< Psalm 68 >

1 [Psalm lal David] God El tuyak ac akfahsryelik mwet lokoalok lal. Elos su srungal elos kutangyukla ac kaingelik.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Adzuke Mulungu, adani ake amwazikane; adani ake athawe pamaso pake.
2 Oana ke kulasr uh ukukla, ouinge God El luselosla. Oapana ke wax uh kofelik ke e uh, Ouinge mwet koluk elos wanginla ye mutun God.
Monga momwe mphepo imachotsera utsi; Inu muwawulutsire kutali. Monga phula limasungunukira pa moto, oyipa awonongeke pamaso pa Mulungu.
3 A mwet suwoswos elos insewowo ac engan ye mutal; Elos insewowo ac sasa ke engan.
Koma olungama asangalale ndi kukondwera pamaso pa Mulungu; iwo akondwere ndi kusangalala.
4 On nu sin God, yuk on in kaksak nu sel; Kowos srukak pusren on ac akfulatye El su kasrusr fin pukunyeng uh! Inel pa LEUM GOD— kowos in engan ye mutal!
Imbirani Mulungu imbirani dzina lake matamando, mukwezeni Iye amene amakwera pa mitambo; dzina lake ndi Yehova ndipo sangalalani pamaso pake.
5 God, su muta in Tempul mutal sel, El nunku ke tulik mukaimtal, ac El karinganang katinmas.
Atate wa ana amasiye, mtetezi wa akazi amasiye, ndiye Mulungu amene amakhala mʼmalo oyera.
6 El sang acn in muta lun mwet mukaimtal, Ac el kolla mwet kapir nu ke sukosok ac engan, A elos su lainul fah muta ke acn na turangangla.
Mulungu amakhazikitsa mtima pansi osungulumwa mʼmabanja, amatsogolera amʼndende ndi kuyimba; koma anthu osamvera amakhala ku malo owuma a dziko lapansi.
7 O God, ke kom tuh kol mwet lom, Ac fahsr sasla yen mwesis,
Pamene munatuluka kutsogolera anthu anu, Inu Mulungu, pamene munayenda kudutsa chipululu,
8 Faclu kusrusrsrusr, ac af kahkla inkusrao me Ke sripen tuku lun God lun Sinai, Su God lun Israel.
dziko lapansi linagwedezeka, miyamba inakhuthula pansi mvula, pamaso pa Mulungu, Mmodzi uja wa ku Sinai. Pamaso pa Mulungu, Mulungu wa Israeli.
9 Kom oru tuh af matol in putat nu faclu Ac aksroksrokyauk acn su munaslana.
Munapereka mivumbi yochuluka, Inu Mulungu; munatsitsimutsa cholowa chanu cholefuka.
10 Mwet lom elos orala acn in muta lalos ingo; Ke pakoten lom, kom sang mwe kasru nu sin mwet sukasrup.
Anthu anu anakhala mʼmenemo ndipo munapatsa anthu osauka zimene zinkawasowa chifukwa cha ubwino wanu Mulungu.
11 Leum El oru sap lal, Ac mutan puspis elos usalik pweng se inge:
Ambuye analengeza mawu, ndipo gulu linali lalikulu la iwo amene anapita kukawafalitsa;
12 “Tokosra uh wi mwet mweun lalos elos kaingelik!” Na mutan su mutana acn selos elos kitalik ma wap inge:
“Mafumu ndi ankhondo anathawa mwaliwiro; mʼmisasa anthu anagawana zolanda pa nkhondo.
13 Luman wule uh ma afla ke silver, Ac posohksok lalos saromrom ke gold nasnas. (Efu ku kutu suwos muta in kalkal lun sheep uh ke len in mweun?)
Ngakhale mukugona pakati pa makola a ziweto, mapiko a nkhunda akutidwa ndi siliva, nthenga zake ndi golide wonyezimira.”
14 Ke God Kulana El akfahsryelik tokosra uh Fineol Zalmon, El oru tuh snow in putat we.
Pamene Wamphamvuzonse anabalalitsa mafumu mʼdziko, zinali ngati matalala akugwa pa Zalimoni.
15 Fuka kuiyen Fineol Bashan, Soko eol su pukanten tohktok fac!
Mapiri a Basani ndi mapiri aulemerero; mapiri a Basani, ndi mapiri a msonga zambiri.
16 Efu ku kowos ngetnget koluk liki tohktok fulat kowos muta we Nu ke eol soko su God El sulela tuh Elan muta we? LEUM GOD El ac fah muta we ma pahtpat!
Muyangʼaniranji mwansanje inu mapiri a msonga zambiri, pa phiri limene Mulungu analisankha kuti azilamulira, kumene Yehova mwini adzakhalako kwamuyaya?
17 Ke tausin chariot fokoko natul, Leum El tuku Sinai me nu in acn mutal sel.
Magaleta a Mulungu ndi osawerengeka, ndi miyandamiyanda; Ambuye wabwera kuchokera ku Sinai, walowa mʼmalo ake opatulika.
18 El utyak nu yen fulat Ac us mwet sruoh puspis welul; El eis mwe sang sin mwet su lainul. LEUM GOD El ac fah muta ingo.
Pamene Inu munakwera mmwamba, munatsogolera a mʼndende ambiri; munalandira mphatso kuchokera kwa anthu, ngakhale kuchokera kwa owukira, kuti Inu Mulungu, mukhale kumeneko.
19 Kaksakin Leum, Su us ma toasr lasr len na len; El pa God su molikutla.
Matamando akhale kwa Ambuye, kwa Mulungu Mpulumutsi wathu amene tsiku ndi tsiku amasenza zolemetsa zathu.
20 God lasr, El God su molela; El pa LEUM GOD, Leum lasr, Su loangekut liki misa.
Mulungu wathu ndi Mulungu amene amapulumutsa; Ambuye Wamphamvuzonse ndiye amene amatipulumutsa ku imfa.
21 Pwayena lah God El ac fah fukulya sifen mwet lokoalok lal, Elos su suk na in mutana in ma koluk lalos.
Ndithu Mulungu adzaphwanya mitu ya adani ake, zipewa za ubweya za iwo amene amapitiriza kuchita machimo awo.
22 Leum El fahk, “Nga ac fah folokonma mwet lokoalok lowos liki Bashan, Nga fah folokunulosma liki acn loal meoa,
Ambuye akunena kuti, “Ndidzawabweretsa kuchokera ku Basani; ndidzawabweretsa kuchokera ku nyanja zozama.
23 Tuh kowos fah fahsr in srah kaclos, Ac kosro ngalngul nutuwos in lohi srah kaclos nwe kena elos muti.”
Kuti muviyike mapazi anu mʼmagazi a adani anu, pamene malilime a agalu anu akudyapo gawo lawo.”
24 O God, mwet nukewa elos liye fahsr in kutangla lom, Aok utyak lun God, Tokosra luk, nu in acn mutal sel.
Mayendedwe aulemu a anthu anu aonekera poyera, Inu Mulungu; mayendedwe olemekeza Mulungu wanga ndi Mfumu yanga yokalowa mʼmalo opatulika.
25 Mwet on elos fahsr meet, ac mwet srital ke mwe on elos fahsr tok, Ac mutan fusr elos fahsr infulwa ac srital ke tambourine natulos.
Patsogolo pali oyimba nyimbo pakamwa, pambuyo pawo oyimba nyimbo ndi zipangizo; pamodzi ndi iwo pali atsikana akuyimba matambolini.
26 “Kaksakin God in walil lulap lun mwet lal. Kaksakin LEUM GOD, kowos fwil natul Jacob!”
Tamandani Mulungu mu msonkhano waukulu; tamandani Yehova mu msonkhano wa Israeli.
27 Benjamin, sruf se ma srik emeet, elan fahsr meet; Toko, mwet kol lun Judah wi mwet lalos, Na tufah mwet kol lun Zebulun ac Naphtali.
Pali fuko lalingʼono la Benjamini, kuwatsogolera, pali gulu lalikulu la ana a mafumu a Yuda, ndiponso pali ana a mafumu a Zebuloni ndi Nafutali.
28 Akkalemye ku lom, O God; Ku se su kom orekmakin kacsr
Kungani mphamvu zanu Mulungu; tionetseni nyonga zanu, Inu Mulungu, monga munachitira poyamba.
29 Liki Tempul lom in Jerusalem, Yen tokosra uh elos use mwe lung nu sum we.
Chifukwa cha Nyumba yanu ku Yerusalemu, mafumu adzabweretsa kwa Inu mphatso.
30 Kael Egypt, su oana kosro lemnak su muta inmasrlon loa uh; Kai mutunfacl uh, su oana un cow mukul wi cow fusr, Nwe ke na elos nukewa suwoli ac asot silver lalos nu sum. Akfahsryeloselik su lungse orek mweun!
Dzudzulani chirombo pakati pa mabango, gulu la ngʼombe zazimuna pakati pa ana angʼombe a mitundu ya anthu. Mochititsidwa manyazi, abweretse mitanda ya siliva. Balalitsani anthu a mitundu ina amene amasangalatsidwa ndi nkhondo.
31 Mwet fulat aolyen facl Egypt fah tuku; Ac mwet Ethiopia elos ac fah asroeak paolos in pre nu sin God.
Nthumwi zidzachokera ku Igupto; Kusi adzadzipereka yekha kwa Mulungu.
32 On nu sin God, tokosrai lun faclu, Onkin on in kaksak nu sin Leum,
Imbirani Mulungu Inu mafumu a dziko lapansi imbirani Ambuye matamando. (Sela)
33 Nu sel su kasrusr inkusrao — Kusrao su oan oemeet me. Porongo, el sala ke sie pusra ku.
Kwa Iye amene amakwera pa mitambo yakalekale ya mmwamba amene amabangula ndi mawu amphamvu.
34 Kowos fahkak ku lun God; Tuh fulat lal oan fin Israel, Ac ku lal oan inkusrao.
Lengezani za mphamvu za Mulungu, amene ulemerero wake uli pa Israeli amene mphamvu zake zili mʼmitambo.
35 Arulana yohk mangoliyen God ke El ac illa liki acn mutal sel — God lun Israel! El sang ku wolana nu sin mwet lal. Kaksakin God!
Ndinu woopsa, Inu Mulungu mʼmalo anu opatulika; Mulungu wa Israeli amapereka mphamvu ndi nyonga kwa anthu ake. Matamando akhale kwa Mulungu!

< Psalm 68 >