< Proverbiorum 17 >

1 [Melior est buccella sicca cum gaudio quam domus plena victimis cum jurgio.
Nʼkwabwino kudya mkute koma pali mtendere, kuposa kuchita madyerero mʼnyumba mʼmene muli mikangano.
2 Servus sapiens dominabitur filiis stultis, et inter fratres hæreditatem dividet.
Kapolo wanzeru adzalamulira mwana wochititsa manyazi, ndipo kapoloyo adzagawana nawo cholowa ngati mmodzi mwa abale.
3 Sicut igne probatur argentum et aurum camino, ita corda probat Dominus.
Siliva amamuyesa mʼngʼanjo ndipo golide amamuyesa mʼngʼanjo, koma Yehova amayesa mitima.
4 Malus obedit linguæ iniquæ, et fallax obtemperat labiis mendacibus.
Munthu woyipa amamvera malangizo oyipa; munthu wabodza amatchera khutu mawu osakaza.
5 Qui despicit pauperem exprobrat factori ejus, et qui ruina lætatur alterius non erit impunitus.
Iye amene amalalatira mʼmphawi amanyoza mlengi wake; amene amakondwerera tsoka la mnzake sadzakhala osalangidwa.
6 Corona senum filii filiorum, et gloria filiorum patres eorum.
Zidzukulu ndiye ulemu wa anthu okalamba, ndipo makolo ndiye ulemerero wa ana.
7 Non decent stultum verba composita, nec principem labium mentiens.
Kuyankhula bwino sikuyenerana ndi chitsiru, nanji kuyankhula bodza kungayenerane kodi ndi mfumu?
8 Gemma gratissima exspectatio præstolantis; quocumque se vertit, prudenter intelligit.
Chiphuphu chili ngati mankhwala amwayi kwa wochiperekayo; kulikonse kumene amapita zinthu zimamuyendera.
9 Qui celat delictum quærit amicitias; qui altero sermone repetit, separat fœderatos.
Iye amene amakhululukira zolakwa za wina, amafunitsitsa chikondi; wobwerezabwereza nkhani amapha chibwenzi.
10 Plus proficit correptio apud prudentem, quam centum plagæ apud stultum.
Munthu wanzeru amamva kamodzi kokha, munthu wopanda nzeru ndi samvamkunkhu.
11 Semper jurgia quærit malus: angelus autem crudelis mittetur contra eum.
Munthu woyipa maganizo ake ali pa kuwukira basi; ndipo bwana adzamutumizira wamthenga wankhanza.
12 Expedit magis ursæ occurrere raptis fœtibus, quam fatuo confidenti in stultitia sua.
Nʼkwabwino kukumana ndi chimbalangondo cholandidwa ana ake kusiyana ndi kukumana ndi chitsiru mu uchitsiru wake.
13 Qui reddit mala pro bonis, non recedet malum de domo ejus.
Ngati munthu abwezera choyipa kusinthana ndi zabwino, ndiye choyipa sichidzachoka mʼnyumba mwake.
14 Qui dimittit aquam caput est jurgiorum, et antequam patiatur contumeliam judicium deserit.]
Chiyambi cha mikangano chili ngati kukhamulira madzi, choncho uzichokapo mkangano usanayambe.
15 [Qui justificat impium, et qui condemnat justum, abominabilis est uterque apud Deum.
Kumasula munthu wolakwa kapena kumanga munthu wosalakwa, zonse ziwirizi Yehova zimamunyansa.
16 Quid prodest stulto habere divitias, cum sapientiam emere non possit? Qui altum facit domum suam quærit ruinam, et qui evitat discere incidet in mala.
Ndalama zogulira nzeru zili ndi phindu lanji mʼmanja mwa chitsiru poti iyeyo mutu wake sumayenda bwino?
17 Omni tempore diligit qui amicus est, et frater in angustiis comprobatur.
Bwenzi lako limakukonda nthawi zonse, ndipo mʼbale wako anabadwa kuti azikuthandiza pamavuto.
18 Stultus homo plaudet manibus, cum spoponderit pro amico suo.
Munthu wopanda nzeru amavomereza zopereka chikole ndipo iyeyo amasanduka chikole cha mnansi wake.
19 Qui meditatur discordias diligit rixas, et qui exaltat ostium quærit ruinam.
Wokonda zolakwa amakonda mkangano, ndipo wokonda kuyankhula zonyada amadziyitanira chiwonongeko.
20 Qui perversi cordis est non inveniet bonum, et qui vertit linguam incidet in malum.
Munthu wamtima woyipa zinthu sizimuyendera bwino; ndipo woyankhula zachinyengo amagwa mʼmavuto.
21 Natus est stultus in ignominiam suam; sed nec pater in fatuo lætabitur.
Mwana wopusa amamvetsa chisoni abambo ake, abambo a chitsiru sakhala ndi chimwemwe.
22 Animus gaudens ætatem floridam facit; spiritus tristis exsiccat ossa.
Mtima wosangalala uli ngati mankhwala abwino, koma mtima wokhumudwa umafowoketsa mafupa.
23 Munera de sinu impius accipit, ut pervertat semitas judicii.
Munthu woyipa amalandira chiphuphu chamseri kuti apotoze chiweruzo cholungama.
24 In facie prudentis lucet sapientia; oculi stultorum in finibus terræ.
Munthu wozindikira zinthu, maso ake amakhala pa nzeru, koma chitsiru chimwazamwaza maso ake pa dziko lonse lapansi.
25 Ira patris filius stultus, et dolor matris quæ genuit eum.
Mwana wopusa amamvetsa chisoni abambo ake ndipo amapweteketsa mtima amayi ake.
26 Non est bonum damnum inferre justo, nec percutere principem qui recta judicat.
Sibwino kulipitsa munthu wosalakwa, kapena kulanga anthu osalakwa.
27 Qui moderatur sermones suos doctus et prudens est, et pretiosi spiritus vir eruditus.
Munthu wosunga pakamwa ndiye wodziwa zinthu, ndipo wodekha mtima ndiye womvetsa bwino zinthu.
28 Stultus quoque, si tacuerit, sapiens reputabitur, et si compresserit labia sua, intelligens.]
Ngakhale chitsiru chimakhala ngati chanzeru chikakhala chete; ndipo chikatseka pakamwa chimakhala ngati munthu wochenjera.

< Proverbiorum 17 >