< Isaiah 8 >

1 LEUM GOD El fahk nu sik, “Eis sie ipin mwe sim lulap ac simusla fac ke mutun sim lulap: ‘Sulaklak Eisla, Aksaya Wapi.’
Yehova anati kwa ine, “Tenga cholembapo chachikulu ndipo ulembepo malemba odziwika bwino: Kusakaza-Kwamsanga Kufunkha-Kofulumira.
2 Eis mwet lulalfongiyuk luo inge tuh elos in mwet loh: mwet tol Uriah, ac Zechariah wen natul Jeberechiah.”
Ndipo ndidzayitana wansembe Uriya ndi Zekariya mwana wa Yeberekiya kuti akhale mboni zanga zodalirika.”
3 Kutu pacl tok, mutan kiuk el pitutu ac oswela wen se. Na LEUM GOD El fahk nu sik, “Sang inel ‘Sulaklak-Eisla-Aksaya-Wapi.’
Ndipo ine ndinapita kwa mneneri wamkazi, ndipo anakhala woyembekezera nabala mwana wamwamuna. Ndipo Yehova anati kwa ine, “Umutche dzina lakuti, ‘Kusakaza-Kwamsanga Kufunkha-Kofulumira.’
4 Meet liki tulik mukul sac ku in fahk ‘Papa’ ac ‘Nina,’ mwe kasrup nukewa lun Damascus ac ma wap nukewa lun Samaria ac fah utukla sin tokosra lun Assyria.”
Mwanayo asanayambe kudziwa kuyitana kuti, ‘Ababa’ kapena ‘Amama’ chuma cha Damasiko ndi zofunkha za Samariya zidzatengedwa ndi mfumu ya ku Asiriya.”
5 LEUM GOD El sifilpa kaskas nu sik.
Yehova anayankhulanso ndi Ine;
6 El fahk, “Ke sripen mwet inge srangesr eis kof mihs ma tuku ke Infacl srisrik Shiloah, a elos engan in eisalosyang nu inpaol Tokosra Rezin ac Tokosra Pekah,
“Popeza anthu a dziko ili akana madzi anga oyenda mwachifatse a ku Siloamu, ndipo akukondwerera Rezini ndi mwana wa Remaliya,
7 nga, LEUM GOD, ac fah use Tokosra Fulat lun Assyria ac un mwet mweun lal nukewa in mweun lain Judah. Elos ac fahsryak oana tuku lun sronot uh, oana kof lulap ke Infacl Euphrates, ac afunla pefacl uh.
nʼchifukwa chake Ambuye ali pafupi kubweretsa madzi amkokomo a mtsinje wa Yufurate kudzalimbana nawo; mfumu ya ku Asiriya ndi gulu lake lonse lankhondo. Madziwo adzasefukira mʼngalande zake zonse ndi mʼmagombe ake onse.
8 Elos ac asrma sasla Judah oana sie sronot ma lapak nu ke fulatan finpisen mwet uh, ac afunla ma nukewa.” God El wi kut! El karingin acn uh ye posohksok lal.
Ndipo adzalowa mwamphamvu mʼdziko la Yuda, adzasefukira, adzapitirira mpaka kumuyesa mʼkhosi. Mapiko ake otambasuka adzaphimba dziko lako lonse, iwe Imanueli!”
9 Kowos mutunfacl uh, tukeni nu sie ke sangeng! Porongo, kowos su muta yen loessula faclu. Akola in mweun, tusruktu kowos in sangeng! Aok akola, tusruktu kowos in sangeng!
Chitani phokoso lankhondo, inu mitundu ya anthu, ndipo munjenjemere! Tamverani, inu mayiko onse akutali. Konzekerani nkhondo ndipo munjenjemere! Konzekerani nkhondo ndipo munjenjemere!
10 Orala oakwuk lowos an, tusruktu ac fah tia ku in orekla. Fahk ma nukewa kowos lungse fahk, tusruktu ac wangin sripa, mweyen God El wi kut.
Konzani kachitidwe kanu kankhondo, koma simudzaphula kanthu, kambiranani zochita, koma zidzalephereka, pakuti Mulungu ali nafe.
11 Ke ku lulap lal, LEUM GOD El sensenkakinyu nga in tia fahsr ke inkanek ma mwet uh fahsr kac. El fahk,
Yehova anandiyankhula ine mwamphamvu, ndipo anandichenjeza kuti ndisamayende mʼnjira za anthuwa. Iye anati:
12 “Nik kom wela pwapa sulal lun mwet, ac nik kom sangeng ke ma elos sangeng kac uh.
“Usamanene kuti ndi chiwembu, chilichonse chimene anthuwa amati ndi chiwembu usamaope zimene anthuwa amaziopa, ndipo usamachite nazo mantha.
13 Esam lah nga, LEUM GOD Kulana, nga mutal. Nga pa kom ac sangeng se uh.
Yehova Wamphamvuzonse ndiye amene uyenera kumuona kuti ndi woyera, ndiye amene uyenera kumuopa, ndiye amene uyenera kuchita naye mantha,
14 Ke sripen mangoliyen mutal luk, nga oana sie eot ma mwet uh tukulkul kac. Nga oana sie sruhf ma ac srifusrya mwet in tokosrai lun Judah ac Israel, oayapa mwet Jerusalem.
ndipo ndiye amene adzakhala malo opatulika; koma kwa anthu a ku Yuda ndi kwa anthu a ku Israeli adzakhala mwala wopunthwitsa, mwala umene umapunthwitsa anthu, thanthwe limene limagwetsa anthu. Ndipo kwa anthu a mu Yerusalemu adzakhala ngati msampha ndi khwekhwe.
15 Mwet puspis fah tukulkul. Elos ac ikori ac itungyuki. Elos ac fah sruh ac utukla.”
Anthu ambiri adzapunthwapo adzagwa ndi kuthyokathyoka, adzakodwa ndi kugwidwa.”
16 Kowos, mwet tumuk lutlut, enenu in karinganang ac sruokya ku kas nukewa ma God El ase nu sik.
Manga umboniwu ndipo umate malamulowa pamaso pa ophunzira anga.
17 LEUM GOD El okanulla sifacna liki mwet lal uh, tuh nga lulalfongel ac filiya finsrak luk in El.
Ndidzayembekezera Yehova, amene akubisira nkhope yake nyumba ya Yakobo. Ine ndidzakhulupirira Iyeyo.
18 Nga pa inge, wi tulik ma LEUM GOD El ase nu sik. LEUM GOD Kulana, su tron lal oan fin Eol Zion, El supwekut nu sin mwet Israel in oana mwe akul moul nu selos.
Onani, ine ndili pano pamodzi ndi ana amene Yehova wandipatsa, ndife zizindikiro ndi zodabwitsa kwa Aisraeli zochokera kwa Yehova Wamphamvuzonse, amene amakhala pa Phiri la Ziyoni.
19 Tusruktu mwet uh ac fah siyuk kom in lolngok yurin mwet susfa ac mwet inutnut, su ac mahma srisrik ac mungulngul. Elos fah fahk, “Ya tia fal mwet uh in sukok kas sin ngun, ac lolngok yurin mwet misa in kasru mwet moul?”
Anthu akakuwuza kuti kafunsire kwa oyankhula ndi mizimu, amene amayankhula monongʼona ndi mongʼungʼudza, kodi anthu sayenera kukafunsira kwa Mulungu wawo? Chifukwa chiyani amafunsira kwa anthu akufa mʼmalo mwa kwa anthu amoyo,
20 Kowos in topkolos ac fahk, “Lipsre ma LEUM GOD El luti nu suwos! Nimet porongo mwet inutnut — ma elos fahk nu suwos uh ac tia ku in kasrekowos.”
kuti akalandireko mawu enieni ndi malangizo? Ngati anthuwo sayankhula monga mwa mawu awa, mwa iwo mulibe kuwala.
21 Mwet uh ac fufahsryesr fin facl sac, ac elos ac munasla ac masrinsralla. Ke sripen masrinsral lalos elos ac kasrkusrak ac selngawi tokosra lalos ac God lalos. Elos ac ngetak nu inkusrao,
Anthu adzayendayenda mʼdziko movutika kwambiri ali ndi njala; pamene afowokeratu ndi njala, iwo adzakwiya kwambiri ndipo adzayangʼana kumwamba ndi kutemberera mfumu yawo ndi Mulungu wawo.
22 ku suiya infohk uh, a wangin ma elos ac liye sayen mwe ongoiya ac lohsr matoltol — aok ac fah sisiyang elos nu in lohsr, ac wangin inkanek lalos in kaingla liki pacl in ongoiya se inge.
Ndipo akadzayangʼana pa dziko lapansi adzangoona mavuto okhaokha ndi mdima woopsa ndi wodetsa nkhawa, ndipo adzaponyedwa mu mdima wandiweyani.

< Isaiah 8 >