< Job 42 >

1 Na Job el topuk LEUM GOD ac fahk,
Pamenepo Yobu anayankha Yehova kuti,
2 “LEUM GOD, nga etu lah ku nukewa oasr sum, Ac kom ku in oru ma nukewa kom lungse.
“Ndikudziwa kuti Inu mungathe kuchita zinthu zonse; chimene mufuna kuchita wina sangaletse konse.
3 Kom siyuk lah fuka tuh nga kusen siyuk ke lalmwetmet lom Ke wangin ma nga etu. Nga tuh kaskas ke ma su nga tia kalem kac, Ke ma usrnguk su yoklala nu sik in etu kac.
Munandifunsa kuti, ‘Kodi ndiwe yani amene ukufuna kusokoneza uphungu wanga ndi mawu opanda nzeru? Zoonadi ndinayankhula zimene sindinazimvetse, zinthu zodabwitsa kwambiri kwa ine zimene sindinazidziwe.
4 Kom tuh fahk mu nga in porongo ke kom ac sramsram, Ac in srike in topuk mwe siyuk lom uh.
“Inu munandiwuza kuti, ‘Mvetsetsa tsopano ndipo ndidzayankhula; ndidzakufunsa ndipo iwe udzandiyankhe.’
5 In pacl meet ah, ma na mwet uh fahk nu sik pa nga etu uh, Tuh pa inge, nga liye kom ke mutuk sifacna.
Ndinkangomva za Inu ndi makutu anga, koma tsopanonso ndakuonani ndi maso anga.
6 Ke ma inge nga arulana mwekin ke ma nukewa nga tuh fahk ah, Ac nga akkalemye auli luk ke nga muta inmasrlon kutkut ac apat.”
Nʼchifukwa chake ndi kuchita manyazi, ndikulapa podzithira fumbi ndi phulusa.”
7 Tukun LEUM GOD El kaskas nu sel Job tari, na El fahk nu sel Eliphaz, “Nga toasr sum ac sin mwet kawuk luo lom ingan, mweyen komtal tia fahk kas pwaye keik, oana ke Job, mwet kulansap luk, el oru.
Yehova atayankhula ndi Yobu mawu amenewa anawuza Elifazi wa ku Temani kuti, “Ine ndakukwiyira pamodzi ndi abwenzi ako awiri, chifukwa simunayankhule zabwino za Ine, monga mmene wayankhulira mtumiki wanga Yobu.
8 Inge, kom fahla ac us itkosr cow mukul ac itkosr sheep mukul an nu yorol Job, ac sang nu sel in mwe kisa lomtal nu sel. Job el ac fah pre keimtal, na nga fah lohng pre lal, ac tia aklusrongtenye komtal oana ma fal in orek nu sumtal. Komtal tuh tia fahk ma pwaye keik oana ke el oru ah.”
Kotero tsopano mutenge ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi kupita nazo kwa mtumiki wanga Yobu kuti mukapereke nsembe zopsereza. Mtumiki wanga Yobu adzakupemphererani, ndipo Ine ndidzalandira pemphero lake. Sindidzakuchitirani kanthu molingana ndi uchitsiru wanu. Inu simunayankhule zabwino za Ine, monga anayankhulira Yobu mtumiki wanga.”
9 Eliphaz, Bildad, ac Zophar oru ma LEUM GOD El fahk eltal in oru ah, na LEUM GOD El lohng pre lal Job.
Motero Elifazi wa ku Temani, Bilidadi wa ku Suki ndi Zofari wa ku Naama anachita zimene Yehova anawawuza ndipo Yehova anamvera pemphero la Yobu.
10 Na tukun Job el pre ke kawuk tolu lal ah, LEUM GOD El sifilpa folokonang mwe kasrup lal in pacl luo yohk liki meet ah.
Yobu atawapempherera abwenzi ake aja, Yehova anamubwezera chuma chake ndipo anamupatsa mowirikiza kuposa zomwe anali nazo kale.
11 Mwet lel Job ac mwet loul, wi mwet kawuk lal nukewa meet, elos tuku nu yorol Job ac welul orek kufwa in lohm sel ah. Elos fahk kas in akwoyal ac akkalemye pakomuta lalos, ke ma nukewa LEUM GOD El tuh akkeokyal kac. Kais sie selos sang mani ac ring gold se nu sel.
Abale ake ndi alongo ake onse, kuphatikizapo onse amene ankamudziwa kale, amabwera kwa iye nʼkudzadya naye chakudya mʼnyumba mwake. Iwo anamutonthoza ndi kumupepesa chifukwa cha mavuto onse amene Yehova analola kuti amugwere. Aliyense wa iwowa anamupatsa ndalama ndi mphete yagolide.
12 LEUM GOD El akinsewowoye tafun moul lal Job tok yohk liki na tafun moul lal meet ah. Oasr tausin singoul akosr sheep, tausin onkosr camel, tausin luo cow, ac tausin se ke donkey natul.
Yehova anadalitsa Yobu pa masiku ake otsirizawa kupambana poyamba paja. Iye anali ndi nkhosa 14,000, ngamira 6,000, ngʼombe zantchito 2,000 ndi abulu aakazi 1,000.
13 Oayapa oasr wen itkosr ac acn tolu sasu natul.
Anaberekanso ana aamuna asanu ndi awiri ndi ana aakazi atatu.
14 El sang inen mutan se ma matu ah Jemimah, ac acn se akluo ah pa Keziah, ac acn se ma srik ah Keren Happuch.
Mwana wake wamkazi woyamba anamutcha Yemima, wachiwiri anamutcha Keziya, wachitatu anamutcha Kereni Hapuki.
15 Wangin mutan fin faclu nufon kato oana acn natul Job inge. Papa tumaltal el tuh sang mwe usru laltal oapana ke el oru nu sin mukul natul ah.
Mʼdziko monsemo munalibe akazi okongola ngati ana a Yobu, ndipo abambo awo anawapatsa cholowa pamodzi ndi alongo awo.
16 Tukun ma inge, Job el tuh sifil moul ke lusen yac siofok angngaul, ac lusen pacl se inge oru el ku in liye fwilin tulik nutin natul, oayapa nutin nutin natul.
Zitachitika zimenezi, Yobu anakhala ndi moyo zaka 140. Iye anaona zidzukulu zake mpaka mʼbado wachinayi.
17 Na el misa ke el arulana matuoh.
Potsiriza, Yobu anamwalira ali nkhalamba ya zaka zochuluka kwambiri.

< Job 42 >