< Isaiah 57 >

1 Mwet wo uh misa, a wangin mwet nunku kaclos ku suk lah efu. Tusruktu ke elos misa tari, wangin mwe ongoiya ku in sonolos.
Anthu olungama amafa, ndipo palibe amene amalingalira mu mtima mwake; anthu odzipereka amatengedwa, ndipo palibe amene amamvetsa chifukwa chake. Anthu olungama amatengedwa kuti tsoka lisawagwere.
2 Elos su moulkin moul wo elos konauk misla ac mongla tukun misa lalos.
Iwo amene amakhala moyo wolungama amafa mwamtendere; amapeza mpumulo pamene agona mu imfa.
3 Kowos mwet koluk, fahsru in nununkeyuk kowos! Kowos tia wo liki mwet inutnut, mwet kosro, ac mutan su lungse kukakin manolos.
“Bwerani kuno, anthu ochita zoyipa, inu muli ngati zidzukulu za mkazi wachigololo ndi wadama!
4 Su kowos isrun an? Kowos mwet kikiap, su kowos yayai uh?
Kodi inu mukuseka yani? Kodi mukumunena ndani ndi kupotoza pakamwa panu? Kodi inu si ana owukira, zidzukulu za anthu abodza?
5 Kowos alu nu sin god lun eslap ke kowos orek kosro ye sak oal sunowos ingan. Kowos sang tulik nutuwos tuh in mwe kisa ke luf inmasrlon eot uh apkuran nu pe infacl uh.
Inu mumapembedza mafano pamene mumalobodoka ndi zilakolako zanu pakati pa mitengo ya thundu, ndiponso pa tsinde pa mtengo uliwonse wa nthambi zambiri. Mumapereka ana anu ngati nsembe mu zigwa ndiponso mʼmingʼalu ya mʼmatanthwe.
6 Kowos eis eot fwel we, ac alu nu kac in srulun god. Kowos okoala wain ac use mwe kisa wheat in mwe sang nu selos. Ya kowos nunku mu nga insewowo ke ma inge?
Mafano a pakati pa miyala yosalala ya mu zigwa ndiye chuma chanu. Inde, ndiye gawo lanu. Mumapereka chopereka cha chakumwa kwa mafanowo, ndipo mumaperekanso chopereka cha chakudya. Kodi zimenezi zingandichititse kuti ndikukomereni mtima?
7 Kowos som nu fineol fulat in orek kisa nu ke ma sruloala, ouinge kowos tia pwaye nu sik.
Inu munayiwala bedi lanu pa phiri lalitali ndi looneka kutali. Mumapita kumeneko kukapereka nsembe zanu.
8 Kowos tulokunak ma sruloala fohkfok lowos in lohm suwos sisken na mutunoa uh. Kowos sisyula. Kowos susarla ac sroang nu fin mwe oan kiowos wi mwet kawuk lowos su kowos moli in oan yuruwos. Ouinge sun lungse koluk lowos.
Mʼnyumba mwanu mwayika mafano kuseri kwa zitseko ndiponso pa mphuthu. Mwandisiya Ine, mwavula zovala zanu. Bedi lanu mwalikulitsa ndipo mwakwera ndi zibwenzi zanu, ndiye mwazilipira kuti mugone nazo. Kumene mwakwaniritsa zilakolako zanu zoyipa.
9 Kowos fifla ke ono keng ac mosrwekowosla ke mwe akmusra, ac som alu nu sin god Molech. Kowos supwala mwet utuk kas nu yen loessula, finne nu in facl lun misa, in suk god saya in alu nu kac. (Sheol h7585)
Mumapita kukapembedza fano la Moleki mutatenga mafuta ndi zonunkhira zochuluka. Munachita kutumiza akazembe anu kutali; inu ngakhale munapita ku manda kwenikweniko! (Sheol h7585)
10 Kowos ne totolana in suk god saya ingan, a kowos tiana fuhleak. Kowos tiana munasla ke sripen kowos pangon mu ma sruloala fohkfok lowos ingan sot ku nu suwos.
Inu mumatopa ndi maulendo anu, koma simunathe kunena kuti, ‘Nʼzopanda phindu.’ Munapezako kumeneko zokhumba zanu nʼchifukwa chake simunalefuke.
11 LEUM GOD El fahk, “Su god inge ma oru kowos sangeng, pwanang kowos kikiap nu sik ac tiana esamyu? Ya kowos tila akfulatyeyu mweyen in pacl na loeloes nga misla ac tia kaskas nu suwos?
“Kodi ndani amene mwachita naye mantha ndi kumuopa, kotero kuti mwakhala mukundinamiza, ndipo Ine simundikumbukira nʼkomwe, kapena kuganizirapo mʼmitima yanu za Ine? Kodi mwaleka kundiopa chifukwa choti ndakhala chete nthawi yayitali?
12 Kowos nunku mu ma kowos oru an pwayena, tusruktu nga fah fahkak luman orekma koluk lowos in eteyuk, ac ma sruloala lowos ac fah tia ku in kasrekowos.
Koma ndaonetsa poyera ntchito zanu zomwe mumati nʼzolungama, ndi mafano anu kuti nʼzosathandiza.
13 Pacl kowos wowoyak in suk kasru, lela ma sruloala lowos ingan in molikowosla! Kitin eng na srisrik ku in okulosla! A elos su lulalfongiyu elos fah mutana in facl se inge, ac alu nu sik in Tempul luk.”
Pamene mufuwula kupempha thandizo, mafano anu amene munasonkhanitsawo ndiyetu akupulumutseni! Mphepo idzanyamula mafano anu onsewo, mpweya chabe udzawulutsa mafanowo. Koma munthu amene amadalira ine adzalandira dziko lokhalamo. Phiri langa lopatulika lidzakhala lakelake.”
14 LEUM GOD El fahk, “Musai inkanek uh, ac akoela! Lela mwet luk in foloko nu yuruk. Eisla ma nukewa su kosrala inkanek lalos!
Ndipo panamveka mawu akuti, “Undani, undani, konzani msewu! Chotsani zotchinga pa njira yoyendamo anthu anga.”
15 “Nga God fulat ac mutal, su moul ma pahtpat. Nga muta in sie acn fulat ac mutal, tusruktu nga oayapa muta yurin mwet pusisel ac mwet auliyak, tuh nga in ku in aksasuye lulalfongi ac finsrak lalos.
Pakuti Iye amene ali Wamkulu ndi Wopambanazonse, amene alipo nthawi zonse, amene dzina lake ndi Woyerayo, akunena kuti, “Ndimakhala pamalo aulemu ndi opatulika, koma ndimakhalanso ndi munthu wodzichepetsa ndi wosweka mtima kuti odzichepetsawo ndiwalimbitse ndi kuwachotsa mantha osweka mtima.
16 Nga sang moul nu sin mwet luk, ac nga fah tia kolla mulat luk ac amei yorolos nwe tok.
Sindidzawatsutsa anthu mpaka muyaya kapena kuwapsera mtima nthawi zonse, popeza kuti ndinalenga anthu anga ndi kuwapatsa mpweya wamoyo.
17 Nga tuh kasrkusrak selos ke sripen ma koluk ac nunak in rapku lalos, ouinge nga tuh kalyaelos ac ngetla lukelos. Tusruktu elos likkekelana ac fahsrna ke ouiya koluk lalos.
Ine ndinakwiya kwambiri chifukwa cha tchimo lawo ladyera; ndinawalanga ndi kuwafulatira mokwiya, koma iwo anapitirirabe kuchita ntchito zawo zoyipa.
18 “Nga liye tari ma elos oru, tusruktu ne ouinge nga fah akkeyalosla. Nga fah kololos ac kasrelos, ac nga fah akwoyalos su tung.
Ndaona zochita zawo, komabe ndidzawachiritsa; kuwapumulitsa ndi kuwapatsa mtendere,
19 Nga sang misla nu selos su muta apkuran ac oayapa elos su muta loessula! Nga fah akkeyala mwet luk.
anthu olira a mu Israeli adzanditamanda ndi milomo yawo. Anthu amene ali kutali ndi apafupi pomwe ndidzawapatsa mtendere,” “Ndipo ndidzawachiritsa.” Akutero Yehova.
20 Tusruktu mwet koluk elos oana noa meoa ma tia tui in sisak kutkut ac ma fohkfok nu fin acn uh.”
Koma anthu oyipa ali ngati nyanja yowinduka, yosatha kukhala bata, mafunde ake amaponya matope ndi ndere.
21 LEUM GOD El fahk, “Wangin misla nu sin mwet koluk.”
“Palibe mtendere kwa oyipa,” akutero Mulungu wanga.

< Isaiah 57 >