< Job 7 >

1 “Moul lun mwet uh oana sie mwet mweun su akkohsyeyuk ye ma sap upa nu sel — Oana moul lun sie mwet ma kemkatu ke oru orekma toasr lun pao,
“Kodi munthu sakhala ndi ntchito yowawa pa dziko lapansi? Kodi masiku ake sali ngati munthu waganyu?
2 Oana sie mwet foko su kena mongla in acn lul uh; Ac oana sie mwet orekma su soano pacl in eis molin orekma lal.
Monga ngati kapolo wolakalaka mthunzi wa nthawi yamadzulo, kapena ngati munthu waganyu woyembekezera malipiro ake,
3 Malem nu ke malem, wanginna sripa nga in moul; Ac fong nu ke fong nga asor na.
choncho ine ndapatsidwa nthawi yongovutika pachabe, ndiponso usiku wamasautso wapatsidwa kwa ine.
4 Ke nga ona in motulla, pacl uh arulana sumui; Nga oanna pikpik fong fon se ac kena in tari lenelik.
Ndikamagona ndimaganiza kuti, ‘Kodi kucha liti?’ Usikuwo umatalika ndipo sindigona tulo mpaka mmawa.
5 Monuk sessesla ke wet; Afla ke kolo keke; Ac sroano koluk sororla ke faf keik uh.
Thupi langa ladzala mphutsi ndi zipsera, khungu langa langʼambika ndipo likutuluka mafinya.
6 Len luk uh somla ac wangin finsrak kac, Ac fahsr la uh mui liki kutap lun sie mwet tatu nwek.
“Masiku anga ndi othamanga kupambana makina wolukira nsalu, ndipo amatha wopanda chiyembekezo.
7 “O God, esam lah moul luk uh oana sie mong, Ac wanginla tari pwar luk.
Inu Mulungu kumbukirani kuti moyo wanga uli ngati mpweya; sindidzaonanso masiku achisangalalo.
8 Kom liyeyu inge, tusruktu kom ac fah tia sifil liyeyu tok. Kom fin ac sukyu, tuh nga nu somla tari.
Amene akundiona tsopano akundiona; mudzandifunafuna koma sindidzapezekanso.
9 Oana sie pukunyeng ac sarla ac wanginla, Ouinge sie mwet misa fah tiana sifil foloko; (Sheol h7585)
Monga mtambo umazimirira ndi kukanganuka, momwemonso munthu amene walowa mʼmanda sabwerera. (Sheol h7585)
10 Mwet nukewa ma etal meet ah, ac tia sifil esamul.
Iye sadzabweranso ku nyumba kwake ndipo onse omudziwa adzamuyiwala.
11 Ke ma inge, nga tia ku in tila kaskas! Nga kasrkusrak ac mwen insiuk. Enenu na nga in fahkla nunak luk uh.
“Nʼchifukwa chake ine sindidzakhala chete; ndidzayankhula mopsinjika mtima, ndidzadandaula mowawidwa mtima.
12 “Efu ku kom sap in taranyuk nga? Mea, kom nunku mu nga pa soko ma sulallal in meoa uh?
Kodi ine ndine nyanja kapena chirombo chamʼnyanja kuti inu mundiyikire alonda?
13 Nga ona ac srike ngan mongla; Nga sukok ma in lusrongla ngal keik uh.
Pamene ndikuganiza kuti ndidzapeza chitonthozo pa bedi panga ndipo pogona panga padzachepetsa madandawulo anga,
14 A kom — kom aksangengyeyu ke mweme; Ac supwama aruruma ac mweme na koluk
ngakhale nthawi imeneyo mumandiopseza ndi maloto ndi kundichititsa mantha ndi masomphenya,
15 Nwe ke na apkuran ngan ke in isasu kwawuk ngan misa, Liki nga in muta in mano keok se inge.
kotero kuti ndimalakalaka kudzikhweza kapena kufa, kupambana kupirira zowawa zimene ndikuzimva mʼthupi mwanga.
16 Nga fuhleak finsrak luk; nga totola ke moul muta uh. Tari fahla likiyu; wanginla sripen moul luk.
Ine ndatopa nawo moyo wanga; sindingakonde kukhala moyo nthawi zonse. Ndisiyeni ndekha pakuti moyo wanga ulibe tanthauzo.
17 “Efu ku kom oru mu yohk sripen mwet uh nu sum? Efu ku kom lohang nu ke ma el oru uh?
“Kodi munthu nʼchiyani kuti muzimuganizira chotere, kuti muzisamala zochita zake,
18 Kom tonel ke lotutang nukewa Ac srikal ke minit nukewa.
kuti muzimusanthula mmawa uliwonse ndi kumamuyesa nthawi yonse?
19 Mea, kom tia ku in ngetla likiyu ke kitin pacl Ngan ku in ukumya sronin oalik?
Kodi simudzaleka kumandizonda kuti ndipezeko mpata wopumula?
20 Ya kom keok ke ma koluk luk, kom su liyaung mwet kapir? Efu ku kom tungalyu oana in sie mwe akoalel lom? Mea, nga mwe toasr se na lom?
Ngati ine ndachimwa, ndachita chiyani kwa Inu, Inu wopenyetsetsa anthu? Chifukwa chiyani mwachititsa kuti ndikhale ngati choponyera chandamale chanu? Kodi ndasanduka katundu wolemera kwa Inu?
21 Mea, kom ac tiana nunak munas nu sik ke ma koluk luk nwe tok? Kom tiana ku in tulala ma sufal nga orala uh? Nga akuranna misa, pukpuki, Ac kom ac sukyu tuh na nga wanginla.”
Chifukwa chiyani simukundikhululukira zolakwa zanga ndi kundichotsera machimo anga? Pakuti posachedwa ndilowa mʼmanda; mudzandifunafuna ine koma simudzandionanso.”

< Job 7 >