< Jeremiah 37 >

1 Tokosra Nebuchadnezzar lun Babylonia el akleumyalak Zedekiah wen natul Josiah, tuh elan tokosrala lun Judah in aolul Jehoiachin wen natul Jehoiakim.
Nebukadinezara mfumu ya Babuloni, inakhazika pa mpando waufumu Zedekiya mwana wa Yosiya kukhala mfumu ya Yuda. Iye analowa mʼmalo mwa Yehoyakini mwana wa Yehoyakimu.
2 Tusruktu Zedekiah ac mwet leum lal ac mwet uh tiana akos kas ma LEUM GOD El ase nu sik in fahkak.
Koma Zedekiya kapena atumiki ake ngakhalenso anthu a mʼdzikomo sanasamalire mawu a Yehova amene anayankhula kudzera mwa mneneri Yeremiya.
3 Tokosra Zedekiah el supwalma Jehucal wen natul Shelemiah, ac mwet tol Zephaniah wen natul Maaseiah, in siyuk sik in aol mutunfacl sesr in pre nu sin LEUM GOD lasr.
Tsono Zedekiya anatuma Yehukali mwana wa Selemiya ndi wansembe Zefaniya mwana wa Maseya kwa mneneri Yeremiya ndi uthenga uwu: “Chonde tipempherereni kwa Yehova Mulungu wathu.”
4 In pacl se inge nga soenna kauli in presin, ac nga srakna sukosok in forfor inmasrlon mwet uh.
Nthawi imeneyinso nʼkuti Yeremiya ali ndi ufulu woyenda pakati pa anthu chifukwa anali asanaponyedwe mʼndende.
5 Mwet mweun lun Babylonia elos kuhlusya Jerusalem, tusruktu ke elos lohngak lah un mwet mweun lun Egypt elos tupalla tari masrol lun Egypt, elos folokla.
Nthawi imeneyinso nʼkuti gulu lankhondo la Farao litatuluka mʼdziko la Igupto. Ndipo Ababuloni amene anali atazinga Yerusalemu atamva zimenezi, anachoka ku Yerusalemuko.
6 Na LEUM GOD lun Israel, El fahk nu sik
Tsono Yehova anawuza mneneri Yeremiya kuti,
7 in fahkang nu sel Zedekiah, “Mwet mweun lun Egypt elos tuku in kasrekom, tusruktu elos ac folokla nu in facl selos.
“Uyiwuze mfumu ya Yuda imene inakutuma kuti udzapemphe nzeru kwa ine kuti Ine Yehova, Mulungu wa Israeli ndikuti, gulu lankhondo la Farao limene linatuluka kuti lidzakuthandize lidzabwerera kwawo ku Igupto.
8 Na mwet Babylonia ac sifilpa foloko. Elos ac fah mweuni siti uh, sruokya, ac esukak.
Ndipo Ababuloni adzabwerera kudzathira nkhondo mzinda uno. Iwo adzawugonjetsa ndi kuwutentha.
9 Nga, LEUM GOD, fahk nu suwos in tia sifacna kiapwekowos ac nunku mu mwet Babylonia elos ac tia foloko, mweyen elos ac foloko.
“Yehova akuti: Musadzinyenge, nʼkumaganiza kuti, ‘Ndithu Ababuloni adzatisiya.’ Ndithudi sadzakusiyani!
10 Kowos finne kutangla un mwet mweun lun Babylonia nufon ac mwet kinet mukena lula oan in lohm nuknuk selos, mwet ingan ac tukakek ac furreak siti se inge nwe ke apatla.”
Ngakhale mutagonjetsa gulu lonse lankhondo la Ababuloni limene likukuthirani nkhondo ndipo mʼmatenti mwawo ndikutsala anthu ovulala okhaokha, amenewo adzabwera ndi kudzatentha mzinda uno.”
11 Un mwet mweun lun Babylonia elos folokla liki acn Jerusalem ke elos etauk lah mwet mweun lun Egypt uh apkuranme.
Gulu lankhondo la Ababuloni litaleka kuthira nkhondo mzinda wa Yerusalemu chifukwa choopa gulu lankhondo la Farao,
12 Ouinge nga ako in mukuila liki acn Jerusalem ac som nu in facl sin Benjamin nga in eis ip luk ke acn lun sou.
Yeremiya ananyamuka kuchoka ku Yerusalemu ndi kumapita ku dziko la Benjamini kuti akalandire gawo lake la minda ya makolo ake.
13 Tusruktu ke nga sun Mutunpot Benjamin, mwet kol lun mwet karingin mutunpot uh, su inel pa Irijah wen natul Shelemiah ma natul Hananaiah, el tulokinyuwi ac fahk, “Kom kaingkinkutla in som kasru mwet Babylonia!”
Koma atafika pa Chipata cha Benjamini, mkulu wa alonda amene dzina lake linali Iriya mwana wa Selemiya, mwana wa Hananiya, anagwira mneneri Yeremiyayo ndipo anati, “Iwe ukuthawira kwa Ababuloni!”
14 Na nga fahk, “Mo! Nga tia kaing.” Tusruktu Irijah el tia lohngyu, a el sruokyuwi ac usyula nu yurin mwet leum.
Yeremiya anati, “Zimenezo si zoona! Ine sindikuthawira kwa Ababuloni.” Koma Iriya sanamumvere. Mʼmalo mwake anagwira Yeremiya nʼkupita naye kwa akuluakulu.
15 Elos arulana kasrkusrak sik ac sap in sringsring nga, ac kaliyuwi in lohm sel Jonathan, mwet sim lun tokosra, mweyen orekmakinyuk lohm sel nu ke iwen kapir.
Akuluakuluwo anamupsera mtima Yeremiya ndipo anamukwapula ndi kumuyika mʼnyumba ya mlembi Yonatani, imene anayisandutsa ndende.
16 Elos filiyuwi in sie fukil srisrik oan ye fohk uh, ac nga muta we ke pacl na loeloes.
Yeremiya anayikidwa mʼndende ya pansi pa nthaka, kumene anakhalako nthawi yayitali.
17 Tok Tokosra Zedekiah el sapla suliyu. Ke nga el mukena muta in lohm sel, el siyuk sik in lukma, “Ya oasr kutena kas sin LEUM GOD me?” Na nga topuk, “Oasr.” Na nga tafwelana in fahk, “Kom fah itukyang nu inpoun tokosra Babylonia.”
Kenaka Mfumu Zedekiya inatuma anthu kuti akayitane Yeremiya ndipo anabwera naye ku nyumba ya mfumu. Atafika mfumu inamufunsa mwamseri kuti, “Kodi pali mawu ena amene Yehova wakuwuza?” Yeremiya anayankha kuti, “Inde. Inu mfumu mudzaperekedwa kwa mfumu ya ku Babuloni.”
18 Na nga siyuk, “Ma koluk fuka nga oru lain kom, ku lain mwet leum lom ac mwet inge, in pwanang kom filiyuwi in presin?
Pamenepo Yeremiya anafunsa Mfumu Zedekiya kuti, “Kodi ndakulakwirani chiyani inuyo kapena akuluakulu anu kapenanso anthu awa, kuti mundiyike mʼndende?
19 Pia mwet palu lom ma fahk mu tokosra lun Babylonia ac fah tia mweuni kom ku facl sum?
Kodi ali kuti aneneri anu amene anakuloserani kuti, ‘Mfumu ya ku Babuloni sidzakuthirani nkhondo pamodzi ndi dziko lino’?
20 Na inge, Leum Fulat luk, nga kwafe sum in porongo mwe siyuk luk. Nunak munas, nimet folokinyula nu in presin in lohm sel Jonathan. Kom fin supweyula, pwayena nga fah misa we.”
Koma tsopano, mbuye wanga mfumu, chonde tamverani. Loleni ndinene pempho langa pamaso panu: Musandibwezere ku nyumba ya mlembi Yonatani, kuopa kuti ndingakafere kumeneko.”
21 Na Tokosra Zedekiah el sapkin nga in kauli na inkalkal lun mwet san ke inkul sin tokosra. Nga mutana we, ac len nukewa ac utuku lof in bread se nak liki nien manman flao, nwe ke na lihsr bread in siti uh.
Tsono Mfumu Zedekiya analamula kuti Yeremiya asungidwe mʼbwalo la alonda. Ankamupatsa buledi tsiku ndi tsiku amene ankamugula kwa ophika buledi. Anapitiriza kutero mpaka buledi yense anatha mu mzindamo. Choncho Yeremiya anapitirira kukhala mʼbwalo la alonda.

< Jeremiah 37 >