< Psalm 44 >

1 [Psalm lun Tulik natul Korah] O God, kut tuh lohng ke insresr sifacna Ma mwet matu lasr elos fahk nu sesr Ke orekma yohk su kom oru nu selos in pacl lalos Ke pacl loeloes somla:
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora. Ife tamva ndi makutu athu, Inu Mulungu; makolo athu atiwuza zimene munachita mʼmasiku awo, masiku akalekalewo.
2 Ke kom sifacna lusla mwet koluk liki facl selos Ac oakiya mwet lom in acn selos; Ac ke kom kai pac mutunfacl saya Ac oru tuh mutunfacl lom in kapkapak.
Ndi dzanja lanu munathamangitsa mitundu ya anthu ena ndi kudzala makolo athu; Inu munakantha mitundu ya anthu, koma makolo athuwo Inu munawapatsa ufulu.
3 Mwet lom elos tia sruokya acn inge ke cutlass natulos, Elos tia kutangla ke ku lalos sifacna, A ke ku lulap lom, Ac ke kom welulos. Ma inge akkalemye lah kom lungse elos.
Sanalande dziko ndi lupanga lawo, si mkono wawo umene unawabweretsera chigonjetso, koma ndi dzanja lanu lamanja, mkono wanu ndi kuwala kwa nkhope yanu, pakuti munawakonda.
4 Kom tokosra luk ac God luk; Kom sang kutangla nu sin mwet lom,
Inu ndinu Mfumu yanga ndi Mulungu wanga amene mumalamulira chigonjetso cha Yakobo.
5 Ac ke ku lom kut kutangla mwet lokoalok lasr.
Kudzera kwa inu ife timabweza adani athu; kudzera mʼdzina lanu timapondereza otiwukirawo.
6 Nga tia lulalfongi ke mwe pisr nutik Ku ke cutlass nutik in moliyula.
Sindidalira uta wanga, lupanga langa silindibweretsera chigonjetso;
7 A kom pa molikutla liki mwet lokoalok lasr Ac kutangulosla su srungakut.
koma Inu mumatigonjetsera adani athu, mumachititsa manyazi amene amadana nafe.
8 Kut ac fah kaksakin kom pacl e nukewa Ac sot kulo nu sum nwe tok ma pahtpat.
Timanyadira mwa Mulungu wathu tsiku lonse, ndipo tidzatamanda dzina lanu kwamuyaya.
9 Tuh pa inge kom siskutla ac lela tuh in kutangyukla kut; Kom tia sifil wi mwet mweun lasr fahsr nu ke mweun.
Koma tsopano mwatikana ndi kutichepetsa; Inu simupitanso ndi ankhondo athu.
10 Kom tuh oru kut kaingkin mwet lokoalok lasr, Na elos eisla ma lasr tuh in ma lalos.
Munachititsa ife kubwerera mʼmbuyo pamaso pa mdani ndipo amene amadana nafe atilanda katundu.
11 Ac kom lela tuh in anwuki kut oana sheep; Kom akfahsryekutelik in facl sin mwetsac.
Inu munatipereka kuti tiwonongedwe monga nkhosa ndipo mwatibalalitsa pakati pa anthu a mitundu ina.
12 Kom kukakunla mwet lom ke moul na srik Oana elos in ma na pilasr.
Inu munagulitsa anthu anu pa mtengo wotsika, osapindulapo kanthu pa malondawo.
13 Ke mwet tulan lasr liye ma kom oru nu sesr inge, Elos aksruksrukye kut ac isrun kut.
Mwachititsa kuti tikhale chochititsa manyazi kwa anthu a mitundu ina, chonyozeka ndi chothetsa nzeru kwa iwo amene atizungulira.
14 Kom orekut in mwe tafunkas inmasrlon mutanfahl uh; Ac mwet uh usruk sifalos kacsr in aksruksrukye kut.
Mwachititsa kuti tikhale onyozeka pakati pa anthu a mitundu ina; anthu amapukusa mitu yawo akationa.
15 Akpusiselyeyuk nga pacl nukewa; Ac arulana yohk mwekin luk
Manyazi anga ali pamaso panga tsiku lonse ndipo nkhope yanga yaphimbidwa ndi manyazi
16 Ke nga lohng pusren aksruksruk ac kas in akkoluk Lun mwet lokoalok luk, su srungayu.
chifukwa cha mawu otonza a iwo amene amandinyoza ndi kundichita chipongwe, chifukwa cha mdani amene watsimikiza kubwezera.
17 Ma inge nukewa sikyak nu sesr Kut finne tiana mulkinkomla Ku kunausla wulela su kom oakiya inmasrlosr ac kom.
Zonsezi zinatichitikira ngakhale kuti ifeyo sitinayiwale Inu kapena kuonetsa kusakhulupirika pa pangano lanu.
18 Kut tiana pilesrekomla; Kut tiana seakos ma sap lom.
Mitima yathu sinabwerere mʼmbuyo; mapazi athu sanatayike pa njira yanu.
19 Ne ouinge kom filikuti inmasrlon kosro lemnak; Ac kom siskutla in nien lohsr matoltol.
Koma Inu mwatiphwanya ndi kuchititsa kuti tikhale ozunzidwa ndi ankhandwe ndipo mwatiphimba ndi mdima waukulu.
20 Kut funu tui ac tila alu nu sin God lasr A kut alu nu sin god saya,
Tikanayiwala dzina la Mulungu wathu kapena kutambasulira manja athu kwa mulungu wachilendo,
21 Kom lukun konauk tari, Mweyen kom etu na pwaye nunak lukma lasr.
kodi Mulungu wathu sakanazidziwa zimenezi, pakuti Iye amadziwa zinsinsi zamumtima?
22 Tuh ke sripom, kutu sesr anwuki len nukewa; Orek kut oana sheep su kokola nu ke misa.
Komabe chifukwa cha Inu timakumana ndi imfa tsiku lonse, tili ngati nkhosa zoyenera kuti ziphedwe.
23 O Leum, ngutalik! Efu kom ku motul? Tukakek! Nikmet siskutla nwe tok!
Dzukani Ambuye! Nʼchifukwa chiyani mukugona! Dziwutseni nokha! Musatikane kwamuyaya.
24 Efu kom ku wikla liki kut? Nikmet mulkunla keok ac ongoiya lasr!
Nʼchifukwa chiyani mukubisa nkhope yanu, ndi kuyiwala mavuto athu ndi kuponderezedwa kwathu?
25 Kut itungyuki nu fin fohk uh; Kut kutangyukla oan infohk uh.
Tatsitsidwa pansi mpaka pa fumbi; matupi athu amatirira pa dothi.
26 Fahsru ac kasrekut! Molikutla ke lungse kawil lom!
Imirirani ndi kutithandiza, tiwomboleni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.

< Psalm 44 >