< Psalm 31 >

1 [Psalm lal David] Nga tuku nu yurum, LEUM GOD, in wikla yurum; Tia lela in kutangyukla nga. Kom sie God suwoswos; Nga pre nu sum tuh kom in moliyula!
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Mwa Inu Yehova, ine ndimathawiramo; musalole nʼkomwe kuti ndichititsidwe manyazi; mundipulumutse chifukwa cha chilungamo chanu.
2 Lohngyu, ac moliyula inge! Kom in eot ku luk, yen nga in wikla we, Sie pot ku in loangeyu.
Tcherani khutu lanu kwa ine, bwerani msanga kudzandilanditsa; mukhale thanthwe langa lothawirapo, linga lolimba kundipulumutsa ine.
3 Kom nien wikla luk ac mwe loango luk; Pwenyu ac kolyu in oana wulela lom.
Popeza Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa, chifukwa cha dzina lanu tsogolereni ndi kundiwongolera.
4 Karinginyu liki mwe kwasrip akoeyukla nu sik; Lisringyuyak liki mwe ongoiya.
Ndimasuleni mu msampha umene anditchera pakuti ndinu pothawirapo panga.
5 Nga sifacna eisyuwot nu inpoum. Kom fah moliyula, LEUM GOD, Tuh kom sie God oaru.
Mʼmanja mwanu ndipereka mzimu wanga; womboleni Yehova Mulungu wachoonadi.
6 Kom srungalos su alu nu sin god kikiap, A nga lulalfongi in kom.
Koma ine ndimadana nawo amene amamamatira mafano achabechabe; ine ndimadalira Yehova.
7 Nga fah engan ac kaksak Ke sripen lungse kawil lom. Kom liye luman keok luk, Ac kom etu mwe ongoiya nu sik.
Ndidzakondwa ndi kusangalala mʼchikondi chanu popeza Inu munaona masautso anga ndipo mumadziwa kuwawa kwa moyo wanga.
8 Kom tia lela tuh mwet lokoalok luk in sruokyuwi; Kom ase sukosok nu sik in fahsr nu yen nga lungse fahsr nu we.
Inu simunandipereke kwa mdani koma mwayika mapazi anga pa malo otakasuka.
9 LEUM GOD, pakomutuk, Tuh nga muta in ongoiya; Mutuk fafwak ke tung luk; Nga arulana totola.
Mundichitire chifundo Inu Yehova pakuti ndili pa mavuto; maso anga akulefuka ndi chisoni, mʼmoyo mwanga ndi mʼthupi mwanga momwe mukupweteka.
10 Nga foroti ke asor, Ac tung luk akfototoyela moul luk. Nga munasla ke sripen mwe akfohs puspis nu sik; Finne sri keik uh munasla pac.
Moyo wanga ukunyeka chifukwa cha kuwawidwa mtima ndi zaka zanga chifukwa cha kubuwula; mphamvu zanga zatha chifuwa cha masautso, ndipo mafupa anga akulefuka.
11 Mwet lokoalok luk nukewa, ac yokna mwet tulan luk, Elos orek angonkas nu sik; Elos su eteyu elos sangeng sik; Ke elos liyeyu inkanek uh, elos kaing.
Chifukwa cha adani anga onse, ndine wonyozeka kwambiri ndi anansi anga; ndine chochititsa manyazi kwa abwenzi anga. Iwo amene amandiona mu msewu amandithawa.
12 Mwet nukewa elos mulkinyula, oana nga in misa tari. Nga oana sie ma sisila.
Ine ndinayiwalika kwa iwo ngati kuti ndinamwalira; ndakhala ngati mʼphika wosweka.
13 Nga lohng ke mwet lokoalok luk elos mahma; Mwe aksangeng rauniyula. Elos orek pwapa in lainyu, Ac suk in uniyuwi.
Pakuti ine ndamva zonena zoyipa za anthu ambiri; zoopsa zandizungulira mbali zonse; iwo akukonza chiwembu kuti alimbane nane, kuti atenge moyo wanga.
14 Tusruktu lulalfongi luk uh oasr in kom, LEUM GOD; Kom God luk.
Koma ndikudalira Inu Yehova; ndikunena kuti, “Ndinu Mulungu wanga.”
15 Moul luk nufon oan inpoum; Moliyula liki poun mwet lokoalok luk, Liki elos su akkeokyeyu.
Masiku anga ali mʼmanja mwanu; ndipulumutseni kwa adani anga ndi kwa iwo amene akundithamangitsa.
16 Ngetnget in kulang nu sin mwet kulansap lom; Moliyula ke lungse kawil lom.
Walitsani nkhope yanu pa mtumiki wanu; pulumutseni mwa chikondi chanu chosatha.
17 Nga pang nu sum, LEUM GOD, Tia lela tuh nga in akmwekinyeyuk. Lela tuh mwet koluk in akmwekinyeyuk; Lela tuh elos in mislana som nu in facl sin mwet misa. (Sheol h7585)
Yehova musalole kuti ndichite manyazi, pakuti ndalirira kwa Inu; koma oyipa achititsidwe manyazi ndipo agone chete mʼmanda. (Sheol h7585)
18 Kaliya oalin mwet kikiap — Elos su filang ac inse fulat, Su kaskas in akkolukye mwet suwoswos.
Milomo yawo yabodzayo ikhale chete, pakuti chifukwa cha kunyada ayankhula modzikuza kutsutsana ndi wolungama.
19 Fuka yokiyen ma wo su kom elosak Nu selos su sunakin kom! Mwet nukewa etu lupan wo kom, Ac ouiyen karinginyuk ku lom nu selos su lulalfongi kom.
Ndi waukulu ubwino wanu umene mwawasungira amene amakuopani, umene mumapereka anthu akuona kwa iwo amene amathawira kwa Inu.
20 Kom okanulosla yurum Liki pwapa koluk lun mwet; Ac in sie acn misla kom okanulosla Liki kas in akkoluk lun mwet lokoalok lalos.
Mu mthunzi wa pamalo popezeka panu muwabisa, kuwateteza ku ziwembu za anthu; mʼmalo anu okhalamo mumawateteza kwa anthu owatsutsa.
21 Kaksakin LEUM GOD! Fuka lupan woiya ke El akkalemye lungse lal nu sik, Ke pacl mwet lokoalok luk rauniyula in mweuniyu!
Matamando akhale kwa Yehova, pakuti anaonetsa chikondi chake chodabwitsa kwa ine pamene ndinali mu mzinda wozingidwa.
22 Nga tuh sangeng ac nunku mu El sisyula liki ye mutal. Tusruktu El lohng pusren tung luk Ke nga pang nu sel in kasreyu.
Ndili mʼnkhawa zanga ndinati, “Ine ndachotsedwa pamaso panu!” Komabe Inu munamva kupempha chifundo kwanga pamene ndinapempha thandizo kwa Inu.
23 Lungse LEUM GOD, kowos mwet oaru lal nukewa, Tuh LEUM GOD El karinganang mwet oaru, A El arulana kaelos su filang.
Kondani Yehova oyera mtima ake onse! Yehova amasunga wokhulupirika koma amalanga kwathunthu anthu odzikuza.
24 Kowos in ku na, ac pulaik na, Kowos nukewa su oasr finsrak lowos in LEUM GOD.
Khalani ndi nyonga ndipo limbani mtima, inu nonse amene mumayembekezera Yehova.

< Psalm 31 >