< Psalm 139 >

1 [Psalm lal David] LEUM GOD, kom liyeyu ac eteyu.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Inu Yehova, mwandisanthula ndipo mukundidziwa.
2 Kom etu ma nukewa nga oru; Kom ne muta loes likiyu, kom etu nunak luk nukewa.
Inu mumadziwa pamene ndikhala pansi ndi pamene ndidzuka; mumazindikira maganizo anga muli kutali.
3 Kom liyeyu lah nga orekma, ku nga mongla; Kom etu mukuikui luk nukewa.
Mumapenyetsetsa pamene ndikutuluka ndi kugona kwanga; mumadziwa njira zanga zonse.
4 Meet liki na nga kaskas, Kom etu tari lah mea nga ac fahk.
Mawu asanatuluke pa lilime langa mumawadziwa bwinobwino, Inu Yehova.
5 Kom apinyula ke siska nukewa, Kom karinginyu ke ku lom.
Mumandizinga kumbuyo ndi kutsogolo komwe; mwasanjika dzanja lanu pa ine.
6 Etu lom keik uh arulana yohk, Yohk liki ma nga ku in kalem kac.
Nzeru zimenezi ndi zopitirira nzeru zanga, ndi zapamwamba kuti ine ndizipeze.
7 Nga ac som nu ya in kaingla liki kom? Nga ac kaing nu ya liki ye motom?
Kodi ndingapite kuti kufuna kuzemba Mzimu wanu? Kodi ndingathawire kuti kuchoka pamaso panu?
8 Nga fin som nu inkusrao, kom oasr we; Nga fin ona infulan misa, kom oasr pac we. (Sheol h7585)
Ndikakwera kumwamba, Inu muli komweko; ndikakagona ku malo a anthu akufa, Inu muli komweko. (Sheol h7585)
9 Nga finne sokla loesla liki kutulap, Ku muta yen loeslana nu roto,
Ngati ndiwulukira kotulukira dzuwa, ngati ndikakhala ku malekezero a nyanja,
10 Kom ac oasr pac we in pwenyu, Kom ac oasr pa ingo in kasreyu.
kumenekonso dzanja lanu lidzanditsogolera, dzanja lanu lamanja lidzandigwiriziza.
11 Nga ku in siyuk lohsr uh in wikinyula Ku kalem su rauniyula in ekla nu ke fong,
Ndikanena kuti, “Zoonadi, mdima udzandibisa ndithu ndipo kuwunika kukhale mdima mondizungulira,”
12 Tusruktu, lohsr uh el tia lohsr nu sum, Ac fong uh arulana kalem nu sum, oana len. Lohsr ac kalem oana sie nu sum.
komabe mdimawo sudzakhala mdima kwa Inu; usiku udzawala ngati masana, pakuti mdima uli ngati kuwunika kwa Inu.
13 Kom lumahla ip nukewa ke monuk; Kom oakiyuwi insien nina kiuk.
Pakuti Inu munalenga za mʼkati mwanga; munandiwumba pamodzi mʼmimba mwa amayi anga.
14 Nga kaksakin kom mweyen fal mwet uh in sangeng sum. Ma nukewa kom oru, usrnguk ac wolana, Nga etu ouinge ke insiuk nufon.
Ndimakuyamikani chifukwa ndinapangidwa mochititsa mantha ndi modabwitsa; ntchito zanu ndi zodabwitsa, zimenezi ndimazidziwa bwino lomwe.
15 Ke mutawauk in lumweyuk sri keik uh, Ac oakiyuki wo insien nina kiuk, Ke nga kapkapak ingo in lukma, Kom nuna etu lah nga oasr we.
Mapangidwe anga sanabisike pamaso panu pamene ndimapangidwa mʼmalo achinsinsi, pamene ndinkawumbidwa mwaluso mʼmimba ya amayi anga.
16 Kom tuh liyeyu meet liki nga isusla. Pisen len ma oakiyuki nu sik tuh nga in moul Simla tari in book nutum Meet liki na kais sie ma inge mutawauk.
Maso anu anaona thupi langa lisanawumbidwe. Masiku onse amene anapatsidwa kwa ine, analembedwa mʼbuku lanu asanayambe nʼkuwerengedwa komwe.
17 O God, arulana pus nunak lom, Ac arulana upa nu sik in kalem kac.
Zolingalira zanu pa ine ndi zamtengowapatali, Inu Mulungu, ndi zosawerengeka ndithu!
18 Nga fin oek, pisalos ac pus liki puk uh. Ke nga ngutalik, nga srakna muta yurum.
Ndikanaziwerenga, zikanakhala zochuluka kuposa mchenga; pamene ndadzuka, ndili nanube.
19 O God, nga kena tuh kom in uniya mwet koluk! Nga arulana kena tuh mwet sulallal in fahsr likiyu.
Ndi bwino mukanangopha anthu oyipa, Inu Mulungu! Chokereni inu anthu owononga anzanu!
20 Elos fahk ma koluk keim; Elos fahk kas na koluk lain Inem.
Amayankhula za Inu ndi zolinga zoyipa; adani anu amagwiritsa ntchito dzina lanu molakwika.
21 O LEUM GOD, nga arulana srungalos su srungakom! Nga kwaselos su tuyak lain Kom.
Kodi ine sindidana nawo amene amakudani, Inu Yehova? Kodi sindinyansidwa nawo amene amakuwukirani?
22 Nga srungalos na pwaye; Nga oakalos mwet lokoalok luk.
Ndimadana nawo kwathunthu; ndi adani anga.
23 Liyeyu, O God, ac etu insiuk; Srikeyu, ac konauk nunak luk.
Santhuleni, Inu Mulungu ndipo mudziwe mtima wanga; Yeseni ndipo mudziwe zolingalira zanga.
24 Suk lah oasr kutena ma sufal in nga Ac kolyu ke inkanek kawil nu tok.
Onani ngati muli mayendedwe aliwonse oyipa mwa ine, ndipo munditsogolere mʼnjira yanu yamuyaya.

< Psalm 139 >