturavit eos.
Iwo anapempha, ndipo Iye anawabweretsera zinziri ndipo anawakhutitsa ndi chakudya chochokera kumwamba.
41 Dirupit petram, et fluxerunt aquæ: abierunt in sicco flumina.
Iye anatsekula thanthwe, ndipo madzi anatuluka; ngati mtsinje anayenda mʼchipululu.
42 Quoniam memor fuit verbi sancti sui, quod habuit ad Abraham puerum suum.
Pakuti anakumbukira lonjezo lake loyera limene linaperekedwa kwa Abrahamu mtumiki wake.
43 Et eduxit populum suum in exsultatione, et electos suos in lætitia.
Iye anatulutsa anthu ake akukondwera, osankhika ake akufuwula mwachimwemwe;
44 Et dedit illis regiones gentium, et labores populorum possederunt:
Iye anawapatsa mayiko a anthu a mitundu ina ndipo anakhala olowamʼmalo a zimene ena anazivutikira,
45 ut custodiant justificationes ejus, et legem ejus requirant.]
kuti iwo asunge malangizo ake ndi kutsatira malamulo ake. Tamandani Yehova.

< Psalmorum 105 >