< Psalm 61 >

1 [Psalm lal David] Lohng tung luk, O God; Porongo pre luk!
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Loyimbidwa ndi zipangizo za zingwe. Imvani kulira kwanga, Inu Mulungu; mvetserani pemphero langa.
2 Nga pang nu sum Ke nga muta loesla liki acn sik ac nga fuhleak finsrak luk. Usyu nu ke sie acn in molela,
Kuchokera ku malekezero a dziko lapansi ine ndimayitana Inu ndimayitana pomwe mtima wanga ukufowoka; tsogolereni ku thanthwe lalitali kuposa ineyo.
3 Tuh kom nien wikla luk, Ac mwet kasru ku luk in lain mwet lokoalok luk.
Pakuti Inu mwakhala pothawirapo panga, nsanja yolimba polimbana ndi adani anga.
4 Lela nga in muta in lohm mutal sum in moul luk nufon; Lela nga in konauk nien molela luk ye lulin poum.
Ine ndikulakalaka kukhala mʼtenti yanu kwamuyaya ndi kupeza chitetezo mu mthunzi wa mapiko anu.
5 Tuh kom lohng wulela luk, O God, Ac kom ase nu sik mwe usru lun mwet su sunakin kom.
Pakuti Inu Mulungu mwamva malumbiro anga; mwandipatsa cholowa cha iwo amene amaopa dzina lanu.
6 Akloesye moul lun tokosra; Lela tuh elan moul paht!
Wonjezerani masiku a moyo wa mfumu, zaka zake kwa mibado yochuluka.
7 Lela tuh elan leum ma pahtpat ye motom, O God; Karinganul ke lungse kawil ac oaru lom.
Iye akhale pa mpando waufumu pamaso pa Mulungu kwamuyaya; ikani chikondi chanu ndi kukhulupirika kwanu kuti zimuteteze.
8 Ke ma inge nga fah on ac kaksakin kom pacl e nukewa, Oana ke nga oru mwe kisa luk nu sum len nukewa, fal nu ke wulela luk.
Kotero ndidzayimba matamando kwamuyaya pa dzina lanu ndi kukwaniritsa malumbiro anga tsiku ndi tsiku.

< Psalm 61 >