< Psalm 118 >

1 Sang kulo nu sin LEUM GOD, tuh El wo, Ac lungkulang lal oan ma pahtpat.
Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.
2 Lela mwet Israel in fahk, “Lungkulang lal oan ma pahtpat.”
Israeli anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
3 Lela mwet tol lun God in fahk, “Lungkulang lal oan ma pahtpat.”
Banja la Aaroni linene kuti, “Chikondi chake ndi chosatha.”
4 Lela elos nukewa su alu nu sel in fahk, “Lungkulang lal oan ma pahtpat.”
Iwo amene amaopa Yehova anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
5 In ongoiya luk nga pang nu sin LEUM GOD. El topukyu ac aksukosokyeyula.
Ndili mʼmasautso anga ndinalirira Yehova, ndipo Iye anayankha pondichotsa mʼmasautsowo.
6 LEUM GOD El wiyu, nga fah tia sangeng; Mea mwet uh ku in oru nu sik?
Yehova ali nane; sindidzachita mantha. Munthu angandichite chiyani?
7 LEUM GOD pa kasreyu, Ac nga fah liye ke mwet lokoalok luk kutangyukla.
Yehova ali nane; Iye ndiye thandizo langa. Ndidzayangʼana adani anga mwachipambano.
8 Wo in lulalfongi LEUM GOD Liki in lulalfongi mwet uh.
Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira munthu.
9 Wo in lulalfongi LEUM GOD Liki in lulalfongi mwet kol faclu.
Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira mafumu.
10 Mwet lokoalok pus rauniyula, Tusruktu nga kunauselosla ke ku lun LEUM GOD!
Anthu a mitundu yonse anandizinga, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
11 Elos apinyula ke siska nukewa, Tusruktu nga kunauselosla ke ku lun LEUM GOD!
Anandizinga mbali zonse, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
12 Elos rirme apinyula oana bee uh, Tusruktu elos firiryak ac sa na wanginla, oana firirla lun mah pao; Nga kunauselosla ke ku lun LEUM GOD.
Anandizinga ngati njuchi, koma anatha msanga ngati moto wapaminga; mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
13 Elos mweuniyu arulana upa, ac nga apkuran in kutangyukla, Tusruktu, LEUM GOD El kasreyu.
Anandikankha uku ndi uko ndipo ndinali pafupi kugwa, koma Yehova anandithandiza.
14 LEUM GOD El oru tuh nga in ku ac fokoko; El moliyula.
Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; Iye wakhala chipulumutso changa.
15 Porongo pusren sasa in engan ke kutangla in lohm nuknuk sin mwet lun God, “Ku lulap lun LEUM GOD pa oru ma inge!
Mfuwu wachimwemwe ndi chipambano ukumveka mʼmatenti a anthu olungama mtima kuti: “Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!
16 Ku lal pa ase kutangla nu sesr, Aok ku lal in pacl in mweun.”
Dzanja lamanja la Yehova latukulidwa mmwamba Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!”
17 Nga fah tia misa, a nga ac moul Ac fahkak ke ma LEUM GOD El oru.
Sindidzafa koma ndidzakhala ndi moyo ndipo ndidzalalika za ntchito ya Yehova.
18 El arulana kaiyu upa, Tusruktu El tiana lela nga in misa.
Yehova wandilanga koopsa, koma sanandipereke ku imfa.
19 Ikasla mutunpot lun Tempul nu sik. Nga ac fah utyak ac sang kulo nu sin LEUM GOD!
Tsekulireni zipata zachilungamo, kuti ndifike kudzayamika Yehova.
20 Pa inge mutunpot lun LEUM GOD; Mwet suwoswos mukena ku in utyak we.
Ichi ndicho chipata cha Yehova chimene olungama mtima okha adzalowerapo.
21 Nga kaksakin kom, LEUM GOD, tuh kom lohngyu, Ac ase kutangla nu sik.
Ndidzakuyamikani chifukwa Inu munandiyankha; mwakhala chipulumutso changa.
22 Eot se su mwet musa elos sisla, Sikyak tuh pa inge eot se ma yohk sripa oemeet.
Mwala umene amisiri omanga nyumba anawukana wasanduka wapangodya;
23 Ma inge ma LEUM GOD El oru; Fuka lupan woiya ke kut liye!
Yehova ndiye wachita zimenezi ndipo nʼzodabwitsa pamaso pathu.
24 Pa inge len se su LEUM GOD El orala; Lela kut in engan ac akfulatye!
Lero ndiye tsiku limene Yehova walipanga; tiyeni tikondwere ndi kusangalala nalo.
25 Molikutla, LEUM GOD, molikutla! Ase wo ouiya nu sesr, LEUM GOD!
Inu Yehova, tipulumutseni; Yehova, tipambanitseni.
26 Lela God Elan akinsewowoye el su tuku ke Inen LEUM GOD! Liki Tempul lun LEUM GOD kut akinsewowoye kom.
Wodala amene akubwera mʼdzina la Yehova. Tikukudalitsani kuchokera ku nyumba ya Yehova.
27 Tuh LEUM GOD El God, El ase kalem nu sesr. Ke lesak inpouwos kowos in mutawauk pacl in akfulat Ac fahsr rauni loang uh.
Yehova ndi Mulungu, ndipo kuwala kwake kwatiwunikira Ife. Lowani nawo pa mʼdipiti wa ku chikondwerero mutanyamula nthambi mʼdzanja lanu, mpaka ku nyanga za guwa.
28 Kom God luk, ac nga sot kulo nu sum; Nga fah fahkak fulat lom.
Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakuyamikani; Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakukwezani.
29 Sang kulo nu sin LEUM GOD, tuh El wo Ac lungkulang lal oan ma pahtpat.
Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.

< Psalm 118 >