< Jeremiah 12 >

1 LEUM GOD, nga fin srukak sie sripa nga kom in tukeni akukuin kac, Ma kom ac fahk uh pa pwaye uh. Ne ouinge, nga ke kusen siyuk nu sum ke nununku suwohs. Efu ku mwet koluk uh kasrupi? Efu ku mwet kutasrik uh wo ouiyalos?
Yehova, Inu mumakhala wokhoza nthawi zonse ndikati nditsutsane nanu. Komabe ndikufuna kuyankhula nanu za mlandu wanga. Chifukwa chiyani anthu oyipa zinthu zimawayendera bwino? Chifukwa chiyani anthu achinyengo amakhala pabwino?
2 Kom yokwalosi, ac elos okahla; Elos kapak ac isus fahko. Elos fahk kas wo keim pacl nukewa A insialos loesla nu sum.
Inu munawadzala ndipo anamera mizu; amakula ndi kubereka zipatso. Dzina lanu limakhala pakamwa pawo nthawi zonse, koma mitima yawo imakhala kutali ndi Inu.
3 Tusruktu, LEUM GOD, kom eteyu. Kom liye ma nga oru Ac etu lah nga lungse kom. Amakunla mwet koluk inge oana sheep ma ac anwuki; Taranulos nu ke pacl lalos in anwuki.
Koma Inu Yehova, ine mumandidziwa; mumandiona ndipo mumayesa zolingalira zanga. Akokeni anthu oyipawo ngati nkhosa zokaphedwa! Ayikeni padera mpaka tsiku loti akaphedwe!
4 Facl sesr uh ac paola nwe ngac? Mah nukewa inima uh ac uli putaka? Kosro ac won uh masla Ke sripen orekma koluk lun mwet lasr — Mwet su fahk mu, “God El tia liye ma kut oru uh.”
Kodi dziko lidzakhala likulirabe mpaka liti ndipo udzu mʼmunda uliwonse udzakhalabe ofota mpaka liti? Nyama ndi mbalame kulibiretu chifukwa anthu amene amakhalamo ndi oyipa. Iwo amati: “Yehova sangathe kuona ntchito zathu.”
5 LEUM GOD El fahk, “Jeremiah, kom fin totola ke kom akutun nu sin mwet, Na kom ac akutun fuka nu sin horse uh? Kom fin tukulkul ke sie acn mwesas, Na kom ac tuyak fuka ke insak matol sisken Infacl Jordan?
Yehova anayankha kuti, “Ngati kukutopetsa kuthamanga pamodzi ndi anthu nanga ungapikisane bwanji ndi akavalo? Ngati ukupunthwa ndi kugwa pa malo abwino, udzatha bwanji kuthamanga mʼnkhalango za ku Yorodani?
6 Finne ma lim, mwet in sou lom sifacna, elos kiapwekomla. Elos welulosyang su lain kom. Nik kom lulalfongelos, elos finne kaskas kulang nu sum.”
Ngakhale abale ako ndi anansi akuwukira, onsewo amvana zokuyimba mlandu. Usawakhulupirire, ngakhale ayankhule zabwino ndi iwe.
7 LEUM GOD El fahk, “Nga ngetla liki Israel. Nga sisla tari mutunfacl se nga sulela in ma luk. Mwet su nga lungse uh nga eisalosyang Nu inpoun mwet lokoalok lalos.
“Ine ndawasiya anthu anga; anthu amene ndinawasankha ndawataya. Ndapereka okondedwa anga mʼmanja mwa adani awo.
8 Mwet solla luk elos forma lainyu. Elos ngutngut nu sik Oana soko lion insak uh. Ke ma inge nga srungalos.
Anthu amene ndinawasankha asanduka ngati mkango wa mʼnkhalango. Akundibangulira mwaukali; nʼchifukwa chake Ine ndikudana nawo.
9 Mwet solla luk elos oana sie won Ma won ngia tuku liki acn nukewa in lainul. Pangonma kosro lemnak nukewa In tuku kangla nufon!
Anthu anga amene ndinawasankha asanduka ngati mbalame yolusa yamawangamawanga imene akabawi ayizinga. Pitani, kasonkhanitseni nyama zakuthengo. Mubwere nazo kuti zidzadye mbalameyo.
10 Mwet kol puspis ke mutunfacl saya elos kunausla ima in grape luk. Elos lolongya ima luk uh. Elos ekulla facl wolana sik nu ke acn mwesis.
Abusa ambiri anawononga munda wanga wa mpesa, anapondereza munda wanga; munda wanga wabwino uja anawusandutsa chipululu.
11 Elos oru acn uh sie acn mwesisla, wangin ma oan fac, Musalla oan ye mutuk. Facl sac nufon ekla nu ke sie acn mwesis, Ac wanginna mwet lohang nu kac.
Unawusandutsadi chipululu. Ukanali wokhawokha chomwecho ukundilirira Ine. Dziko lonse lasanduka chipululu chifukwa palibe wolisamalira.
12 Mwet uh tuku liki acn fulat nukewa yen mwesis uh In usla kutena ma lula we. Nga supwala mweun in kunausla facl sac nufon; Wangin mwet ac muta in misla.
Anthu onse owononga abalalikira ku zitunda zonse za mʼchipululu. Yehova watuma ankhondo ake kudzawatha kuyambira kumalire ena a dziko mpaka ku malire enanso a dziko, ndipo palibe amene adzakhale pa mtendere.
13 Mwet luk elos taknelik wheat, a kosrani kokul. Elos kemkatu ke wangin. Ke sripen kasrkusrak luk Ma sunalos uh tiana fok.”
Anthu anafesa tirigu koma anatuta minga; anadzitopetsa kugwira ntchito koma osapeza phindu lililonse. Choncho mudzachita manyazi ndi zokolola zanu chifukwa cha mkwiyo wa Yehova.”
14 LEUM GOD El fahk, “Oasr ma nga ac fahk ke mwet tulan lun Israel su kunausla facl se nga tuh sang sin mwet luk, mwet Israel. Nga fah eisla mwet kutasrik inge liki facl selos, oana ke soko sak ac fifyak uh. Ac nga fah molela Judah lukelos.
“Anthu oyipa oyandikana ndi anthu anga Aisraeli, akuwalanda Aisraeliwo dziko, cholowa chimene ndinawapatsa. Nʼchifukwa chake ndidzawachotsa mʼdziko limenelo, ndipo ndidzachotsa banja la Yuda pakati pawo.
15 Tusruktu tukun nga usalosla, nga fah pakomutalos. Nga fah folokonma kais sie mutunfacl nu fin acn selos sifacna, ac nu facl selos sifacna.
Komabe nditawachotsa, ndidzawachitiranso chifundo, ndipo ndidzabwezera aliyense cholowa chake ndi dziko lake.
16 Elos fin wi mwet luk alu ke insialos pwaye, ac elos fin fulahk ke kas inge: ‘Oana ke LEUM GOD El moul’ — oana ke elos tuh luti mwet luk in fulahk inen Baal in pacl meet ah — na elos fah ku in oaoala yurin mwet luk, ac wi eis mwe insewowo.
Ndipo ngati iwo adzaphunzira bwino njira za anthu anga ndi kulumbira mʼdzina langa, namanena kuti, ‘Pali Yehova wamoyo,’ monga iwo anaphunzitsira anthu anga kulumbira mʼdzina la Baala, Ine ndidzawakhazikitsa pakati pa anthu anga.
17 Tusruktu kutena mutunfacl fin tia akos, na nga fah fusulosyak ac kunauselosla. Nga, LEUM GOD, pa fahk ma inge.”
Koma ngati mtundu wina uliwonse sudzamvera, Ine ndidzawuchotsa ndi kuwuwonongeratu,” akutero Yehova.

< Jeremiah 12 >