< Joel 2 >

1 Ukya mwe ukuk in okasak mwet uh Fineol Zion, inging mutal lun God. Kowos mwet Judah in rarrar! Len lun LEUM GOD apkuranme.
Lizani lipenga mu Ziyoni. Chenjezani pa phiri langa loyera. Onse okhala mʼdziko anjenjemere, pakuti tsiku la Yehova likubwera, layandikira;
2 Ac fah sie len lohsrlosr ac ohk, Sie len nukla ke pukunyeng sroalsroal. Un locust uh sikme oana un mwet mweun, Oana lohsr matoltol lohsreya fineol uh. Soenna sikyak kain ouiya inge meet, Ac fah wangin pac tok.
tsiku la mdima ndi chisoni, tsiku la mitambo ndi la mdima wandiweyani. Ngati mʼbandakucha umene wakuta mapiri, gulu lalikulu ndi la ankhondo amphamvu likubwera, gulu limene nʼkale lomwe silinaonekepo ngakhale kutsogolo kuno silidzaonekanso.
3 Elos kangla ma kap fin acn uh oana in e uh pa esukla. Meet liki elos tuku, acn uh oana Ima Eden, Tukun elos som, acn uh mwesisla. Wangin ma ku in kaingla lukelos.
Patsogolo pawo moto ukupsereza, kumbuyo kwawo malawi amoto akutentha zinthu. Patsogolo pawo dziko lili ngati munda wa Edeni, kumbuyo kwawo kuli ngati chipululu, kulibe kanthu kotsalapo.
4 Elos oana horse uh; Elos kasrusr oana horse in mweun uh.
Maonekedwe awo ali ngati akavalo; akuthamanga ngati akavalo ankhondo.
5 Na ke elos srosro fin mangon eol uh, Elos erarak oana kusen chariot; Elos kisassas oana mah pao ke ac firir uh. Elos takla oana un mwet mweun lulap ma akola nu ke mweun.
Akulumpha pamwamba pa mapiri ndi phokoso ngati la magaleta, ngati moto wothetheka wonyeketsa ziputu, ngati gulu lalikulu la ankhondo lokonzekera nkhondo.
6 Ke elos sikla, mwet nukewa tuninfongla; Mutun mwet nukewa fasrfasrla.
Akangowaona, anthu a mitundu ina amazunzika mu mtima; nkhope iliyonse imagwa.
7 Elos anwuk oana mwet mweun; Elos fanuk pot uh oana solse uh. Elos nukewa fahsr suwohs nu meet Ac tia kuhfla nu saya,
Amathamanga ngati ankhondo; amakwera makoma ngati asilikali. Onse amayenda pa mizere, osaphonya njira yawo.
8 Ac tia pac asinuki nu sin sie sin sie. Elos fahsryang na alukela kutena mwe kutong nu selos, Ac wangin ma ku in tulokunulosi.
Iwo sakankhanakankhana, aliyense amayenda molunjika. Amadutsa malo otchingidwa popanda kumwazikana.
9 Elos yuyak nu in siti uh; Elos fanukya pot uh; Elos fanyak nu fin lohm uh Ac utyak ke winto uh oana mwet pisrapasr uh.
Amakhamukira mu mzinda, amathamanga mʼmbali mwa khoma. Amakwera nyumba ndi kulowamo; amalowera pa zenera ngati mbala.
10 Faclu usrusryak ke elos fahsr nu meet; Ac yen engyeng uh rarrar. Faht uh ac malem uh lohsrlosrani, Ac itu uh tila saromrom.
Patsogolo pawo dziko limagwedezeka, thambo limanjenjemera, dzuwa ndi mwezi zimachita mdima, ndipo nyenyezi zimaleka kuwala.
11 LEUM GOD El ac sapsap nu sin un mwet mweun lal oana pusren pulahl. Un mwet mweun su aksol Arulana pukanten ac fokoko. Ac fuka lupan mwe aksangeng ke len lun LEUM GOD! Su ac fah ku in painmoulla?
Yehova amabangula patsogolo pawo, gulu lake lankhondo ndi losawerengeka, ndipo amphamvu ndi amene amamvera kulamula kwake. Tsiku la Yehova ndi lalikulu; ndi loopsa. Ndani adzapirira pa tsikulo?
12 LEUM GOD El fahk, “Nwe ouinge, kowos srakna ku in auliyak Ke lalo, tung, ac mwemelil, Ac foloko nu yuruk.
“Ngakhale tsopano, bwererani kwa Ine ndi mtima wanu wonse posala zakudya ndi kukhetsa misozi,” akutero Yehova.
13 Lela inse musalla lowos in akkalemye asor lowos; Seya nuknuk mukena srakna sufal.” Foloko nu yurin LEUM GOD lowos. El kulang ac sessesla ke pakoten. El mongfisrasr ac El karinganang wuleang lal. Pacl nukewa El akola in nunak munas ac tia sa in kai.
Ngʼambani mtima wanu osati zovala zanu. Bwererani kwa Yehova Mulungu wanu, pakuti Iye ndi wokoma mtima ndi wachifundo, wosakwiya msanga ndi wachikondi chochuluka, ndipo amaleka kubweretsa mavuto.
14 Sahp LEUM GOD lowos El ac aolla nunak lal, Ac akinsewowoye kowos ke fokin ima puspis. Na kowos fah ku in sifil kisakin wheat ac wain nu sel.
Akudziwa ndani? Mwina adzasintha maganizo nʼkutimvera chisoni, nʼkutisiyira madalitso, a chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa kwa Yehova Mulungu wanu.
15 Ukya mwe ukuk Fineol Zion; Sapkin in oasr sie tukeni lulap, ac mwet nukewa in lalo.
Lizani lipenga mu Ziyoni, lengezani tsiku losala zakudya, itanitsani msonkhano wopatulika.
16 Eisani mwet nukewa nu sie; Akoelosla nu ke sie tukeni mutal. Usani mwet matu, Oayapa tulik srisrik Ac tulik fusr. Finne mwet ma tufahna payuk an, Elos in filiya lohm selos ac wi pac tuku.
Sonkhanitsani anthu pamodzi, muwawuze kuti adziyeretse; sonkhanitsani akuluakulu, sonkhanitsani ana, sonkhanitsani ndi oyamwa omwe. Mkwati atuluke mʼchipinda chake, mkwatibwi atuluke mokhala mwake.
17 Mwet tol su kulansupu LEUM GOD Inmasrlon loang mutal ac acn in utyak lun Tempul, Enenu in tung ac pre: “O LEUM GOD, pakomuta mwet lom. Nikmet fuhlela mutunfacl saya in pilesrekut ac aksruksrukye kut Ke elos fahk, ‘Pia God lowos an?’”
Ansembe amene amatumikira pamaso pa Yehova, alire pakati pa guwa lansembe ndi khonde la Nyumba ya Yehova. Azinena kuti, “Inu Yehova, achitireni chifundo anthu anu. Musalole kuti cholowa chanu chikhale chinthu chonyozeka, kuti anthu a mitundu ina awalamulire. Kodi nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina amanena kuti, ‘Ali kuti Mulungu wawo?’”
18 Na LEUM GOD El sifil akkalemye nunak lal nu ke acn uh, Ac sifil pakomuta mwet lal.
Pamenepo Yehova adzachitira nsanje dziko lake ndi kuchitira chisoni anthu ake.
19 El topuk pre lalos ac fahk, “Inge nga fah sot nu suwos, Wheat, wain ac oil in olive, Ac kowos ac fah mut. Mutanfahl saya ac fah tia sifil aksruksrukye kowos.
Yehova adzawayankha kuti, “Ine ndikukutumizirani tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta ndipo mudzakhuta ndithu; sindidzakuperekaninso kuti mukhale chitonzo kwa anthu a mitundu ina.
20 Nga fah kunauselik un mwet mweun matol se ma tuku epang me, Ac fah lusla kutu selos nu yen mwesis. U se ma fahsr meet ah, ac ukohkyak nu in Meoa Misa, U se ma fahsr etok ah, ac ukohkyak nu in Meoa Mediterranean. Mano misa lalos ac fohlelana acn uh. Nga fah kunauselosla ke sripen ma nukewa ma elos oru nu suwos.
“Ine ndidzachotsa ankhondo akumpoto kuti apite kutali ndi inu, kuwapirikitsira ku dziko lowuma ndi lachipululu, gulu lawo lakutsogolo ndidzalipirikitsira ku nyanja ya kummawa ndi gulu lawo lakumbuyo, ku nyanja ya kumadzulo. Ndipo mitembo yawo idzawola, fungo lake lidzamveka.” Zoonadi Yehova wachita zinthu zazikulu.
21 “Acn inima uh, nikmet sangeng, A kowos in engan ac insewowo Ke ma nukewa LEUM GOD El oru nu suwos.
Iwe dziko usachite mantha; sangalala ndipo kondwera. Zoonadi Yehova wachita zinthu zazikulu.
22 Kosro inimae, nikmet sangeng. Insroan mah uh srunak folfol; Sak uh isus fahko, Ac arulana pus fokin fig ac grape.
Inu nyama zakuthengo, musachite mantha, pakuti msipu wa ku chipululu ukuphukira. Mitengo ikubala zipatso zake; mitengo ya mkuyu ndi mpesa ikubereka kwambiri.
23 “Mwet Zion, kowos in insewowo, Ac engankin ma LEUM GOD lowos El oru nu suwos. El sot lupan af fal nu suwos ke pacl la. El supweya af se meet ke pacl in taknelik, Ac af se tok ke pacl in kosrani, oana meet ah.
Inu anthu a ku Ziyoni sangalalani, kondwerani mwa Yehova Mulungu wanu, pakuti wakupatsani mvula yoyambirira mwachilungamo chake. Iye wakutumizirani mivumbi yochuluka, mvula yoyambirira ndi mvula ya nthawi ya mphukira, monga poyamba paja.
24 Nien sisi kulun wheat fah sessesla ke wheat, Luf sisken acn in orek wain fah kahkkakla ke wain ac oil in olive.
Pa malo opunthira padzaza tirigu; mʼmitsuko mudzasefukira vinyo watsopano ndi mafuta.
25 Nga fah folokonot ma lowos ma tuh musalla Ke yac ma u in locust uh tuh kangla fokin ima lowos. Nga pa tuh supwama u in locust matol ingan in lain kowos.
“Ine ndidzakubwezerani zonse zimene zinawonongedwa ndi dzombe, dzombe lalikulu ndi dzombe lalingʼono, dzombe lopanda mapiko ndi dzombe lowuluka; gulu langa lalikulu la nkhondo limene ndinalitumiza pakati panu.
26 Inge ac fah pukanten ma kowos in kang ac kowos fah kihp. Kowos fah kaksakin LEUM GOD lowos, Su tuh oru ma usrnguk inmasrlowos. Mwet luk ac fah tia sifilpa akmwekinyeyuk.
Mudzakhala ndi chakudya chambiri, mpaka mudzakhuta, ndipo mudzatamanda dzina la Yehova Mulungu wanu, amene wakuchitirani zodabwitsa; ndipo anthu anga sadzachitanso manyazi.
27 Na mwet Israel, kowos fah etu lah nga oasr inmasrlowos, Ac lah nga, LEUM GOD, pa God lowos, Ac wangin pac sie sayuk. Mwet luk ac fah tiana sifilpa aksruksrukyeyuk.
Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndili mu Israeli, kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu, ndi kuti palibenso wina; ndipo anthu anga sadzachitanso manyazi.
28 “Tukun ma inge, nga fah okoala ngunik nu fin mwet nukewa: Wen nutuwos ac acn nutuwos fah sulkakin kas luk, Mukul matu lowos fah mweme, Ac mukul fusr lowos fah liye aruruma.
“Ndipo patapita nthawi, ndidzakhuthulira Mzimu wanga pa anthu onse. Ana anu aamuna ndi ana anu aakazi adzanenera, nkhalamba zanu zidzalota maloto, anyamata anu adzaona masomphenya.
29 In pacl sac nga fah okoala ngunik Nu fin mwet kulansap pac, kewana mukul ac mutan.
Ngakhalenso pa antchito anga aamuna ndi aakazi ndidzakhuthulira Mzimu wanga masiku amenewo.
30 “Nga fah oru ma sakirik yen engyeng uh ac fin faclu In fahkak ke len sac. Ac fah oasr srah sororla, ac firir lun e, ac pukunyeng in kulasr.
Ndidzaonetsa zodabwitsa mlengalenga ndi pa dziko lapansi, ndizo magazi, moto ndi utsi watolotolo.
31 Faht uh ac fah lohsrla, Ac malem ac fah srusrala oana srah Meet liki len lulap ac aksangeng lun LEUM GOD ac tuku.
Dzuwa lidzadetsedwa ndipo mwezi udzaoneka ngati magazi lisanafike tsiku lalikulu ndi loopsa la Ambuye.
32 Tusruktu elos nukewa su siyuk kasru sin LEUM GOD ac fah moliyukla. Oana ke LEUM GOD El tuh fahk, ‘Kutu sin mwet su muta Fineol Zion ac in Jerusalem ac fah tia sun mwe ongoiya inge. Elos su nga sulela fah painmoulla.’”
Ndipo aliyense amene adzayitana pa dzina la Ambuye adzapulumuka; pakuti chipulumutso chidzakhala pa Phiri la Ziyoni ndi mu Yerusalemu, monga Yehova wanenera, pakati pa otsala amene Yehova wawayitana.

< Joel 2 >