< Isaiah 44 >

1 LEUM GOD El fahk, “Porongo inge, Israel, mwet kulansap luk — Mwet solla luk, fwilin tulik natul Jacob.
Yehova akuti, “Mvera tsopano, iwe Yakobo, mtumiki wanga, Israeli, amene ndinakusankha.
2 Nga LEUM GOD su orekomla; Nga nuna kasrekom oe ke kom isusla ah me. Nik kom sangeng; kom mwet kulansap luk, Mwet sulela luk su nga lungse.
Yehova amene anakupanga iwe, anakuwumba iwe mʼmimba ya amayi ako, ndi amene adzakuthandiza iwe. Iye akuti, Usachite mantha, iwe Yakobo, mtumiki wanga, Yesuruni, amene ndinakusankha.
3 “Nga fah sang kof nu sin acn malu Ac oru tuh infacl in soror ke acn pao. Nga fah okoaot ngunik ac mwe insewowo luk Nu fin fwilin tulik nutum.
Pakuti ndidzathira madzi pa nthaka yowuma, ndi kuyendetsa mitsinje mʼdziko lowuma; ndidzatumiza Mzimu wanga pa ana anu, ndi kutsitsa madalitso anga pa zidzukulu zanu.
4 Elos ac sa in kap oana mah ma aksroksrokyeyuk wo, Oana sak willow ma kap sisken infacl ma yohk kof soror we.
Iwo adzakula ngati udzu wothirira bwino ndi ngati bango lomera mʼmbali mwa mitsinje ya madzi oyenda.
5 “Mwet uh fah kais sie fahk, ‘Nga ma lun LEUM GOD.’ Elos fah tuku in weang mwet Israel. Kais sie fah simusla Inen LEUM GOD fin paol, Ac sifacna fahk mu el sie sin mwet lun God.”
Wina adzanena kuti, ‘Ine ndine wa Yehova;’ wina adzadzitcha yekha wa banja la Yakobo; winanso adzalemba pa dzanja lake, ‘Wa Yehova’ ndipo adzadzitcha wa banja la Israeli.
6 LEUM GOD, su leumi ac karingin Israel, LEUM GOD Kulana, El fahk ouinge: “Nga pa oemeet, ac oayapa safla, ac nga God sefanna; Wangin sie pac god sayuk.
“Yehova Mfumu ndi Mpulumutsi wa Israeli, Yehova Wamphamvuzonse akuti: Ine ndine woyamba ndi wotsiriza; palibenso Mulungu wina koma Ine ndekha.
7 Ya oasr sie sayuk su ku in oru ma nga orala tari? Su ku in palyeak ma nukewa ma sikyak Oe ke mutawauk ah me na nwe ke safla lun faclu?
Ndani nanga angafanane ndi Ine? Muloleni kuti ayankhule. Muloleni andifotokozere ndi kundiyalira bwino lomwe zimene zinachitika kuyambira pamene ndinkakhazikitsa anthu anga akalekale, ndi ziti zimene zidzachitike; inde, muloleni alosere zimene zikubwera.
8 Mwet luk, nimet sangeng! Kowos etu lah oemeet me nu inge Nga fahkak tari ma nukewa ma ac sikyak, Ac kowos mwet loh luk. Mea, oasr pac god saya? Wangin! Wangin siefanna eot ku ma nga etu kac!”
Musanjenjemere, musachite mantha. Kodi sindinakuwuzeni zimenezi ndi kuzilosera kalekale lomwe? Inu ndinu mboni zanga. Kodi aliponso Mulungu wina kupatula Ine? Ayi, palibe Thanthwe linanso limene sindikulidziwa.”
9 Mwet nukewa su taflela ma sruloala uh elos mwet lusrongten, ac god ma elos akfulatye yohk uh wangin sripa. Elos su alu nu ke god inge elos mwet kun ac lalfon — ac elos ac fah akmwekinyeyuk.
Onse amene amapanga mafano ngachabe, ndipo milungu imene amayilemekeza ndi yopanda phindu. Iwo amene amapembedza mafano ndi wosaona; ndipo sazindikira kanthu. Choncho adzawachititsa manyazi.
10 Wanginna ma ac wo ke sie mwet el orala sie lumah ke osra, ac alu nu kac oana sie god!
Ndani amasema mulungu ndi kuwumba fano, limene silingamupindulire?
11 Mwet nukewa su alu nu kac ac fah akpusiselyeyuk. Mwet na pa orala ma sruloala uh. Lela elos in tuku ac tu ye nununku — elos ac fah tuninfongla, na ac fah yokna mwekinla lalos.
Iye pamodzi ndi anzake onse adzawachititsa manyazi; amisiri a mafano ndi anthu chabe. Aloleni onse asonkhane ndi kuyima pabwalo la milandu; onse adzaopsedwa ndipo adzachita manyazi.
12 Mwet orekma ke osra uh ac eis sie ipin osra ac esukla ke e. Ke po ku lal el sang sie hammer tuktukya osra uh nwe ke sikyak lumah se el nunku an. Ke el orekma, el ac masrinsralla, malula, ac totola.
Mmisiri wa zitsulo amatenga chitsulo ndipo amachiyika pa makala amoto; ndi dzanja lake lamphamvu amachisula pochimenya ndi nyundo. Pambuyo pake mʼmisiri uja amamva njala natha mphamvu; iye samwa madzi, ndipo amalefuka.
13 Mwet sroasr se ac srikeya sie sak. El makiya lumah se ma el ke orala uh ke mwe sim, supukla ke kufwen sroasr natul, ac taflela nu ke luman sie mwet na kato, ac filiya in lohm sel.
Mmisiri wa matabwa nayenso amayeza mtengo ndi chingwe ndipo amajambula chithunzi ndi cholembera; amasema bwinobwino ndi chipangizo chake ndipo amachiwongola bwino ndi chida chake. Amachipanga ngati munthu, munthu wake wokongola kuti aliyike mʼnyumba yake yachipembedzo.
14 El ku in pakiya sak cedar elan orekmakin, ku sulela sak oak ku sak cypress insak uh me. Ku el ku pac in yukwiya soko sak cedar ac soano af uh in akkapyauk.
Amagwetsa mitengo ya mkungudza, mwinanso amatenga mtengo wa payini kapena wa thundu nʼkudzisankhira mtengo wabwino pakati pa mitengo ya mʼnkhalango, ndipo amadzala mtengo wa payini ndi kuwuleka kuti ukule ndi mvula.
15 Sie mwet ac orekmakin sie ip ke sak soko ah nu ke etong, ac orek ma sruloala ke sie ip uh. Sie ip uh el ac sang tanak sie e in akfusrfusryal sifacna ac um bread; ac ip se ngia el orala nu ke sie god ac alu nu kac.
Mitengoyo munthu amachitako nkhuni; nthambi zina amasonkhera moto wowotha, amakolezera moto wophikira buledi ndi mbali ina ya mtengowo amapangira mulungu ndipo amapembedza; iye amapanga fano ndi kumaligwadira.
16 El ku in sang kutu ipinsak uh, tanak sie e; manman ikwa, ac kang nwe ke el kihpi. El akfusrfusryal sifacna ac fahk, “We, fusrfusr! Ngeng in e oh!”
Chigawo china cha mtengowo amasonkhera moto wowotcherapo nyama imene amadya, nakhuta. Iye amawotha motowo ndipo amanena kuti, “Aa! Ndikumva kutentha; pano pali moto.”
17 Ma lula ke sak soko ah el orala nu ke sie ma sruloala, na el pasrla nwe ten ac alu nu kac. El pre nu kac ac fahk, “Kom god luk — moliyula!”
Chigawo chotsala amapanga kamulungu, fano lake limenelo; amaligwadira ndi kulipembedza. Amapemphera kwa fanolo ndipo amanena kuti, “Iwe ndiwe mulungu wanga, ndipulumutse.”
18 Mwet ouinge arulana afon ac tia etu ma elos oru. Elos kaliya mutalos ac nunak lalos liki ma pwaye.
Anthu otere sadziwa kanthu, samvetsa kanthu kalikonse; maso awo ndi omatirira ndipo sangathe kuona, ndipo mitu yawo ndi yogontha kotero sangathe kumvetsa.
19 Mwet se ma orek ma sruloala uh el tia ku in nunkauk in fahk, “Kutu sak inge nga esukak. Nga um bread fin mulut uh, ac nga manman ikwa ac kangla. Ma lula ke sak soko ah nga orala nu ke ma sruloala se. Ac inge, nga pasrla nu ke sie polosak!”
Palibe amene amayima nʼkulingalira. Palibe wanzeru kapena womvetsa zinthu bwino woti nʼkunena kuti, chigawo china cha mtengowo ndinasonkhera moto; pa makala ake ndinaphikira buledi, ndinawotchapo nyama ndipo ndinadya. Chigawo chotsalachi ndipangire chinthu chonyansachi. Kodi ndidzagwadira mtengo?
20 Ke el oru ouinge uh, oana elan mongo apat. Nunak lalfon lal uh aktafongyella, oru upa in kasreyuk el. El tia ku in sifacna fahk lah ma sruloala se el sruok inpaol uh tia god se.
Munthu wotere ali ngati wodya phulusa, maganizo ake opusa amusocheretsa; motero kuti sangathe kudzipulumutsa yekha kapena kudzifunsa kuti, “Kodi chinthu chili mʼmanja mwangachi si chabodza?”
21 LEUM GOD El fahk, “Israel, esam ma se inge; Esam lah kom mwet kulansap luk. Nga orekomla tuh in mwet kulansap luk, Ac nga fah tiana mulkinkomla.
Yehova akuti, “Iwe Yakobo, kumbukira zinthu izi popeza kuti ndiwe mtumiki wanga, iwe Israeli. Ine ndinakupanga iwe, ndiwe mtumiki wanga; iwe Israeli, sindidzakuyiwala.
22 Nga pokla tari ma koluk lom, oana ke eng uh okla pukunyeng uh. Foloko nu yuruk; nga pa molikomla uh.”
Ndachotsa zolakwa zako ngati mitambo, ndi machimo ako ngati nkhungu ya mmawa. Bwerera kwa Ine, popeza ndakupulumutsa.”
23 Sasa ke engan, O kowos kusrao! Sala, kowos acn loal faclu! Sasa ke engan, kowos eol ac sak nukewa insak uh! LEUM GOD El fahkak fulat lal Ke El molela Israel, mwet lal.
Imbani mwachimwemwe, inu zolengedwa zamlengalenga, pakuti Yehova wachita zimenezi; fuwula, iwe dziko lapansi. Imbani nyimbo, inu mapiri, inu nkhalango ndi mitengo yonse, chifukwa Yehova wawombola Yakobo, waonetsa ulemerero wake mwa Israeli.
24 “Nga pa LEUM GOD, su langoekomla. Nga pa orekomla uh, Nga LEUM GOD, su orala ma nukewa. Nga mukena pa asroelik kusrao. Ke nga tuh orala faclu, wangin mwet kasreyu.
Yehova Mpulumutsi wanu, amene anakuwumbani mʼmimba ya amayi anu akuti: “Ine ndine Yehova, amene anapanga zinthu zonse, ndinatambasula ndekha zinthu zakuthambo, ndinayala ndekha dziko lapansi.
25 Nga oru mwet susfa uh in oana mwet lalfon, Ac aklusrongtenye ma mwet tuni acn engyeng uh palye. Nga lain kas lun mwet lalmwetmet, Ac nga akkalemye lah lalmwetmet lalos uh ma lalfon.
Ndine amene ndinalepheretsa mipingo ya anthu onyenga, ndipo ndimapusitsa owombeza mawula. Ndimasokoneza anthu a nzeru, ndi kuonetsa kuti nzeru zawo nʼzopusa.
26 A ke pacl mwet kulansap luk oru palu lal, Ac ke nga supwala sie mwet utuk kas in akkalemye lemlem luk, Nga oru tuh lemlem ac palu ingan in akpwayeiyuk. Nga fahk nu sin Jerusalem lah mwet ac fah sifilpa muta we, Ac nu sin siti in acn Judah lah ac sifilpa musaiyuk. Acn ma sikiyukla ingan, siti ac fah sifilpa tulokyak we.
Ndine amene ndimatsimikiza mawu a atumiki ake ndi kukwaniritsa zimene analosera amithenga ake. “Ndine amene ndinanena za Yerusalemu kuti mudzakhalanso anthu. Ndinanenanso za mizinda ya Yuda kuti idzamangidwanso. Za mabwinja awo ndinanena kuti ndidzawawutsanso.
27 Ke sie kas in sap ku luk, nga akpaoyela meoa.
Ndine amene ndinawuza nyanga yayikulu kuti, ‘Uma’ ndipo ndidzawumitsa mitsinje yako.
28 Nga fahk nu sel Cyrus, ‘Kom ac fah aolyu in leumi mwet luk, Ac kom fah oru ma nga lungse kom in oru: Kom fah sapkin Jerusalem in sifil musaiyukla Ac pwelung in Tempul in oakwuki.’”
Ndine amene ndinanena kwa Koresi kuti, ‘Iye ndiye mʼbusa wanga,’ ndipo adzachita zonse zimene ndikufuna; iye adzalamula kuti, ‘Yerusalemu amangidwenso’ ndi kuti, ‘Maziko a Nyumba ya Mulungu ayikidwenso.’”

< Isaiah 44 >