< Oekyuk 33 >

1 Ma simla inge fahkak inen acn ma mwet Israel aktuktuk we tukun elos fahsr liki acn Egypt ke sruf lalos ye kolyuk lal Moses ac Aaron.
Malo otsatirawa ndi omwe Aisraeli anayima pa maulendo awo atatuluka mʼdziko la Igupto mʼmagulu awo motsogozedwa ndi Mose ndi Aaroni.
2 Moses el simusla inen kais sie acn ma elos tulokunak lohm nuknuk selos we, oana ma LEUM GOD El sapkin.
Mose analemba malo amene anayambira maulendo awo molamulidwa ndi Yehova. Maulendo awo ndi malo omwe anayambira ndi awa:
3 Mwet Israel elos som liki Egypt ke len aksingoul limekosr in malem se meet in yac, len se tukun Kufwen Alukela se oemeet. Ye karinginyuk lun LEUM GOD elos illa liki siti Rameses ye mutun mwet Egypt,
Aisraeli ananyamuka kuchokera ku Ramesesi pa tsiku la 15 la mwezi woyamba, itangotha Paska. Iwo anatuluka nayenda molimba mtima Aigupto onse akuona,
4 su pikin wounse mukul natulos ma LEUM GOD El uniya. LEUM GOD El oru ouinge in akkalemye lah El arulana ku liki god lun acn Egypt.
pamene ankayika maliro a ana awo oyamba kubadwa, omwe Yehova anawakantha pakati pawo chifukwa Yehova anaweruza milungu yawo.
5 Mwet Israel som liki acn Rameses ac tulokunak nien aktuktuk lalos Sukkoth.
Aisraeli atachoka ku Ramesesi, anamanga misasa yawo ku Sukoti.
6 Nien aktuktuk lalos akluo pa in acn Etham sisken yen mwesis.
Atachoka ku Sukoti anakamanga misasa yawo ku Etamu, mʼmbali mwa chipululu.
7 Liki acn sac elos folokla nu Pi Hahiroth, kutulap in Baal Zephon, ac aktuktuk apkuran nu Migdol.
Ndipo atachoka ku Etamu, anabwerera ku Pihahiroti, kummawa kwa Baala-Zefoni, ndipo anamanga misasa yawo pafupi ndi Migidoli.
8 Elos mukuila liki Pi Hahiroth ac fahsr sasla in Meoa Srusra nu in acn mwesis lun Shur. Tukun fahsr ke len tolu elos aktuktuk in acn Marah.
Atachoka ku Pihahiroti anadutsa mʼkati mwa nyanja kupita ku chipululu ndipo atayenda masiku atatu mʼchipululu cha Etamu, anamanga misasa yawo ku Mara.
9 Liki acn we elos som nu Elim ac aktuktuk we, mweyen oasr unon in kof singoul luo ac sak palm itngoul we.
Atachoka ku Mara anafika ku Elimu, kumene kunali akasupe a madzi khumi ndi awiri ndi mitengo ya migwalangwa 70 ndipo anamanga misasa yawo kumeneko.
10 Elos fahsr liki Elim ac aktuktuk apkuran nu ke Meoa Srusra.
Atachoka ku Elimu anakamanga misasa yawo mʼmbali mwa Nyanja Yofiira.
11 Acn in aktuktuk se lalos toko pa yen mwesis lun Sin.
Atachoka ku Nyanja Yofiira anakamanga misasa yawo mʼchipululu cha Sini.
12 Na toko elos aktuktuk Dophkah,
Atachoka ku chipululu cha Sini anakamanga ku Dofika.
13 ac toko in acn Alush,
Atachoka ku Dofika anakamanga misasa yawo ku Alusi.
14 ac toko in acn Rephidim, acn se ma wangin kof elos in nim we.
Atachoka ku Alusi anakamanga misasa yawo ku Refidimu, kumene kunalibe madzi woti anthu ndi kumwa.
15 Elos mukuiyak liki acn Rephidim ac som aktuktuk in acn mwesis lun Sinai.
Atachoka ku Refidimu anakamanga ku chipululu cha Sinai
16 Elos som liki acn we nu in acn Kibroth Hattaavah.
Atachoka ku chipululu cha Sinai anakamanga misasa yawo ku Kiburoti-Hataava.
17 Tok elos som ac aktuktuk in kais sie acn inge: Hazeroth,
Atachoka ku Kiburoti-Hataava anakamanga misasa yawo ku Heziroti.
18 Rithmah,
Atachoka ku Heziroti anakamanga ku Ritima.
19 Rimmon Perez,
Atachoka ku Ritima anakamanga ku Rimoni-Perezi.
20 Libnah,
Atachoka ku Rimoni-Perezi anakamanga ku Libina.
21 Rissah,
Atachoka ku Libina anakamanga ku Risa.
22 Kehelathah,
Atachoka ku Risa anakamanga ku Kehelata.
23 Eol Shepher,
Atachoka ku Kehelata anakamanga ku phiri la Seferi.
24 Haradah,
Atachoka ku phiri la Seferi anakamanga ku Harada.
25 Makheloth,
Atachoka ku Harada anakamanga ku Mekheloti.
26 Tahath,
Atachoka ku Mekheloti anakamanga ku Tahati.
27 Terah,
Atachoka ku Tahati anakamanga ku Tera.
28 Mithkah,
Atachoka ku Tera anakamanga ku Mitika.
29 Hashmonah,
Atachoka ku Mitika anakamanga ku Hasimona.
30 Moseroth,
Atachoka ku Hasimona anakamanga ku Moseroti.
31 Bene Jaakan,
Atachoka ku Moseroti anakamanga ku Beni Yaakani.
32 Hor Haggidgad,
Atachoka ku Beni Yaakani anakamanga ku Hori-Hagidigadi.
33 Jotbathah,
Atachoka ku Hori-Hagidigadi anakamanga ku Yotibata.
34 Abronah,
Atachoka ku Yotibata anakamanga ku Abirona.
35 Ezion Geber,
Atachoka ku Abirona anakamanga ku Ezioni-Geberi.
36 acn mwesis lun Zin (pa ingan acn Kadesh),
Atachoka ku Ezioni-Geberi anakamanga ku Kadesi, mʼchipululu cha Zini chimene ndi Kadesi.
37 ac Eol Hor, sisken na facl Edom.
Anachoka ku Kadesi ndi kukamanga ku phiri la Hori, mʼmalire mwa dziko la Edomu.
38 Aaron mwet tol el fanyak nu fin mangon Eol Hor, oana ke LEUM GOD El sapkin nu sel, ac el misa we ke len se oemeet in malem se aklimekosr ke yac akangngaul tukun mwet Israel elos illa liki acn Egypt.
Molamulidwa ndi Yehova, wansembe Aaroni anakwera ku phiri la Hori kumene anakamwalirira pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu, mʼchaka cha makumi anayi, Aisraeli atatuluka mʼdziko la Igupto.
39 Aaron el yac siofok longoul tolu ke el misa Fineol Hor.
Aaroni anamwalira pa phiri la Hori ali ndi zaka 123.
40 Tokosra lun Arad, su oan layen eir in acn Canaan, el lohngak lah mwet Israel apkuranme.
Mfumu ya Akanaani ya ku Aradi yomwe inkakhala ku Negevi kummwera kwa Kanaani, inamva kuti Aisraeli akubwera.
41 Mwet Israel elos mukuiyak liki Eol Hor ac aktuktuk Zalmonah.
Atachoka ku phiri la Hori anakamanga ku Zalimoni.
42 Na toko elos aktuktuk ke kais sie acn inge: Punon,
Atachoka ku Zalimoni anakamanga ku Punoni.
43 Oboth,
Atachoka ku Punoni anakamanga ku Oboti.
44 mahnum Abarim in acn Moab,
Atachoka ku Oboti anakamanga ku Iye-Abarimu.
45 Dibon Gad,
Atachoka ku Iye-Abarimu anakamanga ku Diboni Gadi.
46 Almon Diblathaim,
Atachoka ku Diboni Gadi anakamanga ku Alimoni-Dibulataimu.
47 Fineol Abarim, apkuran nu Fineol Nebo,
Atachoka ku Alimoni-Dibulataimu anakamanga mʼmapiri a Abarimu, pafupi ndi Nebo.
48 ac in acn tupasrpasr Moab su oan layen kutulap in Infacl Jordan tulanang Jericho,
Atachoka ku mapiri a Abarimu anakamanga ku zigwa za Mowabu mʼmbali mwa Yorodani moyangʼanana ndi Yeriko.
49 inmasrlon Beth Jeshimoth na nwe infahlfal Acacia in acn mwesis lun Moab.
Ali ku zigwa za Mowabu anamanga mʼmbali mwa Yorodani kuchokera ku Beti-Yesimoti mpaka ku Abeli-Sitimu.
50 In acn mwesis lun Moab sisken Infacl Jordan tulanang acn Jericho, LEUM GOD El kaskas nu sel Moses ac fahk,
Pa zigwa za Mowabu, mʼmbali mwa Yorodani moyangʼanana ndi ku Yeriko, Yehova anawuza Mose kuti,
51 “Kaskas nu sin mwet Israel, ac fahk nu selos: Pacl se kowos fahsr alukela Infacl Jordan ac utyak nu in facl Canaan,
“Nena kwa Aisraeli kuti, ‘Pamene muwoloka Yorodani kulowa mʼdziko la Kanaani,
52 kowos in lusak mwet nukewa we. Kunausla ma sruloala lalos nukewa — ma orekla ke eot ac ma orekla ke osra — wi acn in alu lalos nukewa.
mukathamangitse nzika zonse za mʼdzikomo pamaso panu. Mukawononge mafano awo onse a miyala ndi osula ndi malo awo achipembedzo.
53 Sruokya facl sac ac oakwuki we, mweyen nga sot acn we tuh in ma suwos.
Mukalande dzikolo ndi kukhalamo chifukwa ndakupatsani dziko limenelo kuti mukhalemo.
54 Kitalik acn we ke fa, nu sin sruf ac sou lowos nukewa. Sang ipin acn ma yohk nu sin sruf ma yohk, ac ipin acn ma srik nu sin sruf ma srik.
Mukagawane dzikolo pochita maere monga mwa mafuko anu. Kwa omwe ali ambiri, cholowa chambiri, ndipo amene ali ocheperapo, chocheperanso. Chilichonse chimene chidzawagwere iwo mwa maere chidzakhala chawo. Mukaligawane monga mwa mafuko a makolo anu.
55 Kowos fin tia lusla mwet nukewa su muta we, na mwet lula uh ac fah arulana aklokoalokye kowos, oana kutkut in atronmotowos, ku oana sak ma oasr otoh kac inpupowos, na tok elos ac foroht lain kowos.
“‘Koma ngati simukathamangitsa nzika zimene zili mʼdzikomo, amene mukawalole kukhalamo adzakhala ngati zisonga mʼmaso mwanu ndi ngati minga mʼmbali mwanu. Adzakubweretserani mavuto mʼdziko limene mudzakhalemolo.
56 Kowos fin tia luselosla, na nga ac kunauskowosla oana ke nga akoo in kunauselosla.”
Ndipo pamenepo ndidzachitira inu zomwe ndinaganiza kuwachitira iwowo.’”

< Oekyuk 33 >