< Nehemiah 8 >

1 Ke malem se akitkosr mwet Israel nukewa elos okaki in acn selos. In len se omeet in malem sac elos nukewa fahsreni nu Jerusalem, ke acn in toeni lun mwet uh sisken na Mutunpot Kof. Elos siyuk sel Ezra, su mwet tol ac mwet sasla ke Ma Sap, tuh elan use book in Ma Sap ma LEUM GOD El tuh sang nu sin mwet Israel sel Moses.
Anthu onse anasonkhana ngati munthu mmodzi pabwalo limene lili patsogolo pa Chipata cha Madzi. Iwo anawuza mlembi Ezara kuti abwere ndi buku la malamulo a Mose limene Yehova anapereka kwa Aisraeli.
2 Ouinge Ezra el use nu yen mwet uh tukeni we — mukul, mutan, ac tulik su matwa fal in kalem kac.
Choncho pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri wansembe Ezara, anabwera ndi buku la malamulo ku msonkhano wa amuna, akazi ndi ana onse amene ankatha kumvetsa zinthu bwino.
3 Na el riti Ma Sap nu selos in acn se sisken mutunpot sac, mutawauk ke lututang nwe ke infulwen len, ac mwet nukewa arulana lohang nu kac.
Choncho Ezara anawerenga bukulo atayangʼana bwalo la Chipata cha Madzi kuyambira mmawa mpaka masana pamaso pa amuna, akazi ndi onse amene ankamvetsa bwino zinthu. Ndipo anthu onse anatchera khutu kuti amve malamulowo.
4 Ezra el tuyak fin sie acn fulat orekla ke sak, ma musaiyukla nu ke toeni sac. Mwet inge tu siskal layen layot: Mattithiah, Shema, Anaiah, Uriah, Hilkiah, ac Maaseiah; ac mwet inge tu siskal layen lasa: Pedaiah, Mishael, Malchijah, Hashum, Hashbaddanah, Zechariah, ac Meshullam.
Mlembi Ezara anayimirira pa nsanja ya mitengo imene anthu anamanga chifukwa cha msonkhanowu. Ku dzanja lake lamanja kunayimirira Matitiya, Sema, Anaya, Uriya, Hilikiya ndi Maaseya, ndipo kudzanja lake lamanzere kunali Pedaya, Misaeli, Malikiya, Hasumu, Hasibadana, Zekariya ndi Mesulamu.
5 Ke Ezra el tu in acn sac, fulat liki mwet uh, elos nukewa suilya na. Ke el ikasla book sac, elos nukewa tuyak.
Tsono Ezara anatsekula buku, akuona popeza anayima pa nsanja. Pamene anafutukula bukulo anthu onse anayimirira.
6 Ezra el fahk, “Kaksakin LEUM GOD, God fulat!” Mwet nukewa kolak paolos nu lucng ac topuk, “Amen! Amen!” Na elos sikukmutuntei ac faksufi in alu.
Ezara anatamanda Yehova, Mulungu wamkulu, ndipo anthu onse anakweza manja awo ndi kuyankha kuti, “Ameni, ameni.” Pambuyo pake onse anaweramitsa pansi mitu yawo napembedza Yehova akanali chizolikire choncho.
7 Na elos tuyak, ac mwet Levi inge aketeya Ma Sap uh nu selos: Jeshua, Bani, Sherebiah, Jamin, Akkub, Shabbethai, Hodiah, Maaseiah, Kelita, Azariah, Jozabad, Hanan ac Pelaiah.
Anthuwo atayimiriranso Alevi awa: Yesuwa, Bani, Serebiya, Yamini, Akubu, Sabetayi, Hodiya, Maaseya, Kerita, Azariya, Yozabadi, Hanani ndi Pelaya anawathandiza kuti amvetse bwino malamulowo.
8 Elos lungasla Ma Sap lun God ac aketeya tuh mwet uh in ku in kalem kac.
Iwo anawerenga buku la malamulo a Mulungu momveka bwino ndi kutanthauzira mawuwo kuti anthu amvetse bwino zowerengedwazo.
9 Ke mwet uh lohng ac kalem ke ma oakwuk in Ma Sap elos in oru, arulana purakak insialos ac elos mutawauk in tung. Ouinge Nehemiah su governor, ac Ezra su mwet tol ac mwet sasla ke Ma Sap, ac mwet Levi su aketeya ke Ma Sap, elos fahk nu sin mwet nukewa, “Len se inge mutal nu sin LEUM GOD lowos. Ouinge kowos in tia asor ac tung.
Tsono bwanamkubwa Nehemiya pamodzi ndi wansembe ndi mlembi Ezara komanso Alevi amene amaphunzitsa anthu anati kwa anthu onse, “Lero ndi tsiku lopatulika kwa Yehova Mulungu wanu. Musakhale ndi chisoni ndipo musalire.” Anayankhula choncho popeza anthu onse ankalira atamva mawu a buku la malamulo lija.
10 Inge kowos som nu acn suwos ac orek kufwa. Kite mongo nowos ac wain nu selos su tia fal yoro. Len se inge mutal nu sin Leum lasr, ke ma inge nikmet asor. Inse engan su LEUM GOD El sot nu suwos, ac fah akkeye kowos.”
Nehemiya anatinso, “Pitani, kachiteni phwando ku nyumba ndipo mukawagawireko ena amene alibe kanthu kalikonse popeza lero ndi tsiku lopatulika kwa Yehova. Musakhale ndi chisoni, pakuti chimwemwe cha Yehova ndiye mphamvu yanu.”
11 Mwet Levi elos forfor inmasrlon mwet uh ac akmisyelos, ac fahk tuh elos in tia asor ke len mutal ouinge.
Alevi anakhalitsa bata anthu onse powawuza kuti, “Khalani chete, pakuti lero ndi tsiku lopatulika ndipo musakhale ndi chisoni.”
12 Na mwet nukewa folokla nu yen selos ac arulana engan ke elos mongo ac nim, ac elos kite ma oasr yorolos nu sin mwet saya, mweyen elos kalem ke ma ritiyuk nu selos.
Anthu onse anachoka kupita kukadya ndi kumwa. Chakudya china anatumiza kwa anzawo. Choncho panali chikondwerero chachikulu popeza tsopano anali atamvetsa bwino mawu a Mulungu amene anawawerengera ndi kuwafotokozerawo.
13 Len se tok ah, sifen sou oayapa mwet tol ac mwet Levi elos som nu yorol Ezra in lutlut ke ma aketeyuki in Ma Sap.
Mmawa mwake atsogoleri a mabanja pamodzi ndi ansembe ndi alevi anasonkhana kwa Ezara, mlembi wa malamulo kuti aphunzire mawu a malamulowo.
14 Elos konauk tuh Ma Sap, su LEUM GOD El akkalemye sel Moses, sapkakin tuh mwet Israel in muta in iwen aktuktuk ke pacl in Kufwa lun Iwen Aktuktuk.
Tsono anapeza kuti zinalembedwa mʼbuku la malamulo kuti Yehova analamula kudzera mwa Mose kuti Aisraeli azikhala mʼzithando pa nthawi yonse ya chikondwerero cha mwezi wachisanu ndi chiwiri.
15 Ouinge elos sang kas inge in sulkakinyukelik in acn Jerusalem ac siti lulap ac siti srisrik in acn saya, ac fahk, “Kowos som nu fineol uh ac use kutu lesak pine, lesak olive, lesak myrtle, lesak palm ac kutu pac lesak saya ma ungung, in sang orek iwen aktuktuk, fal nu ke ma simla in Ma Sap.”
Choncho analengeza ndi kufalitsa mʼmizinda yawo yonse ndi mu Yerusalemu kuti, “Pitani ku phiri mukadule nthambi za mtengo wa olivi, za mtengo wa olivi wa kutchire, za mtengo wa mchisu, za mtengo wa mgwalangwa ndiponso za mitengo ina ya masamba, zomangira zithando monga zalembedweramu ndi kubwera nazo.”
16 Ouinge mwet uh use lesak uh ac orala iwen aktuktuk ke acn tupasrpasr fin lohm selos ac likinum selos, oayapa in kalkal lun Tempul, ac ke acn in toeni lun mwet uh sisken Mutunpot Kof ac sisken Mutunpot Ephraim.
Choncho anthu anapita kukatenga nthambi ndipo aliyense anadzimangira misasa pa denga ya nyumba yake, mʼmabwalo awo, mʼmabwalo a Nyumba ya Mulungu, mʼbwalo la pa Chipata cha Madzi ndiponso mʼbwalo la pa Chipata cha Efereimu.
17 Mwet nukewa su foloko liki sruoh elos orala iwen aktuktuk ac muta loac. Pacl se oemeet orekla ouiya se inge tukun pacl lal Joshua wen natul Nun, ac mwet nukewa arulana pirikyukyak ac engan.
Gulu lonse la anthu limene linabwera ku ukapolo linamanga misasa ndipo linakhala mʼmenemo. Kuyambira nthawi ya Yoswa mwana wa Nuni mpaka tsiku limenelo nʼkuti Aisraeli asanachitepo zimenezi. Choncho panali chimwemwe chachikulu.
18 Elos riti kais sie ip ke Ma Sap lun God ke len nukewa, mutawauk na ke len se oemeet lun kufwa ah nwe ke safla. Elos orek akfulat ke len itkosr. Ke len se akoalkosr elos oru sie tukeni in aksaf, fal nu ke oakwuk lun Ma Sap.
Tsiku ndi tsiku, kuyambira tsiku loyamba mpaka lomaliza, Ezara ankawerenga buku la malamulo a Mulungu. Anthu anachita chikondwerero masiku asanu ndi awiri. Pa tsiku lachisanu ndi chitatu panachitika msonkhano potsata buku la malamulo lija.

< Nehemiah 8 >