< Psalm 24 >
1 [Psalm lal David] Faclu ac koano ma lun LEUM GOD; Faclu ac elos nukewa su muta fac ma pac lun LEUM GOD.
Salimo la Davide. Dziko lapansi ndi la Yehova ndi zonse zimene zili mʼmenemo, dziko ndi onse amene amakhala mʼmenemo;
2 El tulokinya fin kof lulap ye faclu, Ac oakiya ke acn loal meoa.
pakuti Iye ndiye anayika maziko ake pa nyanja ndi kulikhazika pamwamba pa madzi.
3 Su ac fah ku in fanyak nu fineol sin LEUM GOD? Ac su ac ku in utyak nu in acn mutal sel?
Ndani angakwere phiri la Yehova? Ndani angathe kuyima pa malo ake opatulika?
4 El su nasnas pao ac mutal insia; El tia alu nu ke ma sruloala Ku orek wulela kikiap.
Iye amene ali ndi mʼmanja moyera ndi mtima woyera, amene sapereka moyo wake kwa fano kapena kulumbira mwachinyengo.
5 LEUM GOD, su langoella, El ac fah akinsewowoyal ac fahkak lah wangin mwatal.
Iyeyo adzalandira madalitso kwa Yehova ndipo Mulungu mpulumutsi wake adzagamula kuti alibe mlandu.
6 Mwet ouinge pa elos su sokol, Su suk in tuku nu ye mutun God lal Jacob.
Umenewo ndiwo mʼbado wa amene amafunafuna Yehova; amene amafunafuna nkhope yanu, Inu Mulungu wa Yakobo. (Sela)
7 Keyak sifowos, O kowos mutunpot; Ac srukak na nu lucng, kowos mutunpot omeet me, Tuh Tokosra lun wolana Elan utyak.
Tukulani mitu yanu inu zipata; tsekukani, inu zitseko zakalekalenu, kuti Mfumu yaulemerero ilowe.
8 Su Tokosra lun wolana? LEUM GOD su ku ac kulana, LEUM GOD su kutangla ke mweun.
Kodi Mfumu yaulemereroyo ndani? Yehova Wamphamvuzonse, Yehova ndiye wamphamvu pa nkhondo.
9 Keyak sifowos, O kowos mutunpot; Ac srukak na nu lucng, kowos mutunpot omeet me, Tuh Tokosra lun wolana Elan utyak.
Tukulani mitu yanu, inu zipata; tsekukani, inu zitseko zakalekalenu, kuti Mfumu yaulemerero ilowe.
10 Su Tokosra lun wolana? LEUM GOD lun un mwe mweun — El pa Tokosra lun wolana!
Kodi Mfumu yaulemereroyo ndani? Yehova Wamphamvuzonse, Iye ndiye Mfumu yaulemerero. (Sela)