< Psalm 111 >

1 Kaksakin LEUM GOD! Ke insiuk nufon nga fah sang kulo nu sin LEUM GOD In walil lun mwet lal.
Tamandani Yehova. Ndidzathokoza Yehova ndi mtima wanga wonse mʼbwalo la anthu olungama mtima ndi pa msonkhano.
2 Fuka woiyen orekma lun LEUM GOD! Elos nukewa su engan kac elos ke etu kalmeya.
Ntchito za Yehova nʼzazikulu; onse amene amakondwera nazo amazilingalira.
3 Ma nukewa El oru uh fahkak ke ku ac wal fulat lal. Suwoswos lal ac fah oan ma pahtpat.
Zochita zake ndi za ulemerero ndi zaufumu, ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
4 LEUM GOD El tia lela kut in mulkunla orekma wolana lal; El kulang ac pakoten.
Iye wachititsa kuti zodabwitsa zake zikumbukirike; Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo.
5 El sang mwe mongo nu selos su akfulatyal; El tiana mulkunla wuleang lal.
Amapereka chakudya kwa amene amamuopa Iye; amakumbukira pangano lake kwamuyaya.
6 El akkalemye ku lal nu sesr, mwet lal, Ke El ase nu sesr acn sin mwet in mutunfacl saya.
Waonetsa anthu ake mphamvu ya ntchito zake, kuwapatsa mayiko a anthu a mitundu ina.
7 El oaru ac suwoswos in ma nukewa El oru. Sap lal nukewa fal in lulalfongiyuk.
Ntchito za manja ake ndi zokhulupirika ndi zolungama; malangizo ake onse ndi odalirika.
8 Sap lal inge oakwuki na nwe tok, Ituku ke pwaye ac suwoswos.
Malamulo ndi okhazikika ku nthawi za nthawi, ochitidwa mokhulupirika ndi molungama.
9 El aksukosokye mwet lal Ac oru sie muleang kawil yorolos. El mutallana ac kulana.
Iyeyo amawombola anthu ake; anakhazikitsa pangano lake kwamuyaya dzina lake ndi loyera ndi loopsa.
10 Sangeng sin LEUM GOD pa mutaweyen lalmwetmet. Nu selos nukewa su akos ma sap lal, El sang elos in etu in oru sulela wo. Fal in kaksakinyuk El ma pahtpat.
Kuopa Yehova ndicho chiyambi cha nzeru; onse amene amatsatira malangizo ake amamvetsa bwino zinthu. Iye ndi wotamandika mpaka muyaya.

< Psalm 111 >