< Job 40 >

1 Na LEUM GOD El fahk nu sel Job:
Yehova anati kwa Yobu:
2 “Job, kom orek alein nu sin God Kulana. Mea, kom ac tari misla, ku kom akola in topukyu?”
“Kodi iwe ufuna kukangana ndi Wamphamvuzonse? Iwe amene unatsutsana ndi Mulungu umuyankhe Iyeyo!”
3 Na Job el topuk LEUM GOD ac fahk, Nga tuh fahk kas na lalfon. Mea nga ac sang topuk kom uh?
Pamenepo Yobu anayankha Yehova:
4 Nga ac tia sifil srike in fahk kutena ma.
“Ine sindili kanthu konse, kodi ndingathe kukuyankhani chiyani? Ndagwira pakamwa panga.
5 Kas luk ah alukela tari ma fal ngan fahk.”
Ndinayankhula kamodzi, koma pano ndilibe yankho, ndinayankha kawiri, koma sindiwonjezeranso mawu ena.”
6 Na, LEUM GOD El sifilpa kaskas nu sel Job liki eng upa sac me, ac fahk:
Ndipo Yehova anayankha Yobu mʼkamvuluvulu kuti,
7 “Tuyak oana sie mukul, Ac topuk mwe siyuk luk inge.
“Tsopano vala dzilimbe ngati mwamuna; ndikufunsa mafunso ndipo iwe undiyankhe.
8 Ya kom srike in akkalemye mu nga sesuwos — In tuh sutuu sik, a kom pa pwaye uh?
“Kodi iwe unganyoze chiweruzo changa cholungama? Kodi ungandidzudzule kuti iweyo ukhale wolungama?
9 Ya kuiyom oana ku luk? Ya pusrem ku in ngirngir in pulahl, oana pusrek?
Kodi uli ndi dzanja monga la Mulungu, ndipo mawu ako angagunde ngati mphenzi monga a Mulungu?
10 Fin pwaye, tuyak yunikomla ke pwengpeng ac fulat; Nuknukyang ke wal ac ke wolana.
Ngati zili choncho udzikometsere ndi ulemerero ndi kukongola, ndipo udziveke ulemu ndi ulemerero waufumu.
11 Ngetla liye mwet inse fulat uh; Okoaung kasrkusrak lom nu faclos ac akpusiselyalos.
Tsanula ukali wako wosefukirawo, uyangʼane aliyense wodzikuza ndipo umuchepetse,
12 Aok, liyalos akwoya, ac kilukunulosi nwe ten; Itungya mwet sulallal uh ingena yen elos tu we an.
Uyangʼane aliyense wodzikweza ndipo umutsitse, uwapondereze oyipa onse pamalo pomwe alilipo.
13 Puknulosi nufon ye fohk uh; Ac kaprelosi nu in facl sin mwet misa.
Onsewo uwakwirire pamodzi mfumbi; ukulunge nkhope zawo mʼmanda.
14 Na ac nga pa oemeet ac kaksakin kom uh, Ac fahkak lah kom kutangla ke ku lom sifacna.
Ukatero Ine ndidzakuvomereza kuti dzanja lako lamanja lakupulumutsadi.
15 “Nunkuwin ke kosro sulallal Behemoth; Nga pa oralla, ac nga pac pa orekomla. El mongo mah oana cow uh,
“Taganiza za mvuwu, imene ndinayipanga monga momwe ndinapangira iwe, ndipo imadya udzu ngati ngʼombe.
16 Tusruktu arulana yohk kuiyal, Ac yohk musul ke manol!
Mphamvu zake ndi zazikulu kwambiri, thupi lake ndi lanyonga kwambiri!
17 Pulal tuyak nu lucng oana soko sak cedar, Ac ku lun nial uh arulana yokla.
Mchira wake umayima tolotolo ngati mtengo wamkungudza; mitsempha ya ntchafu zake ndi yogwirana bwino.
18 Sri kacl uh ku oana osra bronze, Ac nial oana polo iron uh.
Mafupa ake ali ngati mapayipi amkuwa, nthiti zake zili ngati mipiringidzo yachitsulo.
19 “El pa nga tuh orala oemeet inmasrlon ma orakrak uh! Wanginna ma ku in kutangulla sayen El su oralla.
Mvuwuyo ndi yayikulu mwa zolengedwa za Mulungu, komatu mlengi wake amatha kuyiopseza ndi lupanga lake.
20 Mah ma el kang uh kap fineol, Yen kosro lemnak uh srital we.
Imapeza chakudya chake ku mtunda ndipo nyama zakuthengo zonse zimasewera pambali pake.
21 El ac oan ye sak ma oasr otoh, Ac wikwik ye loa in acn furarrar uh.
Imagona pa tsinde pa zitsamba za mipeta, imabisala mʼbango ndiponso pa thawale.
22 El ac wiklana oan ye lulin sak ma oasr otoh, Ac sak willow ma oan pe infacl uh.
Imaphimbika ndi mthunzi wazitsamba za mipeta; imazunguliridwa ndi misondozi ya mu mtsinje.
23 El tia sangeng ke asrasr lun infacl uh; Ac el ac oakwuk na ke Infacl Jordan ac fwela mutal.
Madzi a mu mtsinje akakokoma, sichita mantha, iyo sitekeseka, ngakhale madzi a mu Yorodani afike mʼkhosi mwake.
24 Su ac ku in aklohsryela mutal ac sruokilya? Ku sruokya infwacl ke sruhf uh?
Kodi alipo amene angathe kukola mvuwu ndi mbedza kapena kuyikola mu msampha?

< Job 40 >