< Soakas 1 >

1 Soakas lal Solomon, wen natul David ac tokosra lun Israel.
Iyi ndi miyambi ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israeli:
2 Soakas uh ma ac ku in kasrekom in ku in akilen lalmwetmet ac kas in kasru wowo, oayapa in kalem ke kas na loal kalmac.
Ndi yothandiza kuti munthu adziwe nzeru ndi malangizo; kuti amvetse mawu a matanthauzo ozama;
3 Ku in luti kom ke moul in etauk, tuh moul lom in pwaye, suwohs, ac fal.
kuti alandire malangizo othandiza kuti achite zinthu mwanzeru, akhale wangwiro, wachilungamo ndiponso wosakondera.
4 Ku in sang etauk nu sin sie mwet srik etu la, ac luti mwet fusr in pah in nunak.
Ndi yothandiza munthu wamba kuti aphunzire nzeru za kuchenjera, achinyamata kudziwa zinthu bwino ndi kulingalira.
5 Soakas inge ku pac in akyokyelik etauk lun mwet lalmwetmet, ac sang inkanek pwaye nu sin mwet etauk
Munthu wanzeru amvetse bwino miyamboyi kuti awonjezere kuphunzira kwake, ndi munthu womvetsa zinthu bwino apatepo luso,
6 tuh elos in ku in etu kalmac lukma lun soakas, ac kalmen pupulyuk lun mwet lalmwetmet.
kuti azimvetsa miyambi ndi mafanizo, mawu a anthu anzeru ndi mikuluwiko.
7 Sangeng sin LEUM GOD pa mutaweyen etauk. Mwet lalfon uh pilesru lalmwetmet, ac srunga suk etauk.
Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru. Zitsiru zimanyoza nzeru ndi malangizo.
8 Tulik nutik, lohng kas in luti lun papa tomom ac nina kiom.
Mwana wanga, mvera malangizo a abambo ako ndipo usakane mawu okuwongolera a amayi ako.
9 Mwe luti lalos uh ac mwe nawu moul lom oana sie mwe yun nu fin sifom, ku sie mwe walwal nu inkwawom.
Ali ngati sangamutu yokongola ya maluwa pamutu pako ndiponso ali ngati mkanda mʼkhosi mwako.
10 Tulik nutik, mwet koluk fin kwafe kom, nik kom wi.
Mwana wanga, ngati anthu oyipa afuna kukukopa usamawamvere.
11 Elos fin fahk, “Fahsru kut som kasriki sie mwet ah, ku kutu mwet wangin mwata, ac uniya mwe na pwar.
Akadzati, “Tiye kuno; tikabisale kuti tiphe anthu, tikabisalire anthu osalakwa;
12 Sahp pacl se kut ac sonolos elos ac moul na fokoko, tusruktu pacl se kut tari selos elos ac misa! (Sheol h7585)
tiwameze amoyo ngati manda, ndi athunthu ngati anthu otsikira mʼdzenje. (Sheol h7585)
13 Kut ac konauk mwe kasrup pus ac nwakla lohm sesr ke ma kut pisrala.
Motero tidzapeza zinthu zosiyanasiyana zamtengowapatali ndi kudzaza nyumba zathu ndi zolanda;
14 Fahsru wi kut. Kut ac kitalik ma nukewa in oana sie nu sesr kewa.”
Bwera, chita nafe maere, ndipo tidzagawana chuma chathu tonse.”
15 Tulik nutik, nimet wi mwet ouinge uh. Fahla lukelos.
Mwana wanga, usayende nawo pamodzi, usatsagane nawo mʼnjira zawozo.
16 Elos rarala in oru ma koluk. Elos akola pacl nukewa in akmas.
Iwowatu amangofuna zoyipa zokhazokha, amathamangira kukhetsa magazi.
17 Tia wo in akoo sie sruhf, ke won se ma kom ke sruokya uh el tu na liye,
Nʼkopanda phindu kutchera msampha mbalame zikuona!
18 mweyen mwet oru ouinge uh sifacna akoo mwe kwasrip nu selos, sie mwe kwasrip ma elos ac misa kac.
Koma anthu amenewa amangobisalira miyoyo yawo yomwe; amangodzitchera okha msampha!
19 Pacl nukewa, pisrapasr uh ac eisla moul lun mwet rapku — pa inge ma ac sikyak nu sin kutena mwet su moulkin moul sulallal.
Awa ndiwo mathero a anthu opeza chuma mwankhanza; chumacho chimapha mwiniwake.
20 Porongo! Lalmwetmet el pang inkanek uh ac in iwen kuka uh.
Nzeru ikufuwula mu msewu, ikuyankhula mokweza mawu mʼmisika;
21 El wowoyak ke mutunoa in siti uh, ac in acn nukewa mwet uh tukeni we:
ikufuwula pa mphambano ya misewu, ikuyankhula pa zipata za mzinda kuti,
22 “Mwet lalfon, kowos ac lungse in lalfon putaka? Kowos ac pwarkin in aksruksruki etauk uh nwe ngac? Ya kowos ac tiana lutlut in etu mau?
“Kodi inu anthu osachangamukanu, mudzakondwera ndi kusachangamuka mpaka liti? Nanga anthu onyogodola adzakondabe kunyogodola mpaka liti? Kapena opusa adzadana ndi nzeru mpaka liti?
23 Lohng ke pacl nga kai kowos. Nga ac sot kas in kasru wo ac oayapa etauk luk nu suwos.
Tamverani mawu anga a chidzudzulo. Ine ndikukuwuzani maganizo anga ndi kukudziwitsani mawu anga.
24 Nga tuh pangon kowos ac suli kowos in tuku, a kowos tia lungse lohng. Kowos likinsaiyu.
Popeza ndinakuyitanani koma inu munakana kumvera. Ndinayesa kukuthandizani koma panalibe amene anasamala.
25 Kowos pilesru kas in kasru luk nukewa, ac tia lungse nga in aksuwosye kowos.
Uphungu wanga munawunyoza. Kudzudzula kwanga simunakusamale.
26 Ouinge ke pacl kowos ac sun ongoiya, nga fah isrun kowos. Nga ac fah aksruksruki kowos ke pacl mwe aksangeng uh sikyak —
Ndiye inenso ndidzakusekani mukadzakhala mʼmavuto; ndidzakunyogodolani chikadzakugwerani chimene mumachiopacho.
27 pacl se ac tuku nu fowos oana paka, ac use mwe ongoiya oana sie eng na upa, ac kowos muta in keok ac waiok.
Chiwonongeko chikadzakugwerani ngati namondwe, tsoka likadzakufikirani ngati kamvuluvulu, mavuto ndi masautso akadzakugwerani.
28 Na kowos ac fah pang nu ke lalmwetmet, tuh nga ac tia topuk. Kowos ac sukyu yen nukewa, tuh kowos ac tia ku in koneyuyak.
“Tsono mudzandiyitana koma sindidzayankha; mudzandifunafuna, koma simudzandipeza.
29 Wanginna pacl kowos lohang nu ke etauk, ac pacl nukewa kowos srunga akos LEUM GOD.
Popeza iwo anadana ndi chidziwitso ndipo sanasankhe kuopa Yehova,
30 Kowos tiana lungse eis kas in kasru luk, ku porongo pacl nga aksuwosye kowos uh.
popeza iwo sanasamale malangizo anga ndipo ananyoza chidzudzulo changa.
31 Ke ma inge, kowos ac fah kosrani fal nu ke orekma lowos, ac pwapa koluk lowos ac tingilkowosi ac pwanang kowos maskin.
Tsono adzadya zipatso zoyenera mayendedwe awo ndi kukhuta ndi ntchito zimene anachita kwa ena.
32 Mwet selalkung uh misa ke sripen elos pilesru lalmwetmet. Mwet lalfon uh kunausyukla ke nunak in aksrikyaten lalos.
Pakuti anthu osachangamuka amaphedwa chifukwa cha kusochera kwawo, ndipo zitsiru zimadziwononga zokha chifukwa cha mphwayi zawo.
33 Tusruktu, kutena mwet su lohngyu fah muta in misla. Moul lal ac fah wo, ac el ac fah tia enenu in sangeng ke kutena ma.”
Koma aliyense wondimvera adzakhala mwa bata; adzakhala mosatekeseka posaopa chilichonse.”

< Soakas 1 >