< Jeremiah 18 >
1 LEUM GOD El fahk nu sik,
Yehova anawuza Yeremiya kuti,
2 “Oatula nu ke lohm sin mwet orek ahlu ke fohk kle, ac ingo nga fah sot nu sum kas ma nga lungse kom in fahkak.”
“Pita ku nyumba ya munthu wowumba mbiya, ndipo kumeneko ndikakuwuza mawu anga.”
3 Ouinge nga som nu we, ac nga liyauk mwet orek ahlu sac ke el orekma ke wheel in orekma lal.
Choncho ndinatsikira ku nyumba ya wowumba mbiya, ndipo ndinamuona akuwumba mbiya pa mkombero.
4 El fin orala sie ahlu tuh tia sun lungse lal, el ac eis kle sac ac ekulla nu ke sie pacna lumah.
Tsono amati ngati mbiya imene waumba ikhala yosawumbika bwino ankayiphwanya nʼkuwumbanso ina monga mmene afunira ndi dothi lake lomwe lija.
5 Na LEUM GOD El fahk nu sik,
Kenaka Yehova anandiwuza kuti,
6 “Ya tia oasr ku luk in oru nu suwos, mwet Israel, oana ke mwet orek ahlu se ac oru ke kle lal uh? Kowos muta inpouk oana ke kle uh oan inpoun mwet orek ahlu.
“Inu Aisraeli, kodi Ine sindingathe kuchita nanu monga amachitira wowumba mbiya?” akutero Yehova. “Inu muli mʼmanja mwanga ngati mtapo mʼmanja mwa wowumba mbiya.
7 Nga fin fahk ke kutu pacl mu nga ac fusak, koteya, ku kunausla kutena mutunfacl ku tokosrai,
Ngati nditalengeza kuti mtundu wina wa anthu kapena ufumu wina ndiwuzula, kuwugwetsa ndi kuwuwononga,
8 a toko mutunfacl sac forla liki orekma koluk lal, na nga ac tila oru ma nga tuh fahkla mu nga ac oru.
ndipo ngati mtundu wa anthu umene ndawuchenjezawo ulapa zoyipa zawo, ndiye kuti Ine ndidzaleka ndipo sindidzabweretsa pa anthuwo mavuto amene ndinakonzekera kuwachitira.
9 Ku nga fin fahk mu nga ac musaeak ku akkeye sie mutunfacl ku tokosrai,
Ndipo ngati ndilengeza kuti ndikufuna kumanga ndi kukhazikitsa mtundu wa anthu kapena ufumu.
10 na toko mutunfacl sac tia akosyu ac orekma koluk, na nga ac tila oru ma nga fahkla mu nga ac oru.
Koma mtunduwo ukachita choyipa pamaso panga nʼkusandimvera, ndiye kuti sindidzawuchitiranso zabwino zimene ndimafuna ndiwuchitire.
11 Ke ma inge, fahkang nu sin mwet Judah ac mwet Jerusalem lah nga akoo in lainulos ac kalyaelos. Fahkang elos in tui liki moul koluk lalos, ac aolla ouiya ma elos oru ingan.
“Ndipo tsopano kawawuze anthu a ku Yuda ndi amene akukhala mu Yerusalemu kuti, ‘Yehova akuti, Taonani! Ndikukukonzerani mavuto, ndi kuganizira zoti ndikulangeni. Kotero siyani makhalidwe anu oyipa aliyense wa inu, ndipo mukonzenso makhalidwe anu ndi zochita zanu.’
12 Elos ac topuk kom ac fahk, “Mo, efu ku kut in tui? Kut ac likkekena ac oru na ma koluk ke lungse lasr.”
Koma iwo adzayankha kuti, ‘Zimenezo nʼzosathandiza. Ife tidzapitiriza kuchita zomwe takonzekera; aliyense wa ife adzatsatira zoyipa za mtima wake wokanika.’”
13 LEUM GOD El fahk, “Siyuk sin mutunfacl nukewa lah nu oasr pacl ma Kain ouiya inge nu sikyak meet. Ouiya na koluk se pa mwet Israel uh oru inge!
Yehova akuti, “Uwafunse anthu a mitundu ina kuti: Kodi ndani anamvapo zinthu zofanana ndi zimenezi? Israeli amene anali ngati namwali wanga wachita chinthu choopsa kwambiri.
14 Ya nu oasr pacl wanginla snow fin acn eoteot fulat Lebanon? Ya sungan infacl oyohu we uh nu oasr pacl mihnla?
Kodi chisanu chimatha pa matanthwe otsetsereka a phiri la Lebanoni? Kodi madzi ozizira amitsinje ochokera ku phiri la Lebanoni adzamphwa?
15 Ma inge finne fahsrna wo, a mwet luk uh mulkinyula. Elos esukak mwe keng nu ke ma sruloala. Elos tukulkul ke inkanek lalos. Elos tia sifilpa fahsr ke ouiya meet ah, A elos fahsr ke inkanek ma tia akilenyuki.
Komatu anthu anga andiyiwala; akufukiza lubani kwa mafano achabechabe. Amapunthwa mʼnjira zawo zakale. Amayenda mʼnjira zachidule ndi kusiya njira zabwino.
16 Elos orala acn se inge in sie mwe aksangeng, Ma ac srungayukla nwe tok. Elos nukewa su fahsr we ac fah arulana lut ke ma elos liye. Elos ac fah usruk sifalos ke fwefela lalos.
Dziko lawo amalisandutsa chipululu, chinthu chochititsa manyazi nthawi zonse; onse odutsapo adzadabwa kwambiri ndipo adzapukusa mitu yawo.
17 Nga ac fah luselik mwet luk ye mutun mwet lokoalok lalos, Oana ke kutkut uh ukukla ke eng kutulap. Nga ac fah ngetla lukelos, Ac tia kasrelos ke pacl in ongoiya nu selos.”
Ngati mphepo yochokera kummawa, ndidzawabalalitsa pamaso pa adani awo; ndidzawafulatira osawathandiza pa tsiku la mavuto awo.”
18 Na mwet uh fahk, “Wona in oasr ma kut oru nu sel Jeremiah! Oasr mwet tol yorosr in luti kut, ac mwet lalmwetmet in aknunakye kut, ac mwet palu in fahkak kas lun God nu sesr. Lela kut in orek loh kikiap lainul ac tia sifil lohng ma el fahk uh.”
Anthuwo anati, “Tiyeni, tipangane zoti timuchitire Yeremiya; pakuti ansembe otiphunzitsa malamulo tidzakhala nawobe. Anthu anzeru otilangiza tidzakhala nawo, ndiponso aneneri otilalikira mawu. Choncho tiyeni timupezere chifukwa ndipo tisamvere chilichonse chimene akunena.”
19 Na nga pre ac fahk, “LEUM GOD, lipsre pre luk, ac porongo ma mwet lokoalok luk inge fahk keik.
Ndipo ndinapemphera kwa Yehova kuti, “Inu Yehova, ndimvereni; imvani zimene adani anga akunena za ine!
20 Ya ma koluk uh pa molin ma wo? A liye, elos pukanak luf se nu sik nga in putatyang nu loac. Esam lah nga tuh tuku nu yurum in kwafe kaclos, ac srike in loangelos liki kasrkusrak lom.
Kodi chinthu choyipa nʼkukhala dipo la chinthu chabwino? Komabe iwo andikumbira dzenje. Kumbukirani kuti ndinadzayima pamaso panu kudzawapempherera kuti muwachotsere mkwiyo wanu.
21 Ke ma inge, LEUM GOD, lela tulik natulos in misa ke masrinsral, ac in anwuki pac ke mweun. Lela mukul uh in misa ke mas ac mwet fusr in anwuki ke mweun. Mutan an in katinmasla, ac wangin tulik natulos.
Choncho langani ana awo ndi njala; aperekeni kuti aphedwe ndi lupanga. Akazi awo asanduke opanda ana ndi amasiye; amuna awo aphedwe ndi mliri, anyamata awo aphedwe ndi lupanga ku nkhondo.
22 Supwala sie un mwet koluk in kunausya lohm selos ac usla koano uh ke wangin eteya selos. Oru elos in wowoyak ke tuninfong. Mwet inge pukanak sie luf nga in putatyang nu loac, ac oakiya mwe kwasrip in sruokyuwi.
Kulira kumveke kuchokera mʼnyumba zawo mutawatumizira gulu lankhondo mwadzidzidzi kuti liwakanthe. Iwo andikumbira dzenje kuti ndigweremo ndipo atchera msampha mapazi anga.
23 LEUM GOD, kom etu nufon pwapa lalos in uniyuwi. Nikmet nunak munas nu selos ke orekma koluk lalos, ku tulalosla liki ma sufal lalos. Siselosi nu in fohk uh ac kutangulosla. Oru ma inge nu selos in kasrkusrak lom.”
Koma Inu Yehova, mukudziwa ziwembu zawo zonse zofuna kundipha. Musawakhululukire zolakwa zawo kapena kufafaniza machimo awo pamaso panu. Agonjetsedwe pamaso panu; muwalange muli wokwiya.”