< Proverbiorum 10 >

1 [Filius sapiens lætificat patrem, filius vero stultus mœstitia est matris suæ.
Miyambo ya Solomoni: Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake, koma mwana wopusa amamvetsa amayi ake chisoni.
2 Nil proderunt thesauri impietatis, justitia vero liberabit a morte.
Chuma chochipeza mwachinyengo sichipindulitsa, koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.
3 Non affliget Dominus fame animam justi, et insidias impiorum subvertet.
Yehova salola kuti munthu wolungama azikhala ndi njala; koma amalepheretsa zokhumba za anthu oyipa.
4 Egestatem operata est manus remissa; manus autem fortium divitias parat. Qui nititur mendaciis, hic pascit ventos; idem autem ipse sequitur aves volantes.
Wochita zinthu mwaulesi amasauka, koma wogwira ntchito mwakhama amalemera.
5 Qui congregat in messe, filius sapiens est; qui autem stertit æstate, filius confusionis.
Amene amakolola nthawi yachilimwe ndi mwana wanzeru, koma amene amangogona nthawi yokolola ndi mwana wochititsa manyazi.
6 Benedictio Domini super caput justi; os autem impiorum operit iniquitas.
Madalitso amakhala pa mutu wa munthu wolungama, koma pakamwa pa munthu woyipa pamaphimba chiwawa.
7 Memoria justi cum laudibus, et nomen impiorum putrescet.
Munthu wolungama anzake adzamukumbukira ngati mdalitso, koma dzina la munthu woyipa lidzayiwalika.
8 Sapiens corde præcepta suscipit; stultus cæditur labiis.
Munthu wa mtima wanzeru amasamala malamulo, koma chitsiru chomangolongolola chidzawonongeka.
9 Qui ambulat simpliciter ambulat confidenter; qui autem depravat vias suas manifestus erit.
Munthu woyenda mwangwiro amayenda mosatekeseka; koma amene amayenda njira yokhotakhota adzadziwika.
10 Qui annuit oculo dabit dolorem; et stultus labiis verberabitur.]
Aliyense wotsinzinira maso mwachinyengo amabweretsa mavuto, koma wodzudzula chitsiru molimba mtima amabweretsa mtendere.
11 [Vena vitæ os justi, et os impiorum operit iniquitatem.
Pakamwa pa munthu wolungama ndi kasupe wamoyo, koma pakamwa pa munthu woyipa pamabisa chiwawa.
12 Odium suscitat rixas, et universa delicta operit caritas.
Udani umawutsa mikangano, koma chikondi chimaphimba zolakwa zonse.
13 In labiis sapientis invenitur sapientia, et virga in dorso ejus qui indiget corde.
Nzeru imapezeka pa milomo ya munthu wozindikira zinthu, koma pa msana pa munthu wopanda nzeru sipachoka chikwapu.
14 Sapientes abscondunt scientiam; os autem stulti confusioni proximum est.
Anzeru amasunga chidziwitso koma pakamwa pa chitsiru pamatulutsa zowononga.
15 Substantia divitis, urbs fortitudinis ejus; pavor pauperum egestas eorum.
Chuma cha munthu wolemera ndiye chitetezo chake; koma umphawi ndiye chiwonongeko cha osauka.
16 Opus justi ad vitam, fructus autem impii ad peccatum.
Moyo ndiye malipiro a munthu wolungama, koma phindu la anthu oyipa ndi uchimo ndi imfa.
17 Via vitæ custodienti disciplinam; qui autem increpationes relinquit, errat.
Wosamalira malangizo amayenda mʼnjira ya moyo, koma wonyoza chidzudzulo amasochera.
18 Abscondunt odium labia mendacia; qui profert contumeliam, insipiens est.
Amene amabisa chidani chake ndi munthu wonama, ndipo amene amafalitsa miseche ndi chitsiru.
19 In multiloquio non deerit peccatum, qui autem moderatur labia sua prudentissimus est.
Mawu akachuluka zolakwa sizisowa, koma amene amasunga pakamwa pake ndi wanzeru.
20 Argentum electum lingua justi; cor autem impiorum pro nihilo.
Mawu a munthu wolungama ali ngati siliva wabwino kwambiri, koma mtima wa munthu woyipa ndi wopanda phindu.
21 Labia justi erudiunt plurimos; qui autem indocti sunt in cordis egestate morientur.]
Milomo ya anthu olungama imalimbikitsa ambiri; koma chitsiru chimafa chifukwa chosowa nzeru.
22 [Benedictio Domini divites facit, nec sociabitur eis afflictio.
Mdalitso wa Yehova ndiwo umabweretsa chuma, ntchito za munthu siziwonjezerapo kanthu.
23 Quasi per risum stultus operatur scelus, sapientia autem est viro prudentia.
Kwa chitsiru kuchita zinthu zoyipa ndiye chinthu chomusangalatsa, koma kwa munthu womvetsa bwino zinthu nzeru ndiyo imamusangalatsa.
24 Quod timet impius veniet super eum; desiderium suum justus dabitur.
Chimene munthu woyipa amachiopa chidzamuchitikira; chimene munthu wolungama amachilakalaka adzachipeza.
25 Quasi tempestas transiens non erit impius; justus autem quasi fundamentum sempiternum.
Pamene namondwe wawomba, anthu oyipa amachotsedwa, koma anthu olungama amakhazikika mpaka muyaya.
26 Sicut acetum dentibus, et fumus oculis, sic piger his qui miserunt eum.
Momwe amakhalira vinyo wosasa mʼkamwa ndi momwe umakhalira utsi mʼmaso, ndi momwenso amakhalira munthu waulesi kwa amene amutuma.
27 Timor Domini apponet dies, et anni impiorum breviabuntur.
Kuopa Yehova kumatalikitsa moyo; koma zaka za anthu oyipa zidzafupikitsidwa.
28 Exspectatio justorum lætitia, spes autem impiorum peribit.
Chiyembekezo cha olungama chimapatsa chimwemwe, koma chiyembekezo cha anthu ochimwa chidzafera mʼmazira.
29 Fortitudo simplicis via Domini, et pavor his qui operantur malum.
Njira za Yehova ndi linga loteteza anthu ochita zabwino, koma wochita zoyipa adzawonongeka.
30 Justus in æternum non commovebitur, impii autem non habitabunt super terram.
Munthu wolungama sadzachotsedwa, pamalo pake koma oyipa sadzakhazikika pa dziko.
31 Os justi parturiet sapientiam; lingua pravorum peribit.
Pakamwa pa munthu wolungama pamatulutsa za nzeru, koma lilime lokhota lidzadulidwa.
32 Labia justi considerant placita, et os impiorum perversa.]
Milomo ya anthu olungama imadziwa zoyenera kuyankhula, koma pakamwa pa anthu ochimwa pamatulutsa zokhota zokhazokha.

< Proverbiorum 10 >