< Jeremiah 4 >

1 LEUM GOD El fahk, “Mwet Israel, kowos fin lungse forla, kowos forma nu sik. Kowos fin pwaye nu sik ac sisla ma sruloala ma nga srunga ingan,
“Ngati mukufuna kubwerera, inu Aisraeli, bwererani kwa Ine,” akutero Yehova. “Chotsani mafano anu onyansa pamaso panga ndipo musasocherenso.
2 na ac tufah fal kowos in fulahk ke Inek. Mutunfacl nukewa fah siyuk sik in akinsewowoyalos, ac elos fah kaksakinyu.”
Muzilumbira mokhulupirika ndiponso mwa chilungamo kuti, ‘Pali Yehova wamoyo.’ Mukatero anthu a mitundu ina yonse adzandipempha kuti ndiwadalitse ndipo adzanditamanda.”
3 LEUM GOD El fahk nu sin mwet Judah ac Jerusalem, “Akfisrasryeak fohk ke acn ma soenna imaiyuk. Nimet yukwiya fita sunowos inmasrlon kokul uh.
Zimene Yehova akunena kwa anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu ndi izi: “Limani masala anu musadzale pakati pa minga.
4 Kowos mwet Judah ac Jerusalem, kowos in karinganang wuleang su nga, LEUM GOD lowos, orala inmasrlok ac kowos, ac kowos in sifacna kisakinkowosme nu sik. Kowos fin tia oru, na kasrkusrak luk ac tayak oana e, ke sripen ma koluk kowos oru. Ac fah firir ac wangin sie ku in konela.”
Dziperekeni nokha kwa Ine kuti munditumikire ndi mtima wanu wonse, inu anthu a ku Yuda ndi ku Yerusalemu. Muzichita zimenezi kuopa kuti mkwiyo wanga ungabuke ngati moto ndi kukutenthani, chifukwa cha ntchito zanu zoyipazo popanda wina wowuzimitsa.
5 Ukya mwe ukuk in sasla facl sac nufon! Sasa in yohk ac kalem! Fahkang nu sin mwet Judah ac Jerusalem In kaing nu ke siti ma potiyukyak ku.
“Lengeza ku Yuda ndi kulalikira mu Yerusalemu kuti, ‘Lizani lipenga mʼdziko lonse!’ Ndipo fuwulani kuti, ‘Sonkhanani! Tiyeni tithawire ku mizinda yotetezedwa!’
6 Srisrngi inkanek nu Zion! Kaing, kom in moulla! Nimet pahtlac! LEUM GOD El use ongoiya Ac kunausten lulap liki acn epang.
Kwezani mbendera kuyangʼana ku Ziyoni! Musachedwe, thawani kuti mupulumuke! Pakuti Ine ndikubweretsa chilango kuchokera kumpoto, kudzakhala chiwonongeko choopsa.”
7 Sie su kunausla mutunfacl uh mukuiyak tari, Oana soko lion otyak liki acn in wikwik lal. El tuku in kunausla Judah. Siti lun Judah ac oan musalla, Ac wangin mwet ac muta we.
Monga mkango umatulukira mʼngaka yake momwemonso wowononga mayiko wanyamuka ndi kutuluka ku mbuto yake. Watero kuti awononge dziko lanu. Mizinda yanu idzakhala mabwinja popanda wokhalamo.
8 Ke ma inge nokomang nuknuk yohk eoa, ac tung ac mwemelil Mweyen kasrkusrak upa lun LEUM GOD Tiana forla liki Judah.
Choncho valani ziguduli, lirani ndi kubuwula, pakuti mkwiyo waukulu wa Yehova sunatichokere.
9 LEUM GOD El fahk, “In len sac, tokosra ac mwet fulat ac fah wanginla pulaik lalos. Mwet tol ac arulana lut, ac mwet palu ac fah oela.”
“Pa tsiku limenelo, mfumu ndi nduna zake adzataya mtima, ansembe adzachita mantha kwambiri, ndipo aneneri adzathedwa nzeru,” akutero Yehova.
10 Na nga fahk, “LEUM GOD Fulatlana, kom arulana kiapwela mwet Jerusalem! Kom fahk mu ac fah oasr misla, a cutlass se pa oanna inkwawalos.”
Ndipo ine ndinati, “Haa, Ambuye Yehova, ndithu munawanyenga anthu awa pamodzi ndi Yerusalemu pamene munanena kuti, ‘Mudzakhala pa mtendere,’ chonsecho lupanga lili pakhosi pathu.”
11 Pacl se ac tuku ke ac fah fwackyang nu sin mwet Jerusalem lah sie eng na fol ac tuku yen mwesis uh nu yorolos. Ac fah tia sie eng srisrik mwe na okla kulun wheat —
Nthawi imeneyo anthu awa ndi Yerusalemu adzawawuza kuti, “Mphepo yotentha yochokera ku magomo a mʼchipululu ikuwomba pa anthu anga, osati mphepo yopeta kapena yoyeretsa;
12 a ac fah sie eng na upa supweyuku sin LEUM GOD. LEUM GOD sifacna pa akkalemye nununku lal nu sin mwet lal.
koma mphepo yamphamvu kwambiri yochokera kwa Ine. Tsono ndi Ineyo amene ndikuwaweruza.”
13 Ngetla liye — mwet lokoalok el tuku oana pukunyeng uh. Chariot in mweun lal oana eng fohru, ac horse natul uh mui liki eagle uh. We nu sesr! Kut ac sikiyukla!
Taonani, adani akubwera ngati mitambo, magaleta awo akubwera ngati kamvuluvulu, akavalo awo ndi aliwiro kupambana chiwombankhanga. Tsoka ilo! Tawonongeka!
14 O Jerusalem, ohlla ma koluk liki insiom tuh kom in ku in moul. Kom ac nunku nunak koluk uh nwe ngac?
Iwe Yerusalemu, tsuka mtima wako kuchotsa zoyipa kuti upulumuke. Kodi maganizo ako oyipawo udzakhala nawo mpaka liti?
15 Mwet utuk kas tuku Dan me, ac liki fineol in acn Ephraim, in sulkakinelik pweng koluk.
Pakuti amithenga akulalika mawu mʼdziko la Dani; akulengeza za masautso kuchokera ku mapiri a Efereimu.
16 Elos tuku in sensenkakin mutunfacl uh, ac in fahk nu sin Jerusalem lah mwet mweun elos tuku liki sie facl loessula. Mwet lokoalok inge fah wowoyak lain siti lun Judah
Iwo akuti, “Fotokozani zimenezi kwa anthu a mitundu ina, lengezani zimenezi mu Yerusalemu kuti, ‘Ankhondo akubwera kuchokera ku dziko lakutali, akufuwula ndi kudzazinga mizinda ya Yuda.
17 ac elos fah rauneak Jerusalem oana mwet san elos rauneak ima se, mweyen mwet lal uh orek likkeke lain LEUM GOD. LEUM GOD pa fahk ma inge.
Azinga Yerusalemu ngati anthu olondera munda, chifukwa Yerusalemu wandiwukira,’” akutero Yehova.
18 Judah, kom sifacna oru ma inge in tuku nu fom. Ouiyen moul lom ac orekma koluk lom pa pwanang keok se inge in fakiskomi sasla insiom.
“Makhalidwe anu ndi zochita zanu zakubweretserani zimenezi. Chimenechi ndiye chilango chanu. Nʼchowawa kwambiri! Nʼcholasa mpaka mu mtima!”
19 Nga waiok! Nga tia ku in muteng waiok se inge! Insiuk kihmkimyak ke sangeng! Nga tia ku in misla. Nga lohng mwe ukuk Ac pusren sasa lun mweun.
Mayo, mayo, ndikumva kupweteka! Aa, mtima wanga ukupweteka, ukugunda kuti thi, thi, thi. Sindingathe kukhala chete. Pakuti ndamva kulira kwa lipenga; ndamva mfuwu wankhondo.
20 Mwe ongoiya uh kalkalwen in sun kut; Facl sac nufon sikiyukla. Lohm nuknuk sesr kunausyukla in kitin pacl na. Mwe lisrlisr uh mihsasa uh.
Tsoka limatsata tsoka linzake; dziko lonse lasanduka bwinja. Mwadzidzidzi matenti athu awonongedwa, mwa kanthawi kochepa nsalu zake zotchinga zagwetsedwa.
21 Nga ac liye flag lun mweun nwe ngac, Ac lohng pusren mwe ukuk putaka?
Kodi ndikhale ndikuona mbendera ya nkhondo, ndi kumva kulira kwa lipenga mpaka liti?
22 LEUM GOD El fahk, “Mwet luk elos lalfon; Elos tia eteyu. Elos oana tulik lalfon; Wangin etauk lalos. Elos sasla ke oru ma koluk, A tiana etu in oru ma wo.”
Yehova akuti, “Anthu anga ndi zitsiru; iwo sandidziwa. Iwo ndi ana opanda nzeru; samvetsa chilichonse. Ali ndi luso lochita zoyipa, koma sadziwa kuchita zabwino.”
23 Nga ngetla liye faclu — wangin lumah ac wangin koano. Nga ngetak nu yen engyeng uh — wangin kalem we.
Ndinayangʼana dziko lapansi, ndipo linali lopanda anthu ndi lopanda kanthu; ndinayangʼana thambo, koma linalibe kuwala kulikonse.
24 Nga ngetang nu ke eol uh, tuh na kusrusrsrusr, Ac tohktok uh wacwat.
Ndinayangʼana mapiri, ndipo ankagwedezeka; magomo onse ankangosunthira uku ndi uku.
25 Nga liye lah wangin mwet. Finne won yen engyeng uh — sohkla wanginla.
Ndinayangʼana, ndipo sindinaone anthu; mbalame iliyonse ya mlengalenga inali itathawa.
26 Acn ma imaiyukla ekla yen mwesis. Siti nukewa kunausyukla Ke sripen kasrkusrak upa lun LEUM GOD. (
Ndinayangʼana, dziko lachonde linali litasanduka chipululu; mizinda yake yonse inali itasanduka bwinja pamaso pa Yehova, chifukwa cha mkwiyo wake.
27 LEUM GOD El fahk mu faclu nufon ac fah mwesisla ac wangin ma oan fac, tusruktu El fah tia kunausla nufon.)
Yehova akuti, “Dziko lonse lidzasanduka chipululu komabe sindidzaliwononga kotheratu.
28 Faclu ac fah mwemelil; Inkusrao fah lohsrla. LEUM GOD El fahk ma inge, Ac El fah tia ekulla nunak lal. El orala tari sulela lal Ac fah tiana ekla liki.
Chifukwa chake dziko lapansi lidzalira ndipo thambo lidzachita mdima, pakuti ndayankhula ndipo sindidzafewa mtima, ndatsimikiza ndipo sindidzabwerera mʼmbuyo.”
29 Ke kusen kasrusr lun un mwet mweun fin horse ac mwet pisr, Mwet nukewa ac kaingla. Kutu ac kaing nu insak uh, Ac kutu ac fanyak nu inmasrlon eot lulap. Siti nukewa ac pisala, Ac wangin mwet ac sifil muta we.
Pakumva phokoso la okwera pa akavalo ndi la anthu oponya mivi, anthu a mʼmizinda adzathawa. Ena adzabisala ku nkhalango; ena adzakwera mʼmatanthwe mizinda yonse nʼkuyisiya; popanda munthu wokhalamo.
30 Jerusalem, kom sikiyukla tari! Mwe mea kom in nukum nuknuk srusra? Mwe mea kom in yunikomla ke mwe naweyuk gold ac sang sroal in akkatoye motom? Kom sifacna oru kom in kato ke wangin! Mwet kawuk lom siskomla Ac kena unikomi!
Iwe Yerusalemu, ndiwe bwinja! Ukutanthauza chiyani kuvala zovala zofiira ndi kuvalanso zokometsera zagolide? Ngakhale udzikonze maso ako powapaka zokometsera, ukungodzivuta chabe. Zibwenzi zako zikukunyoza; zikufuna kuchotsa moyo wako.
31 Nga lohng sie sao, oana pusren sie mutan akola in isus, Oana pusren tung lun sie mutan oswe tulik se oemeet natul. Pa inge tung lun Jerusalem, ke el suk mongol Ac asroelik paol ac fahk, “Nga ac misa! Elos tuku in uniyuwi!”
Ndikumva kulira ngati kwa mayi pa nthawi yake yobereka, kubuwula ngati kwa mayi amene akubereka mwana wake woyamba. Kuliraku ndi kwa anthu a mu Ziyoni, wefuwefu. Atambalitsa manja awo nʼkumati, “Kalanga ife! Tikukomoka. Moyo wathu waperekedwa kwa anthu otipha.”

< Jeremiah 4 >