< Psalm 65 >

1 [Psalm lal David] O God, fal kut in kaksakin kom in Zion Ac karingin wulela lasr nu sum,
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Nyimbo. Matamando akudikira Inu Mulungu mu Ziyoni; kwa inu malumbiro athu adzakwaniritsidwa.
2 Mweyen kom topuk pre. Mwet in acn nukewa ac fah tuku nu yurum
Inu amene mumamva pemphero, kwa inu anthu onse adzafika.
3 Ke sripen ma koluk lalos. Ma sutuu lasr uh kutangkutla, Tusruktu kom nunak munas nu sesr kac.
Pamene tinathedwa nzeru ndi machimo, Inu munakhululukira mphulupulu zathu.
4 Insewowo elos su kom sulela, Su kom use in muta in acn mutal sum. Kut ac fah insewowokin ma wo su oan in lohm sum, Oayapa ke mwe insewowo in Tempul mutal lom.
Odala iwo amene inu muwasankha ndi kuwabweretsa pafupi kukhala mʼmabwalo anu! Ife tadzazidwa ndi zinthu zabwino za mʼNyumba mwanu, za mʼNyumba yanu yoyera.
5 Kom topuk kut ke kom ase kutangla nu sesr, Ac kom oru pac ma wolana in molikutla. Mwet fin faclu nufon, Ac yen loeslana in meoa, elos wi pac lulalfongi in kom.
Mumatiyankha ife ndi ntchito zodabwitsa zachilungamo, Inu Mulungu Mpulumutsi wathu, chiyembekezo cha mathero onse a dziko lapansi ndi cha nyanja zomwe zili kutali kwambiri,
6 Kom oakiya eol uh ke ku lom, Su mwe akkalemye ku lulap lom.
amene munapanga mapiri ndi mphamvu zanu, mutadziveka nokha ndi mphamvu.
7 Kom akmisye ngirngir in meoa uh Ac pusren noa uh; Kom akmisye pac fohsak lulap lun mwet uh.
Amene munakhalitsa bata nyanja kukokoma kwa mafunde ake, ndi phokoso la anthu a mitundu ina.
8 Faclu nufon fwefela in liye Ma usrnguk su kom oru. Orekma lom oru tuh mutanfahl nukewa In sasa ke engan, liki acn kutulap na nwe roto.
Iwo amene akukhala kutali amaopa zizindikiro zozizwitsa zanu; kumene dzuwa limatulukira ndi kumene dzuwa limalowera. Inu mumafuna nyimbo zachimwemwe.
9 Kom supwama af nu faclu in akkalemye lah kom karingin acn uh. Kom akkasrupye fokin acn uh in isus fahko wo. Kom nwakla infacl uh ke kof, Ac kom sang tuh in oasr fokin acn uh. Pa inge oreya sum:
Inu mumasamalira dziko lapansi ndi kulithirira; Inuyo mumalilemeretsa kwambiri. Mtsinje wa Mulungu ndi wodzaza ndi madzi kuti upereke tirigu kwa anthu, pakuti Inu munakhazikitsa zimenezi.
10 Kom supwama af na matol nu in imae Ac sroksrokunak infohk uh; Kom akfisrasrye fohk uh ke af srisrik, Ac oru tuh sacn srisrik in kapak.
Mwadzaza nthaka yake ndi madzi ndi kusalaza migula yake, mwayifewetsa ndi mvula yamawawa ndi kudalitsa mbewu zake.
11 Fuka kasrupiyen kosrani lulap su kom oru inge! Acn nukewa kom som nu we, pukanten ma we.
Inu mumaveka chaka ndi zinthu zochuluka, ndipo ngolo zanu zimasefukira ndi zinthu zochuluka.
12 Inimae nwanala ke un kosro; Ac pe eol uh sessesla ke engan.
Malo a udzu a mʼchipululu amasefukira; mapiri avekedwa ndi chisangalalo.
13 Inimae nwanala ke sheep; Ac infahlfal uh sessesla ke wheat. Ma inge nukewa on ac sasa ke engan.
Madambo akutidwa ndi zoweta ndi zigwa zavekedwa ndi tirigu; izo pamodzi zikufuwula ndi kuyimba mwachimwemwe.

< Psalm 65 >