< Psalm 22 >

1 [Psalm lal David] God luk, God luk, efu kom ku fahsr likiyu? Nga tung ke insiuk nufon in suk kasru A wangin kasru tuku.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa “Mbawala yayikazi ya Mmawa.” Salimo la Davide. Mulungu wanga, Mulungu wanga, nʼchifukwa chiyani mwandisiya? Chifuwa chiyani simukundithandiza ndi pangʼono pomwe? Nʼchifukwa chiyani simukumva mawu a kudandaula kwanga?
2 Ke len uh nga pang nu sum, God luk, A kom tia topuk; Nga pang ke fong A nga tia ku in mongla.
Inu Mulungu wanga, ine ndimalira masana, koma simuyankha, usikunso, ndipo sindikhala chete.
3 Tusruktu kom muta fin tron lom oana El su Mutal, Su mwet Israel elos kaksakin.
Inu ndinu Woyera, wokhala pa mpando waufumu; ndinu matamando a Israeli.
4 Mwet matu lasr meet ah elos filiya lulalfongi lalos in kom; Elos lulalfongi kom, ac kom molelosla.
Pa inu makolo athu anadalira; iwo anadalira ndipo Inu munawapulumutsa.
5 Elos tuh pang nu sum, ac kom molelosla liki mwe sensen; Ac ke elos lulalfongi kom, elos tiana akmwekinyeyuk.
Analirira kwa inu ndipo munawapulumutsa. Iwo anakhulupirira Inu ndipo simunawakhumudwitse.
6 A inge nga tia sifilpa mwet se; nga oana wet soko, Mwet nukewa srungayu ac aksruksrukyeyu.
Koma ine ndine nyongolotsi osati munthu, wosekedwa ndi wonyozedwa ndi anthu onse.
7 Elos nukewa su liyeyu elos aksruksrukyeyu; Elos yayaiyu ac isrunyu.
Onse amene amandiona amandiseka; amandiyankhulira mawu achipongwe akupukusa mitu yawo kunena kuti
8 Elos fahk nu sik, “Kom lungsena lulalfongi LEUM GOD, Efu El ku tia molikomla? Fin pwaye LEUM GOD El lungse kom, Efu ku El tia kasrekom?”
“Iyeyu amadalira Yehova, musiyeni Yehovayo amulanditse. Musiyeni Yehova amupulumutse popeza amakondwera mwa Yehovayo.”
9 Kom pa akisusyeyula liki insien nina kiuk, Ac karinginyu ke nga katitiiyuk.
Komabe Inu ndinu amene munandibadwitsa, munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga. Munachititsa kuti ndizikudalirani ngakhale pa nthawi imene ndinkayamwa.
10 Nga nuna lulalfongi kom e ke len se nga isusla ah me, Ac kom nuna God luk.
Chibadwire ine ndinaperekedwa kwa Inu; kuchokera mʼmimba mwa amayi anga Inu mwakhala muli Mulungu wanga.
11 Nik kom loesla likiyu! Mwe ongoiya apkuranme Ac wangin mwet in kasreyu.
Musakhale kutali ndi ine, pakuti mavuto ali pafupi ndipo palibe wina wondipulumutsa.
12 Mwet lokoalok puspis apinyula oana cow mukul; Elos rauniyula yen nukewa Oana cow mukul sulallal in acn Bashan.
Ngʼombe zazimuna zandizungulira; ngʼombe zazimuna zamphamvu za ku Basani zandizinga.
13 Elos mangelik oana lion Su ngutngut ac kena kunausyula.
Mikango yobangula pokadzula nyama, yatsekula kwambiri pakamwa pawo kulimbana nane.
14 Ku luk wanginla, Wanginla oana kof ma kahkla nu infohk uh. Sri nukewa keik tufwaclik; Insiuk kofelik oana kiris.
Ine ndatayika pansi ngati madzi ndipo mafupa anga onse achoka mʼmalo mwake. Mtima wanga wasanduka phula; wasungunuka mʼkati mwanga.
15 Kapinsrulyuk pulamlamla oana kutkut, Ac louk fulfuli nu ke lac oalik lucng. Kom sisyula oana mwet misa se infohk uh.
Mphamvu zanga zauma ngati phale, ndipo lilime langa lamamatira ku nsagwada; mwandigoneka mʼfumbi la imfa.
16 Sie un mwet koluk rauniyula, Oana sie un kosro ngalngul su kuhlusyuwi Ac ngalis pouk ac niuk.
Agalu andizungulira; gulu la anthu oyipa landizinga. Alasa manja ndi mapazi anga.
17 Sri keik nukewa pisryak — ku in liyeyuk. Mwet lokoalok luk elos ngetma ac suiyuwi.
Ine nditha kuwerenga mafupa anga onse; anthu amandiyangʼanitsitsa ndi kundidzuma.
18 Elos susfa ke nuknuk luk Ac kitalik inmasrlolos.
Iwo agawana zovala zanga pakati pawo ndi kuchita maere pa zovala zangazo.
19 O LEUM GOD, nik kom muta loesla likiyu. Fahsru aksaye ac kasreyu!
Koma Inu Yehova, musakhale kutali; Inu mphamvu yanga, bwerani msanga kuti mudzandithandize.
20 Moliyula liki cutlass; Molela moul luk liki kosro ngalngul inge.
Pulumutsani moyo wanga ku lupanga, moyo wanga wopambanawu ku mphamvu ya agalu.
21 Moliyula liki lion inge; Wangin ku luk in lain cow mukul lemnak inge.
Ndilanditseni mʼkamwa mwa mikango; pulumutseni ku nyanga za njati.
22 Nga fah fahkak Inem nu sin mwet luk, Nga ac fah kaksakin kom ke pacl in tukeni lalos:
Ine ndidzalengeza dzina lanu kwa abale anga; ndidzakutamandani mu msonkhano.
23 “Kowos mwet kulansap lun LEUM GOD, kowos in kaksakunul! Mwet in fwil natul Jacob, kowos in akfulatyal! Mwet Israel, kowos in alu nu sel!
Inu amene mumaopa Yehova mutamandeni! Inu zidzukulu zonse za Yakobo, mulemekezeni! Muopeni mwaulemu, inu zidzukulu zonse za Israeli!
24 El tia pilesru mwet sukasrup ku ngetla liki keok lalos; El tia forla lukelos, A El topuk ke elos pang in suk kasru sel.”
Pakuti Iye sanapeputse kapena kunyoza kuvutika kwa wosautsidwayo; Iye sanabise nkhope yake kwa iye. Koma anamvera kulira kwake kofuna thandizo.
25 Nga ac fah kaksakin orekma lom inmasrlon walil uh; Ye mutalos su alu nu sum Nga ac fah oru mwe kisa su nga wulela kac.
Ndidzakutamandani pa msonkhano waukulu chifukwa cha zimene mwandichitira. Ndidzakwaniritsa lonjezo langa pamaso pa amene amaopa Inu.
26 Mwet enenu elos ac fah mongo nwe ke na elos kihpi; Elos su suk LEUM GOD elos fah kaksakunul. Lela tuh in wo ouiyalos nu tok ma pahtpat!
Osauka adzadya ndipo adzakhuta; iwo amene amafunafuna Yehova adzamutamanda. Mitima yanu ikhale ndi moyo mpaka muyaya!
27 Mutunfacl nukewa ac fah esam LEUM GOD. Liki acn nukewa fin faclu elos ac fah forla nu sel; Kain tuhn nukewa fin faclu fah alu nu sel.
Malekezero onse a dziko lapansi adzakumbukira Yehova ndi kutembenukira kwa Iye, ndipo mabanja a mitundu ya anthu adzawerama pamaso pake,
28 LEUM GOD El tokosra, Ac El leumi mutunfacl uh nufon.
pakuti ulamuliro ndi wake wa Yehova ndipo Iye amalamulira anthu a mitundu yonse.
29 Mwet nukewa su ku in mano fah mongo ac pasrla nu sel. Mwet nukewa su misa tari fah oayapa putati nu ye mutal, Aok, mwet nukewa su sukawil moul lalos.
Anthu olemera onse a dziko lapansi adzachita phwando ndi kulambira; onse amene amapita ku fumbi adzagwada pamaso pake; iwo amene sangathe kudzisunga okha ndi moyo.
30 Fwil tok uh ac fah kulansap nu sel; Elos ac fah kaskas ke Leum nu sin mwet in fwil tokolos.
Zidzukulu zamʼtsogolo zidzamutumikira Iye; mibado ya mʼtsogolo idzawuzidwa za Ambuye.
31 Ac fah srumunyuk nu sin mwet su soenna isusla Lah LEUM GOD El molela mwet lal.
Iwo adzalengeza za chilungamo chake kwa anthu amene pano sanabadwe pakuti Iye wachita zimenezi.

< Psalm 22 >