< Zephaniah 3 >

1 Acn Jerusalem ac musalla, sie siti olafohkfok ac tunyuna, su akkeokye mwet lal sifacna.
Tsoka kwa mzinda wa anthu opondereza, owukira ndi odetsedwa!
2 El tuh tia porongo LEUM GOD, ku insewowo in eis kas in kaiyuk lal. El tia filiya lulalfongi lal in LEUM GOD, ku suk kasru sel.
Sumvera aliyense, sulandira chidzudzulo. Sumadalira Yehova, suyandikira pafupi ndi Mulungu wake.
3 Mwet leum lun acn we elos oana lion ngutngut; mwet nununku we oana kosro wolf masrinsral su arulana rapku ac tia lela soko sri in oan nu ke lotu tok uh.
Akuluakulu ake ali ngati mikango yobuma, olamulira ake ndi olusa ngati mimbulu ya nthawi ya madzulo, zimene pofika mmawa sizisiya chilichonse.
4 Mwet palu elos tiana oru ma kunalos ac elos kutasrik; mwet tol elos akfohkfokyela ma mutal ac ikil ma sap lun God in wo nu selos sifacna.
Aneneri ake ndi odzikuza; anthu achinyengo. Ansembe ake amadetsa malo opatulika ndipo amaphwanya lamulo.
5 Tusruktu LEUM GOD El srakna oasr in siti uh; El oru ma suwohs ac tia ku in oru ma sufal. Lotutang nukewa El tia tui in oru nununku suwohs nu sin mwet lal. A ne ouinge, mwet sesuwos we srakna oru na ma koluk ac tia mwekin.
Yehova amene ali pakati pawo ndi wolungama; Iye salakwa. Tsiku ndi tsiku amaweruza molungama, ndipo tsiku lililonse salephera, komabe ochita zoyipa sachita manyazi nʼkomwe.
6 LEUM GOD El fahk, “Nga sukela mutunfacl puspis. Nga kunausla siti selos ac filiya pot ac tower ke siti inge in musalla na oan. Siti uh wanginla mwet we, inkanek uh oalalla — wangin mwet lula.
“Ndachotseratu mitundu ya anthu; ndagwetsa malinga awo. Ndipo sindinasiye ndi mmodzi yemwe mʼmisewu mwawo, popanda aliyense wodutsa. Mizinda yawo yawonongedwa; palibe aliyense adzatsalemo.
7 Nga tuh nunku mu ma inge ac tuh oru mwet luk in asmakla ac akfulatye kaiyuk luk, ac tia mulkunla mwe luti luk nu selos. A tia paht na elos sifil oru koluk oana meet ah.
Ndinati, ‘Ndithudi, anthu a mu mzindawu adzandiopa ndi kumvera kudzudzula kwanga!’ Ndipo sindidzawononga nyumba zawo, kapena kuwalanganso. Koma iwo anali okonzeka kuchita mwachinyengo zinthu zonse zimene amachita.
8 Ac LEUM GOD El fahk, “Soano na. Tupan len se nga ac tuyak ac orek loh lain mutunfacl uh. Nga wulela tari tuh nga fah orani mutunfacl ac tokosrai, ac oru elos in pula ku lun kasrkusrak luk. Faclu nufon ac fah kunausyukla ke kasrkusrak luk, su oana sie firir in e.
Choncho mundidikire,” akutero Yehova, “chifukwa cha tsiku limene ndidzaperekera umboni. Ndatsimikiza kusonkhanitsa pamodzi mitundu ya anthu, kusonkhanitsa maufumu ndi kutsanulira ukali wanga pa iwo; mkwiyo wanga wonse woopsa. Dziko lonse lidzatenthedwa ndi moto wa mkwiyo wa nsanje yanga.
9 “Na nga fah ekulla ouiyen kaskas lun mwet in mutunfacl nukewa, ac elos fah pre nu sik mukena, ac tia nu sin kutena god saya. Elos nukewa fah akosyu.
“Pamenepo ndidzayeretsa milomo ya anthu a mitundu yonse kuti anthu onsewo ayitane dzina la Yehova ndi kumutumikira Iye pamodzi.
10 Finne acn Ethiopia su oan loeslana, mwet luk su fahsrelik elos ac fah use mwe kisa nu sik we me.
Kuchokera kutsidya kwa mitsinje ya ku Kusi anthu anga ondipembedza, omwazikana, adzandibweretsera zopereka.
11 In pacl sac, kowos mwet luk fah tia sifilpa enenu in mwekin lah kowos tuh tuyak lainyu. Nga fah lusla mwet nukewa su filang ac inse fulat, ac kowos fah tia sifilpa tunyuna lainyu fin eol mutal sik.
Tsiku limenelo simudzachita manyazi chifukwa cha zoyipa zonse munandichitira, popeza ndidzachotsa onse mu mzinda uwu amene amakondwera chifukwa cha kunyada kwawo. Simudzakhalanso odzikuza mʼphiri langa lopatulika.
12 Nga fah oakiya sie mutunfacl pusisel ac efal in acn we, su fah tuku ac sukok kasru sik.
Koma ndidzasiya pakati panu anthu ofatsa ndi odzichepetsa, amene amadalira dzina la Yehova.
13 Mwet Israel su lula ac fah tia oru kutena ouiya koluk nu sin kutena mwet, ku fahk kas kikiap, ku srike in aklalfonye mwet. Elos fah kapkapak ac muta in misla, ac tia sangeng sin kutena mwet.”
Aisraeli otsala sadzachitanso zolakwika; sadzayankhulanso zonama, ngakhale chinyengo sichidzatuluka mʼkamwa mwawo. Adzadya ndi kugona ndipo palibe amene adzawachititse mantha.”
14 On ac sasa ke engan, kowos mwet Israel! Jerusalem, engan ke insiom nufon!
Imba, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni; fuwula mokweza, iwe Israeli! Sangalala ndi kukondwera ndi mtima wako wonse, iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu!
15 LEUM GOD El tulokinya kaiyuk lal nu sum. El lusak mwet lokoalok lom nukewa. LEUM GOD, su tokosra lun Israel, El wi kom. Inge kowos tia enenu in sifilpa sangeng.
Yehova wachotsa chilango chako, wabweza mdani wako. Yehova, Mfumu ya Israeli, ali pakati pako; sudzaopanso chilichonse.
16 Pacl se apkuran me ke elos fah fahk nu sin Jerusalem, “Nikmet sangeng, siti Zion! Nikmet lela poum in munasla!
Pa tsiku limenelo adzanena kwa Yerusalemu kuti, “Usaope, iwe Ziyoni; usafowoke.
17 LEUM GOD lom El wi kom; Ku lal ac fah sot kutangla nu sum. LEUM GOD El fah enganak keim, Ac ke lungse yohk lal El fah sot nu sum sie moul sasu. El fah on ac arulana engan keim,
Yehova Mulungu wako ali pakati pako, ali ndi mphamvu yopulumutsa. Adzakondwera kwambiri mwa iwe, adzakukhalitsa chete ndi chikondi chake, adzayimba mokondwera chifukwa cha iwe.”
18 Aok, oana engan lun mwet uh ke pacl in kufwa.” LEUM GOD El fahk, “Nga aksafyela tari mwe aksangeng lun ongoiya Ac eisla mwe mwekin lom.
“Ndidzakuchotserani zowawa za pa zikondwerero zoyikika; nʼzolemetsa ndi zochititsa manyazi.
19 Pacl se apkuranme! Nga fah akkeokye mwet ma akkolukye kom; Nga fah molela mwet ul nukewa Ac folokonma mwet sruoh nu yen selos. Nga fah ekulla mwekin lalos nu ke akfulat, Ac faclu nufon fah kaksakunulos.
Taonani, nthawi imeneyo ndidzathana ndi onse amene anakuponderezani; ndidzapulumutsa olumala ndi kusonkhanitsa amene anamwazika. Ndidzawayamikira ndi kuwachitira ulemu mʼdziko lililonse mmene anachititsidwa manyazi.
20 Pacl se apkuranme! Nga fah oru tuh mwet lom nukewa su fahsrelik in folokeni nu yen selos. Nga fah oru kom in pwengpeng fin faclu nufon Ac sifilpa akkasrupye kom.” LEUM GOD El fahk ouinge.
Pa nthawi imeneyo ndidzakusonkhanitsani; pa nthawi imeneyo ndidzakubweretsani ku mudzi kwanu. Ndidzakuyamikirani ndi kukuchitirani ulemu pakati pa mitundu ya anthu a dziko lapansi pamene ndidzabwezeretsa mtendere wanu inu mukuona,” akutero Yehova.

< Zephaniah 3 >