< Zechariah 1 >

1 In malem se akoalkosr ke yac se akluo in pacl Darius el Tokosra Fulat lun Persia, LEUM GOD El sang kas inge nu sel mwet palu Zechariah, su wen natul Berechiah, su ma natul Iddo.
Mwezi wachisanu ndi chitatu, mʼchaka chachiwiri cha ulamuliro wa Dariyo, Yehova anayankhula ndi mneneri Zekariya mwana wa Berekiya, mwana wa Ido, kuti:
2 LEUM GOD Kulana El fahkang nu sel Zechariah in fahk nu sin mwet uh, “Nga, LEUM GOD, tuh arulana kasrkusrak sin mwet matu lowos,
“Yehova anakwiya kwambiri ndi makolo anu.
3 tusruktu inge nga fahk nu suwos, ‘Kowos foloko nu yuruk, ac nga fah folokot nu yuruwos.
Choncho awuze anthuwa kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Bwererani kwa Ine,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse. ‘Ndipo Ine ndidzabwerera kwa inu,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
4 Nimet kowos oana mwet matu lowos. In pacl loes somla, mwet palu elos tuh fahkak kas luk nu selos, ac fahk mu elos in tia sifil moulkin moul koluk, ac tia sifil oru ma koluk.’ A elos tiana porongeyu ku akosyu.
Musakhale ngati makolo anu, amene aneneri akale anawalalikira kuti: Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Tsopano lekani njira zanu zoyipa ndi machitidwe anu oyipawo.’ Koma iwo sanamvere kapena kulabadira za Ine, akutero Yehova.
5 Mwet matu lowos ac mwet palu ingo elos wanginla.
Kodi makolo anuwo ali kuti tsopano? Nanga aneneri, kodi amakhalapo mpaka muyaya?
6 Nga tuh sang sap luk nu sin mwet kulansap luk, mwet palu, kas in akesmakyalos, tusruktu elos tiana lohang nu kac, oru elos tuh keokkin seakos lalos. Na elos auliyak ac fahkak lah elos akilen lah nga, LEUM GOD Kulana, tuh kalyaelos fal nu ke ouiyalos, oana ke nga sulela in oru.”
Kodi mawu anga ndi malangizo anga, amene ndinawawuza atumiki anga aneneri, suja anawachitira makolo anu? “Tsono iwo analapa ndi kunena kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse watichitira zomwe zikuyenera njira zathu ndi machitidwe athu, monga anatsimikiza kuti adzachita.’”
7 In yac se akluo lal Tokosra Fulat Darius, ke len aklongoul akosr in malem se aksingoul sie (malem in Shebat), LEUM GOD El ikasla nu sik sie mwe fahkak in sie aruruma ke fong.
Tsiku la 24 la mwezi wa 11, mwezi wa Sebati, chaka chachiwiri cha ulamuliro wa Dariyo, Yehova anayankhula ndi Zekariya mwana wa Berekiya, mwana wa Ido.
8 Nga tuh liye mwet se kasrusr fin soko horse srusra. El tui inmasrlon sak myrtle infahlfal se, ac oasr pac kutu horse tokol — kutu srusra, kutu tuhntun, ac kutu fasrfasr.
Nthawi ya usiku ndinaona masomphenya. Ndinaona munthu atakwera pa kavalo wofiira. Iye anayima pakati pa mitengo ya mchisu mʼchigwa. Kumbuyo kwake kunali akavalo ofiira, akhofi ndi oyera.
9 Na nga siyuk sel, “Leum se, mea kalmen horse ingan?” Na lipufan se ma kaskas nu sik ah topuk ac fahk, “Nga fah akkalemye nu sum lah mea kalmac.
Ine ndinafunsa kuti, “Mbuye wanga, kodi zimenezi ndi chiyani?” Mngelo amene amayankhula nane anayankha kuti, “Ndidzakuonetsa kuti zimenezi ndi chiyani.”
10 LEUM GOD El sap elos in som ac tuni lah mea orek faclu.”
Pamenepo munthu amene anayima pakati pa mitengo ya mchisu anafotokoza kuti, “Amenewa ndiwo amene Yehova wawatuma kuti ayendere dziko lonse lapansi.”
11 Na elos tuh fahk nu sin lipufan sac, “Kut foroht forma fin faclu nufon ac konauk tuh na faclu arulana wanginla ku la, ac misla na.”
Ndipo okwera pa akavalo enawo anafotokoza kwa mngelo wa Yehova, amene anayima pakati pa mitengo ya mchisu kuti, “Ife tayendera dziko lonse lapansi ndipo tapeza kuti dziko lonselo lili pa bata ndi mtendere.”
12 Na lipufan sac fahk, “LEUM GOD Kulana, kom tuh kasrkusrak sin Jerusalem ac sin siti nukewa lun Judah ke yac itngoulla. Ac putaka lula na kom fah akkalemye pakomuta lom nu selos?”
Tsono mngelo wa Yehova anati, “Yehova Wamphamvuzonse, kodi mpaka liti mudzakhala osaonetsa chifundo chanu kwa Yerusalemu ndi mizinda ya Yuda, amene mwawakwiyira kwa zaka izi 70?”
13 LEUM GOD El topuk lipufan sac ke kas in akwoye,
Choncho Yehova anayankhula mawu abwino ndi achitonthozo kwa mngelo amene ankayankhula nane.
14 ac lipufan sac fahk nu sik nga in sulkakin kas ma LEUM GOD El fahk inge: “Nga arulana nunku yohk ke Jerusalem, siti mutal luk,
Pamenepo mngelo amene ankayankhula nane anati, “Lengeza mawu awa: Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Ine ndikuchitira nsanje Yerusalemu ndi Ziyoni,
15 ac nga kasrkusrak sin mutunfacl su okak ac mutana in misla, mweyen ke pacl se ma nga srusruok mulat luk sin mwet luk, mutunfacl ingan tuh akyokye keok nu sin mwet luk upa liki meet ah.
koma ndakwiya kwambiri ndi anthu a mitundu ina amene akuganiza kuti ali pa mtendere. Ndinakwiyira anthu anga pangʼono pokha, koma iwo anawonjeza kuzunza anthu angawo.’
16 Na pa nga foloko nu Jerusalem in tuh akkalemye pakomuta luk nu ke siti sac. Tempul luk ac fah folokyak, ac siti uh ac fah sifil musaiyukla.”
“Choncho, Yehova akuti, ‘Ndidzabwerera ku Yerusalemu ndi mtima wachifundo, nyumba yanga adzayimanganso kumeneko. Ndipo adzatenganso chingwe choyezera kuti amange Yerusalemu,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
17 Lipufan sac fahk pac nu sik in sulkakin kas inge: “LEUM GOD Kulana El fahk mu siti nukewa lal ac fah sifilpa akkasrupyeyuk, ac El fah sifilpa eisla Jerusalem tuh in ma lal sifacna.”
“Lengezanso kuti, Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Mizinda yanga idzakhalanso ndi zokoma zosefukira ndipo Yehova adzatonthoza Ziyoni ndi kusankhanso Yerusalemu.’”
18 In sie pac aruruma nga liye koen cow akosr.
Kenaka ndinayangʼananso, ndipo patsogolo panga panali nyanga zinayi.
19 Na nga siyuk sin lipufan se ma kaskas nu sik ah, “Mea kalmen koac inge?” El topuk ac fahk, “Elos akkalemye ku lulap lun faclu ma akfahsryelik mwet Judah, mwet Israel, ac mwet Jerusalem.”
Ndinamufunsa mngelo amene amayankhula nane kuti, “Kodi zimenezi ndi chiyani?” Iye anandiyankha kuti, “Izi ndi nyanga zimene zinabalalitsa Yuda, Israeli ndi Yerusalemu.”
20 Na LEUM GOD El ikasla nu sik ac nga liye mwet orekma akosr utuk hammer.
Kenaka Yehova anandionetsa amisiri azitsulo anayi.
21 Ac nga siyuk, “Mea mwet inge tuku in oru uh?” El topuk ac fahk, “Elos tuku in aksangengye ac kunausla mutunfacl nukewa su tuh arulana itungya acn Judah ac akfahsryelik mwet we.”
Ndinafunsa kuti, “Amisiri a zitsulowa akudzachita chiyani?” Iye anayankha kuti, “Izi ndi nyanga zimene zinabalalitsa Yuda kotero kuti panalibe wina amene akanalimbana nazo, koma amisiri a zitsulowa abwera kudzaziopseza ndi kugwetsa nyanga zimenezi za mitundu ya anthu amene analimbana ndi dziko la Yuda ndi kubalalitsa anthu ake.”

< Zechariah 1 >