< Psalm 140 >

1 [Psalm lal David] LEUM GOD, moliyula liki mwet koluk; Langoeyula liki mwet sulallal.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Landitseni Yehova kwa anthu oyipa; tetezeni kwa anthu ankhanza,
2 Pacl nukewa elos pwapa in oru ma koluk; Elos purakak akukuin in pacl e nukewa.
amene mu mtima mwawo amakonza zinthu zoyipa ndi kuyambitsa nkhondo tsiku lililonse.
3 Lohulos oana serpent sulallal; Kas lalos oana pwasin ke wet cobra.
Iwo amanola malilime awo kukhala akuthwa ngati a njoka; pa milomo yawo pali ululu wa mamba. (Sela)
4 LEUM GOD, moliyula liki ku lun mwet koluk; Langoeyula liki mwet sulallal Su kena tuh nga in ikori.
Tetezeni Inu Yehova, kwa anthu oyipa; tchinjirizeni kwa anthu ankhanza amene amakonza zokola mapazi anga.
5 Mwet filang elos kena sruokyuwi; Elos oakiya mwe kwasrip lalos, Ac filiya sruhf pe inkanek uh in sruokyu.
Anthu odzikuza anditchera msampha mobisika; iwo atchera zingwe za maukonde awo ndipo anditchera misampha pa njira yanga. (Sela)
6 Nga fahk nu sin LEUM GOD, “Kom God luk.” LEUM GOD, porongeyu ke nga pang in suk kasru sum!
Inu Yehova, ine ndikuti, “Ndinu Mulungu wanga.” Imvani kupempha kwanga Yehova.
7 LEUM GOD Fulatlana luk, ke ku lom Kom langoeyula in pacl in mweun.
Inu Ambuye Wamphamvuzonse, Mpulumutsi wanga wamphamvu, mumateteza mutu wanga tsiku lankhondo.
8 LEUM GOD, nikmet sang nu sin mwet koluk ma lungse lalos; Nikmet akfahsrye pwapa koluk lalos.
Musawapatse anthu oyipa zokhumba zawo, Inu Yehova; musalole kuti zokonza zawo zitheke, mwina iwo adzayamba kunyada. (Sela)
9 Nikmet sang kutangla nu sin mwet lokoalok luk, Lela tuh ma koluk elos akoo nu sik in folokyang nu faclos.
Mitu ya amene andizungulira iphimbidwe ndi masautso amene milomo yawo yayambitsa.
10 Lela tuh mulut firir in putati faclos; Lela in sisila elos nu in luf loal ma elos tia ku in sifil illa liki.
Makala amoto agwere pa iwo; aponyedwe pa moto, mʼmaenje amatope, asatulukemonso.
11 Lela mwet su kinauk kas sutuu ke mwet saya in tia akilenyuk, A ma koluk in ukweya na mwet sulallal ac kunauselosla.
Musalole kuti anthu achipongwe akhazikike mʼdziko; choyipa chilondole anthu ankhanza.
12 LEUM GOD, nga etu lah kom loango sripa lun mwet sukasrup Ac orala nununku suwohs nu sin mwet enenu.
Ndikudziwa kuti Yehova amapereka chiweruzo cholungama kwa anthu osauka, ndipo amateteza zolinga za anthu osowa.
13 Pwayena lah mwet suwoswos elos fah kaksakin kom. Elos fah muta ye motom.
Zoonadi anthu olungama adzatamanda dzina lanu, ndipo anthu owongoka mtima adzakhala pamaso panu.

< Psalm 140 >