< Psalm 54 >

1 [Psalm lal David tukun mwet tuku Ziph me nu yorol Saul a fahk nu sel la David el wikwik oan in acn selos.] O God, moliyula ke ku lom; Aksukosokyeyu ke ku lulap lom!
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Ndakatulo ya Davide. Pamene anthu a ku Zifi anapita kwa Sauli ndipo anati, “Kodi Davide sakubisala pakati pathu.” Pulumutseni Inu Mulungu, mwa dzina lanu; onetsani kuti ndine wosalakwa mwamphamvu yanu.
2 Lohng pre luk, O God; Porongo kas luk.
Imvani pemphero langa, Inu Mulungu mvetserani mawu a pakamwa panga.
3 Mwet inse fulat elos tuku in lainyu, Ac mwet sulallal elos srike in uniyuwi — Mwet su tia akfulatye God.
Alendo akundithira nkhondo; anthu ankhanza akufunafuna moyo wanga, anthu amene salabadira za Mulungu.
4 Tusruk God El mwet kasru luk. Leum El mwe loango luk.
Zoonadi Mulungu ndi thandizo langa; Ambuye ndiye amene amandichirikiza ine.
5 Lela tuh God Elan lain mwet lokoalok luk ke ma koluk lalos sifacna. El ac fah kunauselosla mweyen El oaru.
Lolani kuti choyipa chifike pa iwo amene amandichita chipongwe; mwa kukhulupirika kwanu awonongeni.
6 Nga ac fah engan in oru mwe kisa nu sum, O LEUM GOD; Nga fah sot kulo nu sum Mweyen kom wo.
Ine ndidzapereka nsembe yaufulu kwa Inu; ndidzatamanda dzina lanu, Inu Yehova, pakuti ndi labwino.
7 Tuh kom moliyula liki ongoiya luk nukewa, Ac nga liye ke mwet lokoalok luk elos kutangyukla.
Pakuti Iyeyo wandipulumutsa ku masautso anga onse, ndipo maso anga apenya kupambana kwa pa adani anga.

< Psalm 54 >