< Joel 1 >

1 Pa inge kas lun LEUM GOD nu sel Joel, wen natul Pethuel.
Yehova anayankhula ndi Yoweli mwana wa Petueli.
2 Kowos mwet matu, lohng ma inge, Mwet Judah nukewa in porongo. Ku nu oasr kain ouiya inge sikyak in pacl lowos uh, Ku ke pacl lun papa tomowos?
Inu akuluakulu, imvani izi; mvetserani, nonse amene mumakhala mʼdziko. Kodi zinthu zokhala ngati izi zinayamba zaonekapo mʼnthawi yanu, kapena mʼnthawi ya makolo anu?
3 Srumun ma inge nu sin tulik nutuwos, Ac elos fah srumun nu sin tulik natulos, Su ac fah srumun pac nu sin fwil tok ah.
Muwafotokozere ana anu, ndipo ana anuwo afotokozere ana awo, ndipo ana awo adzafotokozere mʼbado winawo.
4 Fwilin locust puspis tuhwi tari fin ima lowos uh, Fahko ma lula tukun sie u in locust, u se toko ah kangla.
Chimene dzombe losamera mapiko lasiya dzombe lowuluka ladya; chimene dzombe lowuluka lasiya dzombe lalingʼono ladya; chimene dzombe lalingʼono lasiya chilimamine wadya.
5 Ngutalik ac tung, kowos mwet sruhi; Tung, kowos mwet lungse nimnim, Mweyen grape mwe orek wain sasu kunausyukla.
Dzukani, inu zidakwa ndipo mulire! Lirani mofuwula, inu nonse amene mumamwa vinyo; lirani mofuwula chifukwa cha vinyo watsopano, pakuti wachotsedwa pakamwa panu.
6 Sie un locust na matol utyak tari nu in acn sesr oana un mwet mweun. Elos arulana fokoko ac pusla, tia ku in oaoala. Wihselos arulana kosroh oana wihsen soko lion.
Mtundu wa anthu wathira nkhondo dziko langa, wamphamvu ndi wosawerengeka; uli ndi mano a mkango, zibwano za mkango waukazi.
7 Elos kunausla ima in grape lasr, Ac kontonauk sak fig sunasr. Elos ngalesla kulun sak uh Nwe ke na lah nukewa fasrfasrla.
Wawononga mphesa zanga ndipo wathyola mitengo yanga ya mkuyu. Wakungunula makungwa ake ndi kuwataya, kusiya nthambi zake zili mbee.
8 Mwet uh in tung, oana sie mutan fusr su mwemelil ke misa Lun mukul se el akola in payuk nu se.
Lirani ngati namwali wovala chiguduli, chifukwa cha mwamuna wa utsikana wake.
9 Wangin wheat ku wain kowos ac kisakin in Tempul uh. Mwet tol elos asor mweyen wangin ma elos ac kisakin nu sin LEUM GOD.
Chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa sizikuperekedwa ku nyumba ya Yehova. Ansembe akulira, amene amatumikira pamaso pa Yehova.
10 Ima uh sikiyukla, Ac infohk uh mwemelil Mweyen wheat uh kunausyukla, Grape uh masla, Ac sak olive uli.
Minda yaguga, nthaka yauma; tirigu wawonongeka, vinyo watsopano watha, mitengo ya mafuta yauma.
11 Kowos mwet ima in arulana asor, Kowos su karingin ima in grape in tung, Mweyen wheat ac barley — Aok, mwe yok nukewa kunanula.
Khalani ndi nkhawa, inu alimi, lirani mofuwula inu alimi a mphesa; imvani chisoni chifukwa cha tirigu ndi barele, pakuti zokolola za mʼmunda zawonongeka.
12 Ima grape ac sak fig nukewa uli; Sak nukewa ma isus fahko uli ac masla. Mwe akenganye mwet uh wanginla.
Mpesa wauma ndipo mtengo wamkuyu wafota; makangadza, kanjedza ndi mitengo ya apulosi, mitengo yonse ya mʼmunda yauma. Ndithudi chimwemwe cha anthu chatheratu.
13 Kowos mwet tol su kulansap ke loang uh, Nokomang nuknuk yohk eoa ac tung. Utyak nu in Tempul ac mwemelil fong fon! Wangin wheat ku wain in sang nu sin God lowos.
Inu ansembe, valani ziguduli ndipo lirani; lirani mofuwula, inu amene mumatumikira pa guwa lansembe. Bwerani, fundani ziguduli usiku wonse, inu amene mumatumikira pamaso pa Mulungu wanga; pakuti chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa sizikupezekanso mʼnyumba ya Mulungu wanu.
14 Sapkin in oasr sie tukeni lulap, Ac mwet nukewa in lalo. Pangoneni mwet kol Ac mwet Judah nukewa Nu in Tempul lun LEUM GOD lowos Ac pang nu sel!
Lengezani tsiku lopatulika losala zakudya, itanani msonkhano wopatulika. Sonkhanitsani akuluakulu ndi anthu onse okhala mʼdziko ku nyumba ya Yehova Mulungu wanu ndipo alirire Yehova.
15 Len lun LEUM GOD apkuranme, Len se ma God Kulana El ac kunausla ma nukewa. Fuka lupan sangeng ac rarrar ac sikyak ke len sac!
Kalanga ine tsikulo! Pakuti tsiku la Yehova layandikira; lidzabwera ngati chiwonongeko chochokera kwa Wamphamvuzonse.
16 Kut ngetang na liye ke ima lasr uh masla, ac wangin ma kut ku in oru. Wanginla pwar in Tempul lun God lasr.
Kodi chakudya chathu sichachotsedwa ife tikuona? Kodi mʼnyumba ya Mulungu wathu simulibe chimwemwe ndi chisangalalo?
17 Infohk uh paola ac fita uh masla. Wanginla wheat in oan ke nien filma, Ouinge lohm in filma uh musalla.
Mbewu zikunyala poti pansi ndi powuma. Nyumba zosungiramo zinthu zawonongeka; nkhokwe zapasuka popeza tirigu wauma.
18 Cow uh wowoyak ke keok lalos Mweyen wangin acn elos in mongo we. Un sheep uh wi pac keok.
Taonani mmene zikulirira ziweto; ngʼombe zikungoyenda uku ndi uku chifukwa zilibe msipu; ngakhalenso nkhosa zikusauka.
19 O LEUM GOD, nga pang nu sum, Mweyen ima uh ac insak uh paola ac masla, Oana in isisyak.
Kwa Inu Yehova ndilirira, pakuti moto wapsereza msipu wakuthengo, malawi amoto apsereza mitengo yonse ya mʼtchire.
20 Finne kosro lemnak elos wowoyak pac nu sum, Mweyen infacl uh paola.
Ngakhale nyama zakuthengo zikulirira Inu; timitsinje tonse taphwa ndipo moto wapsereza msipu wa kuthengo.

< Joel 1 >