< Soakas 3 >

1 Tulik nutik, nimet mulkunla ma nga luti nu sum. Esam ma nukewa ma nga fahk nu sum in oru.
Mwana wanga, usayiwale malangizo anga, mtima wako usunge malamulo anga.
2 Mwe luti luk ac fah akloesye moul lom ac akinsewowoye.
Ukatero zaka za moyo wako zidzachuluka ndipo udzakhala pa mtendere.
3 Nimet lela kulang ac inse pwaye in wanginla liki kom. Kapriya inkwawom, ac simusla insiom.
Makhalidwe ochitira ena chifundo ndi owonetsa kukhulupirika asakuchokere. Uwamangirire mʼkhosi mwako ngati mkanda ndi kuwalemba pa mtima pako.
4 Kom fin oru ouinge, kom ac fah ohi yurin God ac mwet uh.
Ukatero udzapeza kuyanja ndi mbiri yabwino pamaso pa Mulungu ndi anthu.
5 Lulalfongi LEUM GOD ke insiom kewa. Nimet lulalfongi etu lom sifacna.
Uzikhulupirira Yehova ndi mtima wako wonse ndipo usadalire nzeru zako za kumvetsa zinthu.
6 Esam LEUM GOD in ma nukewa kom oru, ac El ac fah akkalemye inkanek suwohs nu sum.
Pa zochita zako zonse uvomereze kuti Mulungu alipo, ndipo Iye adzawongola njira zako.
7 Nimet sifacna nunku mu kom arulana fas in lalmwetmet lom; akos LEUM GOD ac fahsr liki ma koluk.
Usamadzione ngati wa nzeru. Uziopa Yehova ndi kupewa zoyipa.
8 Kom fin oru ouinge, ac fah akkeye monum, ac sot ku nu sum.
Ukatero thupi lako lidzakhala la moyo wabwino ndi mafupa ako adzakhala olimba.
9 Akfulatye LEUM GOD ke mwe sang lom nu sel ke mwe kasrup lom, ac ke fahko se meet ke ima lom.
Uzilemekeza Yehova ndi chuma chako chonse; zokolola zonse zoyamba kucha uzilemekeza nazonso Yehova.
10 Kom fin oru ouinge, nien filma lom ac fah nwanala ke wheat, ac nien wain lom ac fah kahkkakla ke wain.
Ukatero nkhokwe zako zidzadzaza ndi zinthu zambiri, ndiponso mitsuko yako idzadzaza ndi vinyo.
11 Tulik nutik, nimet pilesru kas in kai lun LEUM GOD nu sum, a lohang nu kac ac eis mu mwe sensenkakin kom.
Mwana wanga usanyoze malangizo a Yehova, ndipo usayipidwe ndi chidzudzulo chake.
12 LEUM GOD El kaelos su El lungse, oana ke sie papa kai tulik su el insewowo kac.
Paja Yehova amadzudzula amene amamukonda, monga abambo achitira mwana amene amakondwera naye.
13 Insewowo mwet se su konauk lalmwetmet, ac su sun etauk.
Wodala munthu amene wapeza nzeru, munthu amene walandira nzeru zomvetsa zinthu,
14 Ma laesla kac yohk liki ma laesla ke silver, ac yohk sripa nu sum liki gold.
pakuti phindu la nzeru ndi labwino kuposa la siliva, phindu lakelo ndi labwino kuposanso golide.
15 Lalmwetmet el saok liki wek saok. Wangin kutena ma kom lungse ku in lumweyuk nu kac.
Nzeru ndi yoposa miyala yamtengowapatali; ndipo zonse zimene umazikhumba sizingafanane ndi nzeru.
16 Lalmwetmet uh ac akloesye moul lom, akkasrupye kom, ac oru in sunakinyuk kom.
Mʼdzanja lake lamanja muli moyo wautali; mʼdzanja lake lamanzere muli chuma ndi ulemu.
17 Inkanek lun lalmwetmet uh ac mwe engan nu sum, ac kol kom nu ke moul in misla.
Njira zake ndi njira zosangalatsa, ndipo mu njira zake zonse muli mtendere.
18 Lalmwetmet uh oana sak in moul nu selos su eisal, ac mwe insewowo nu selos su akfulatyal.
Nzeru ili ngati mtengo wopatsa moyo kwa oyigwiritsitsa; wodala munthu amene amayigwiritsa kwambiri.
19 LEUM GOD El orala faclu ke lalmwetmet lal, Ke etu lal El oakiya ma oan inkusrao.
Yehova anakhazikitsa dziko lapansi pogwiritsa ntchito nzeru. Anagwiritsanso ntchito nzeru zakudziwa bwino zinthu pamene ankakhazikitsa zakumwamba.
20 Lalmwetmet lal uh oru kof ye faclu in unonak, Ac pukunyeng uh in kahkunma af nu fin faclu.
Mwa nzeru zake Yehova anatumphutsa madzi kuchokera mʼnthaka ndiponso mitambo inagwetsa mvula.
21 Tulik nutik, sruokya ku liyaten, ac lohang in wo nu ke ma kom oru.
Mwana wanga usunge nzeru yeniyeni ndi khalidwe lomalingarira zinthu bwino. Zimenezi zisakuchokere.
22 Ma inge ac sot moul wo ac insewowo nu sum.
Zimenezi zidzakupatsa moyo, moyo wake wosangalatsa ndi wabwino ngati mkanda wa mʼkhosi.
23 Kom ac fah fahsr ke inkanek in misla, ac tiana tukulkul.
Choncho udzayenda pa njira yako mosaopa kanthu, ndipo phazi lako silidzapunthwa;
24 Kom ac fah tia sangeng ke kom motul, ac kom ac fah motul folosowosla ke fong uh.
pamene ugona pansi, sudzachita mantha; ukadzagona pansi tulo tako tidzakhala tokoma.
25 Kom ac tia sensen ke mwe fosrnga su ac sa sikyak, oana paka ma sun mwet koluk uh.
Usaope tsoka lobwera mwadzidzidzi kapena chiwonongeko chimene chidzagwera anthu oyipa,
26 LEUM GOD El ac karingin kom. El ac fah tia lela niom in sremla.
pakuti Yehova adzakulimbitsa mtima ndipo adzasunga phazi lako kuti lisakodwe mu msampha.
27 In pacl nukewa ma kom ku, kom in kasrelos su fal in eis kasru, ac tia sruokya ma wo lukelos.
Usaleke kuchitira zabwino amene ayenera kulandira zabwino, pamene uli nazo mphamvu zochitira zimenezi.
28 Nimet fahk nu sin mwet tulan lom in soano nu ke len tok ah, kom fin ku in kasrel ingena.
Usanene kwa mnansi wako kuti, “Pita, uchite kubweranso. Ndidzakupatsa mawa” pamene uli nazo tsopano.
29 Nimet akoo kutena ma ac tuh akkolukye mwet tulan lom; el muta siskom ac lulalfongi kom.
Usamukonzere chiwembu mnansi wako, amene anakhala nawe pafupi mokudalira.
30 Nimet akukuin nu sin sie mwet ke wangin sripa, fin wangin ma el oru in akkolukye kom.
Usakangane ndi munthu wopanda chifukwa pamene iye sanakuchitire zoyipa.
31 Nimet mwel ma lun mwet sulallal, ku nunkauk in oru oana elos oru,
Usachite naye nsanje munthu wachiwawa kapena kutsanzira khalidwe lake lililonse.
32 mweyen LEUM GOD El srunga mwet orekma koluk, a El insraelak nu sin mwet suwoswos.
Pakuti Yehova amanyansidwa ndi munthu woyipa koma amayanjana nawo anthu olungama.
33 Mwe selnga lun LEUM GOD oan fin lohm sin mwet koluk, a mwe insewowo lal oan fin lohm sin mwet suwoswos.
Yehova amatemberera nyumba ya munthu woyipa, koma amadalitsa nyumba ya anthu olungama.
34 El tiana lohang nu sin mwet inse fulat, a El kulang nu sin mwet pusisel.
Anthu onyoza, Iye amawanyoza, koma amakomera mtima anthu odzichepetsa.
35 Mwet lalmwetmet uh ac akfulatyeyuk, a mwet lalfon uh ac yokelik mwekin lalos.
Anthu anzeru adzalandira ulemu, koma zitsiru adzazichititsa manyazi.

< Soakas 3 >