< Psalm 119 >

1 Insewowo elos su wangin mwatalos, Su moul fal nu ke ma sap lun LEUM GOD.
Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa, amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
2 Insewowo elos su fahsr ke ma sap lal, Su aksol ke insialos nufon.
Odala ndi amene amasunga malamulo ake, amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
3 Elos tiana oru ma koluk; A elos fahsr fal nu ke ma lungse lun LEUM GOD.
Sachita cholakwa chilichonse; amayenda mʼnjira zake.
4 LEUM GOD, kom ase tari ma sap lom Ac kom sapkin tuh kut in arulana akos.
Inu mwapereka malangizo ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
5 Saok ngan ku in arulana oaru In liyaung mwe luti lom!
Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika pa kumvera zophunzitsa zanu!
6 Nga fin liyaung ma sap lom nukewa, Na nga fah tia akmwekinyeyuk.
Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi, poganizira malamulo anu onse.
7 Ke nga lutlut ke nununku suwoswos lom Nga fah kaksakin kom ke inse nasnas.
Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama, pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
8 Nga fah akos ma sap lom; Nikmet sisyula.
Ndidzamvera zophunzitsa zanu; musanditaye kwathunthu.
9 Sie mwet fusr ac liyaung fuka tuh in nasnas moul lal? Pa inge: el fin akos ma sap lom.
Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake? Akawasamala potsata mawu anu.
10 Ke insiuk nufon nga srike in kulansupwekom; Nik kom lela nga in seakos ma sap lom.
Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse; musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
11 Nga likiya ma sap lom insiuk, Tuh nga in tia orekma koluk lain kom.
Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga kuti ndisakuchimwireni.
12 Nga kaksakin kom, O LEUM GOD, Lutiyu inkanek lom.
Mutamandike Inu Yehova; phunzitseni malamulo anu.
13 Nga fah kaskaskin Ma sap nukewa ma kom oakiya.
Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse amene amachokera pakamwa panu.
14 Nga engan in fahsr ke ma sap lom Liki na in eis mwe kasrup yohk.
Ndimakondwera potsatira malamulo anu monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
15 Nga lutlut ke oakwuk lom; Nga lohang nu ke mwe luti lom.
Ndimalingalira malangizo anu ndipo ndimaganizira njira zanu.
16 Nga insewowo ke ma sap lom, Nga fah tiana mulkunla kas lom.
Ndimakondwera ndi malamulo anu; sindidzayiwala konse mawu anu.
17 Nga mwet kulansap lom, kom in kulang nu sik Tuh nga fah ku in moul ac akos mwe luti lom.
Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; kuti tsono ndisunge mawu anu.
18 Ikasla mutuk tuh nga fah ku in akilen Wolana lun mwe luti pwaye lom.
Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
19 Nga muta fin faclu ke kitin pacl na fototo; Nikmet okanla ma sap lom likiyu.
Ine ndine mlendo pa dziko lapansi; musandibisire malamulo anu.
20 Insiuk kena ma lulap In liye nununku lom pacl e nukewa.
Moyo wanga wafowoka polakalaka malamulo anu nthawi zonse.
21 Kom kai mwet filang; Elos su tia akos ma sap lom elos selngawiyuk.
Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa, amene achoka pa malamulo anu.
22 Eisla kaskou ac aksruksruk lalos likiyu, Tuh nga liyaung na ma sap lom.
Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo pakuti ndimasunga malamulo anu.
23 Mwet leum elos tukeni ac pwapa koluk lainyu, Tusruktu nga fah lutlut ke mwe luti lom.
Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza, mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
24 Kas in luti lom akinsewowoyeyu Ac oana mwet kasru nu sik.
Malamulo anu amandikondweretsa; ndiwo amene amandilangiza.
25 Nga putatla nu infohk uh ke kutangyukla nga, Tukasyuyak, oana kom tuh wulela kac.
Moyo wanga wakangamira fumbi; tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
26 Nga fahkyuyak nu sum, ac kom topukyu; Luti nu sik inkanek lom.
Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha; phunzitseni malamulo anu.
27 Kasreyu tuh nga in kalem ke ma sap lom, Ac nga fah nunku yohk ke kas in luti wolana lom.
Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu; pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
28 Insiuk munasla ke asor; Akkeyeyu, oana kom tuh wulela kac.
Moyo wanga wafowoka ndi chisoni; limbikitseni monga mwa mawu anu.
29 Sruokyuwi liki inkanek tafongla; Ke kulang lom, luti nu sik ke ma sap lom.
Mundichotse mʼnjira zachinyengo; mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
30 Nga sulela tuh nga in akosten; Nga lohang nu ke nununku lom.
Ndasankha njira ya choonadi; ndayika malamulo anu pa mtima panga.
31 LEUM GOD nga liyaung na mwe luti lom, Nikmet lela tuh nga in akmwekinyeyuk.
Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
32 Nga arulana engan in akos ma sap lom, Mweyen kom ac fah akyokye etauk luk.
Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu, pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
33 O LEUM GOD, luti nu sik kalmen ma sap lom, Na nga fah akos in pacl e nukewa.
Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu; ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
34 Aketeya ma sap lom nu sik, ac nga fah akos; Nga fah liyaung ke insiuk nufon.
Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
35 Oru tuh nga in fahsr fal nu ke ma sap lom, Tuh nga konauk insewowo kac.
Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu, pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
36 Oru tuh nga in lungse akos ma sap lom Yohk liki na tuh nga in kasrup.
Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu, osati chuma.
37 Furokla mutuk liki ma lusrongten; Liyeyume oana kom tuh wulela kac.
Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe; sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
38 Nga mwet kulansap lom, akfalye wulela lom nu sik, In oana wulela su kom oru nu selos su akos kom.
Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu, kuti Inu muopedwe.
39 Moliyula liki kaskas kou su nga sangeng kac; Fuka woiyen nununku lom!
Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa, pakuti malamulo anu ndi abwino.
40 Nga kena akos ma sap lom; Ase moul sasu nu sik, tuh kom suwoswos.
Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu! Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
41 LEUM GOD, akkalemye lupan lungse lom nu sik, Ac moliyula oana kom wulela kac.
Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova, chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
42 Na nga fah ku in topkolos su kaskas kou keik, Mweyen nga lulalfongi ke kas lom.
ndipo ndidzayankha amene amandinyoza, popeza ndimadalira mawu anu.
43 Oru tuh nga in ku in kaskas pwaye pacl e nukewa, Tuh finsrak luk oan in nununku lom.
Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga, pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
44 Nga ac fah liyaung ma sap lom pacl e nukewa, Nu tok ma pahtpat.
Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse, ku nthawi za nthawi.
45 Nga fah muta in sukosok pwaye, Mweyen nga srike in akos kas in luti lom.
Ndidzayendayenda mwaufulu, chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
46 Nga fah fahkak nu sin tokosra uh ma kom sapkin, Ac nga fah tia akmwekinyeyuk.
Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
47 Nga pulakin insewowo ke nga akos ma sap lom, Mweyen nga arulana lungse kas lom.
popeza ndimakondwera ndi malamulo anu chifukwa ndimawakonda.
48 Nga sunakin ac lungse ma sap lom, Ac nga fah nunku yohk ke mwe luti lom.
Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda, ndipo ndimalingalira malangizo anu.
49 Esam wulela lom nu sik, mwet kulansap lom, Tuh ma inge ase finsrak nu sik.
Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu, popeza mwandipatsa chiyembekezo.
50 Finne in pacl in keok luk, nga akwoyeyuk Mweyen wulela lom ase moul nu sik.
Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi: lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
51 Mwet filang elos aksruksrukiyu pacl nukewa, Tusruktu nga tiana fahsr liki ma sap lom.
Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa, koma sindichoka pa malamulo anu.
52 Nga esam nununku lom in pacl oemeet, Ac ma inge akwoyeyu, O LEUM GOD.
Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale, ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
53 Ke nga liye mwet koluk ke elos lain ma sap lom, Nga arulana kasrkusrak.
Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa amene ataya malamulo anu.
54 In pacl fototo luk fin faclu Nga kinala on ke sap lom.
Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga kulikonse kumene ndigonako.
55 Ke fong uh nga esam kom, O LEUM GOD, Ac nga nunku ke ma sap lom.
Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova, ndipo ndidzasunga malamulo anu.
56 Nga pulakin insewowo Ke nga akos ma sap lom.
Ichi ndicho ndakhala ndikuchita: ndimasunga malangizo anu.
57 O LEUM GOD, kom na pa nga enenu, Ac nga wulela tuh nga fah akos ma sap lom.
Yehova, Inu ndiye gawo langa; ndalonjeza kumvera mawu anu.
58 Nga siyuk sum ke insiuk nufon Tuh kom in pakomutuk, in oana wulela lom.
Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse; mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
59 Ke nga nunku ke ouiyen moul luk, Nga wulela nga in sifil forla ac fahsr tukun mwe luti lom.
Ndinalingalira za njira zanga ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
60 Nga sulaklak, ac tia tuptupan In akos ma kom sapkin.
Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza kumvera malamulo anu.
61 Mwet koluk elos filiya mwe kwasrip nu sik, Tusruktu nga tiana mulkunla ma sap lom.
Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe, sindidzayiwala lamulo lanu.
62 Ke infulwen fong nga tukakek Ac kaksakin kom ke nununku suwoswos lom.
Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu chifukwa cha malamulo anu olungama.
63 Nga mwet kawuk lun mwet nukewa su kulansupwekom, Aok, elos nukewa su akos ma sap lom.
Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani, kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
64 LEUM GOD, faclu sessesla ke lungkulang lom; Lutiyu ke ma sap lom.
Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika, phunzitseni malamulo anu.
65 LEUM GOD, kom oru wo nu sik, mwet kulansap lom, Fal nu ke wulela lom.
Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu molingana ndi mawu anu.
66 Ase etauk ac lalmwetmet nu sik, Tuh nga lulalfongi ke sap lom.
Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino, pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
67 Meet liki kom tuh kaiyu, nga fahsr sayen ma sap lom, A inge nga akos kas lom.
Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera, koma tsopano ndimamvera mawu anu.
68 Kom arulana wo ac arulana kulang! Lutiyu ke sap lom.
Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino; phunzitseni malamulo anu.
69 Mwet filang elos tuh fahk kas kikiap keik, Tusruktu nga akos mwe luti lom ke insiuk nufon.
Ngakhale odzikuza andipaka mabodza, ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
70 Wanginna kalem lun mwet inge, A funu nga, nga insewowo ke ma sap lom.
Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa, koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
71 Kaiyuk lom nu sik mwe akwoyeyu, Mweyen ke sripa sac nga lutlut ke ma sap lom.
Ndi bwino kuti ndinasautsidwa kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
72 Ma sap su kom ase nu sik, yohk kalmac nu sik Liki mani nukewa fin faclu.
Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
73 Kom oreyula ac karinginyu; Ase etauk nu sik tuh nga fah luti ma sap lom.
Manja anu anandilenga ndi kundiwumba; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
74 Elos su akfulatye kom elos ac engan ke elos liyeyu, Mweyen nga lulalfongi ke wulela lom.
Iwo amene amakuopani akondwere akandiona, chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
75 LEUM GOD, nga etu tuh nununku lom suwohs, Ac kom kaiyu mweyen kom inse pwaye.
Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
76 Lela lungse kawil lom in akwoyeyu, Oana kom tuh wulela nu sik, mwet kulansap lom.
Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa, molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
77 Pakomutuk, ac nga fah moul, Tuh nga insewowo ke ma sap lom.
Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo, popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
78 Lela mwet filang in mwekin lah elos akkolukyeyu ke kikiap; A funu nga, nga fah arulana nunku ke kas in luti lom.
Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa; koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
79 Lela tuh elos su akfulatye kom in tuku nu yuruk — Elos nukewa su etu ke ma sap lom.
Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine, iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
80 Lela nga in akos na pwaye ma sap lom Tuh nga fah tia akmwekinyeyuk.
Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu kuti ndisachititsidwe manyazi.
81 LEUM GOD, nga totola in soano molela lom nu sik; Nga filiya lulalfongi luk ke kas lom.
Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu, koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
82 Mutuk totola in tupan ma kom tuh wulela kac, Ac nga fahk, “Kom ac kasreyu ngac?”
Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu; Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
83 Nga oana sie pak in neinyuk wain ma sisila ac wanginla sripa, Tusruktu nga tiana mulkunla ma sap lom.
Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi sindiyiwala zophunzitsa zanu.
84 Nga ac soano putaka? Kom ac kai mwet su akkeokyeyu ngac?
Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti? Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
85 Mwet filang su tia akos ma sap lom, Elos pukanak luf in sruokyuwi.
Anthu osalabadira za Mulungu, odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
86 Ma sap lom nukewa fal in lulalfongiyuk; Mwet elos akkeokyeyu ke kas kikiap — kasreyu!
Malamulo anu onse ndi odalirika; thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
87 Elos apkuranna in uniyuwi, Tusruk nga tiana pilesrala ma sap lom.
Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi koma sindinataye malangizo anu.
88 Ke lungse kawil lom, oru wo nu sik, Tuh nga fah akos ma sap lom.
Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
89 Kas lom, O LEUM GOD, oan ma pahtpat, Aok, oan ma pahtpat inkusrao.
Mawu anu Yehova ndi amuyaya; akhazikika kumwambako.
90 Oaru lom oanna ke fwil nukewa; Kom tuh oakiya faclu, ac faclu srakna oan.
Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse; Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
91 Ma nukewa oanna nwe misenge ke sripen sap lom, Ac ma nukewa kulansapwekom.
Malamulo anu alipobe mpaka lero lino, pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
92 Ma sap lom funu tia ase insewowo nu sik, Nga lukun misa tari ke mwe keok nu sik.
Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa, ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
93 Nga fah tiana pilesru kas in luti lom; Tuh ke ma inge kom moliyula.
Ine sindidzayiwala konse malangizo anu, pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
94 Nga ma lom — moliyula! Nga srike na in akos ma sap lom.
Ndine wanu, ndipulumutseni; pakuti ndasamala malangizo anu.
95 Mwet koluk elos soano in uniyuwi, Tusruktu nga fah arulana nunku ke ma sap lom.
Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge, koma ndidzalingalira umboni wanu.
96 Nga etu tari lah oasr saflaiyen ma nukewa; Tusruktu ma sap lom wangin saflaiya.
Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe malire konse.
97 Arulana yohk lungse luk ke ma sap lom! Nga nunku kac ke len nufon.
Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu! Ndimalingaliramo tsiku lonse.
98 Ma sap lom wiyu pacl e nukewa Ac oru nga lalmwetmet liki mwet lokoalok luk.
Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga, popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
99 Nga kalem kac yohk liki mwet luti luk nukewa, Mweyen nga arulana nunku ke kas in luti lom.
Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse popeza ndimalingalira umboni wanu.
100 Yohk lalmwetmet luk liki mwet matu, Mweyen nga akos ma sap lom.
Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba, popeza ndimamvera malangizo anu.
101 Nga taranyu liki orekma koluk nukewa, Mweyen nga lungse akos kas lom.
Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa kuti ndithe kumvera mawu anu.
102 Nga tiana pilesrala kas in luti lom, Mweyen kom na pa lutiyu.
Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu, pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
103 Kas in luti lom arulana emwem, Aok, emwem liki na honey nu ke oalik!
Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa, otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
104 Nga eis lalmwetmet ke ma sap lom, Ke ma inge nga srunga inkanek koluk nukewa.
Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu; kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
105 Kas lom lam nu ke niuk Ac kalem nu ke inkanek luk.
Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
106 Nga orala sie wulela na ku Tuh nga in akos kas in luti suwoswos lom.
Ndalumbira ndipo ndatsimikiza, kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
107 LEUM GOD, pwayena lah mwe keok luk arulana upa; Sruokya moul luk, oana ke kom wulela.
Ndazunzika kwambiri; Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
108 Eis pre in sang kulo luk, O LEUM GOD, Ac lutiyu ke ma sap lom.
Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
109 Nga akola pacl nukewa in pilesrala moul luk, Tuh nga tiana mulkunla ma sap lom.
Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi, sindidzayiwala malamulo anu.
110 Mwet koluk elos filiya mwe kwasrip nu sik, Tuh nga tiana pilesrala ma sap lom.
Anthu oyipa anditchera msampha, koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
111 Ma sap lom mwe usru luk nwe tok, Aok, mwe engan lun insiuk.
Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya; Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
112 Nga sulela tari tuh nga in akos ma sap lom Nwe ke na nga misa.
Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu mpaka kumapeto kwenikweni.
113 Nga srungalos su tia inse pwaye nu sum, A nga lungse ma sap lom.
Ndimadana ndi anthu apawiripawiri, koma ndimakonda malamulo anu.
114 Kom nien wikla luk ac lango luk; Nga filiya finsrak luk in wuleang lom.
Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
115 Mwet koluk, kowos fahla likiyu. Nga ac fah akos ma sap lun God luk.
Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa, kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
116 Akkeyeyu, oana kom wulela, ac nga fah moul; Nikmet lela tuh nga in toasrla ke sripen tia sun mwe finsrak luk!
Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
117 Sruokyuwi tuh nga fah tu na ku, Ac nga fah lohang nu ke ma sap lom pacl e nukewa.
Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa; nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
118 Kom ngetla liki mwet nukewa su seakos ma sap lom; Pwapa kutasrik lalos wangin sripa.
Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu, pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
119 Kom oru mwet koluk nukewa oana kutkut, Ke ma inge nga lungse kas in luti lom.
Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala; nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
120 Ke sripom nga sangeng; Nga arulana sangeng ke sripen nununku lom.
Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu; ndimachita mantha ndi malamulo anu.
121 Nga oru ma suwohs ac pwaye; Nikmet filiyula nu inpoun mwet lokoalok luk.
Ndachita zolungama ndi zabwino; musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
122 Wulela nu sik lah kom ac kasru mwet kulansap lom; Nikmet lela mwet inse fulat in akkeokyeyu.
Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino, musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
123 Mutuk totola in soano molela lom nu sik Su kom tuh wulela kac.
Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu, kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
124 Oru nu sik fal nu ke lungse kawil lom, Ac luti nu sik sap ku lom.
Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
125 Nga mwet kulansap lom; ase etauk nu sik Tuh nga fah etu kas in luti lom.
Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa, kuti ndimvetsetse umboni wanu.
126 LEUM GOD, pacl fal kom in kai mwet uh, Mweyen elos seakos ma sap lom.
Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu; malamulo anu akuswedwa.
127 Nga lungse ma sap lom yohk liki gold, Yohk liki gold ma arulana nasnas.
Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
128 Ke ma inge nga fahsr ke inkanek in luti lom nukewa; Ac nga srunga inkanek sutuu nukewa.
ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka, ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
129 Kas in luti lom wolana; Nga akos ke insiuk nufon.
Maumboni anu ndi odabwitsa nʼchifukwa chake ndimawamvera.
130 Aketeyen mwe luti lom ase kalem, Ac sang etauk nu sin mwet nikin.
Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika; ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
131 In kena luk nu ke sap ku lom Nga mangelik na ke malak luk.
Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu, kufunafuna malamulo anu.
132 Forma nu sik ac pakomutuk, Oana kom oru nu selos nukewa su lungse kom.
Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo, monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
133 Sruokyuwi nga in tia ikori, fal nu ke wulela lom, Ac tia lela tuh ma koluk in kutangyula.
Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu; musalole kuti tchimo lizindilamulira.
134 Moliyula liki mwet su akkeokyeyu, Tuh nga fah akos sap lom.
Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza, kuti ndithe kumvera malangizo anu.
135 Kom in akinsewowoyeyu ke kalem lun motom, Ac lutiyu ke oakwuk lom.
Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
136 Sroninmutuk sororla oana soko infacl Mweyen mwet uh elos tia akos ma sap lom.
Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga, chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
137 LEUM GOD, kom suwoswos, Ac ma sap lom suwosna.
Yehova ndinu wolungama, ndipo malamulo anu ndi abwino.
138 Oakwuk ma kom ase tari Arulana fal ac suwohs.
Maumboni amene munatipatsa ndi olungama; ndi odalirika ndithu.
139 Kasrkusrak luk tayak in nga oana sie e, Mweyen mwet lokoalok luk elos tia akilen ma sap lom.
Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
140 Wulela lom pwayena! Nga arulana lungse!
Mawu anu ndi woyera kwambiri nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
141 Nga mwet lusrongten, ac kwaseyuk nga, Tusruktu nga tia pilesru kas in luti lom.
Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka, sindiyiwala malangizo anu.
142 Suwoswos lom ac fah oan ma pahtpat, Ac ma sap lom pwaye pacl e nukewa.
Chilungamo chanu nʼchamuyaya, ndipo malamulo anu nʼchoona.
143 Nga arulana keok ac fosrnga, Tusruktu ma sap lom akinsewowoyeyu.
Mavuto ndi masautso zandigwera, koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
144 Kas in luti lom suwosna in pacl e nukewa; Ase nu sik etauk ac nga fah moul.
Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
145 Nga pang nu sum ke insiuk nufon. Topukyu, O LEUM GOD, ac nga fah akos ma sap lom.
Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova, ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
146 Nga pang nu sum, Moliyula, ac nga fah liyaung ma sap lom.
Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni ndipo ndidzasunga umboni wanu.
147 Meet liki lenelik nga pang nu sum in kasreyu; Nga filiya finsrak luk in wulela lom.
Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
148 In fong nufon se nga oanna ngetnget, Ac nunku yohk ke kas in luti lom.
Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku, kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
149 Lohngyu, O LEUM GOD, ke sripen lungse lom kawil; Pakomutuk ac moliyula.
Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
150 Mwet su akkeokyeyu elos apkuranme, Aok, elos su tiana karinganang ma sap lom.
Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira, koma ali kutali ndi malamulo anu.
151 Tusruk kom apkuran nu yuruk, LEUM GOD, Ac ma sap lom nukewa oanna nwe tok.
Koma Inu Yehova muli pafupi, malamulo anu onse ndi woona.
152 In pacl loeloes somla nga lutlut ke mwe luti lom, Tuh kom oakiya in oan ma pahtpat.
Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
153 Liye keok luk, ac moliyula, Mweyen nga tiana pilesru ma sap lom.
Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
154 Loangeyu ac aksukosokyeyu; Moliyula, oana kom tuh wulela.
Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola; sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
155 Mwet koluk ac fah tia moliyukla, Mweyen elos tia akos ma sap lom.
Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa, pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
156 A pakoten lom yoklana, LEUM GOD. Akkalemye pakoten lom ac moliyula.
Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu; sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
157 Pus mwet lokoalok luk ac mwet kalyeiyu, Tusruktu nga tiana mulkunla in akos ma sap lom.
Adani amene akundizunza ndi ambiri, koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
158 Ke nga liye mwet kutasrik inge, nga arulana toasr selos, Mweyen elos tia liyaung sap lom.
Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro, popeza samvera mawu anu.
159 LEUM GOD, liye lupan lungse luk nu ke kas in luti lom. Lungse lom uh tiana ekyek, ke ma inge moliyula!
Onani momwe ndimakondera malangizo anu; sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
160 Kas nukewa in ma sap lom arulana pwaye, Ac nununku suwoswos nukewa lom oan ma pahtpat.
Mawu anu onse ndi owona; malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
161 Mwet leum elos kalyeiyu ke wangin mwetik, Tusruktu nga akfulatye ma sap lom.
Olamulira amandizunza popanda chifukwa, koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
162 Nga arulana engan ke wuleang lom Oana sie mwet su konauk mwe kasrup yohk lal.
Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu, ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
163 Nga srunga ac kwase ma kikiap nukewa, A nga lungse ma sap lom.
Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho, koma ndimakonda malamulo anu.
164 Pacl itkosr in len se nga fahkak kulo luk nu sum, Ke sripen nununku suwohs lom.
Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku pakuti malamulo anu ndi olungama.
165 Elos su lungse ma sap lom elos muta in misla wo, Ac wangin kutena ma ac fah aktukulkulyelos.
Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
166 LEUM GOD, nga soano kom in moliyula, Ac nga oru ma kom sapkin.
Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova, ndipo ndimatsatira malamulo anu.
167 Nga akos kas in luti lom, Ac lungse ma inge ke insiuk nufon.
Ndimamvera umboni wanu pakuti ndimawukonda kwambiri.
168 Nga akos ma sap lom ac mwe luti lom; Kom liye ma nukewa nga oru.
Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu, pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
169 Lela pusren pang luk nu sum in sun kom, LEUM GOD! Ase etauk nu sik, oana kom tuh wulela.
Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova; patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
170 Porongo pre luk, Ac moliyula, fal nu ke wulela lom!
Kupempha kwanga kufike pamaso panu; pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
171 Nga fah kaksakin kom pacl e nukewa, Mweyen kom lutiyu ke ma sap lom.
Matamando asefukire pa milomo yanga, pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
172 Nga fah onkakin ma sap lom, Mweyen ma sap lom suwohs.
Lilime langa liyimbe mawu anu, popeza malamulo anu onse ndi olungama.
173 Akola pacl nukewa in kasreyu, Tuh nga sulela in fahsr tukun ma sap lom.
Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza pakuti ndasankha malangizo anu.
174 O LEUM GOD, nga kena eis kasru sum in moliyula. Nga konauk engan in ma sap lom.
Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova, ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
175 Lela nga in moul, tuh nga fah ku in kaksakin kom; Lela tuh mwe luti lom in kasreyu.
Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni, ndipo malamulo anu andichirikize.
176 Nga nikinyula in fufahsryesr luk oana soko sheep tuhlac; Ke ma inge fahsru ac sukyu, mwet kulansap lom, Mweyen nga tiana pilesru ma sap lom.
Ndasochera ngati nkhosa yotayika, funafunani mtumiki wanu, pakuti sindinayiwale malamulo anu.

< Psalm 119 >