< Isaiah 38 >

1 Ke pacl se inge Tokosra Hezekiah el masak ac apkuran in misa. Mwet palu Isaiah, wen natul Amoz, el som nu yorol ac fahk nu sel, “LEUM GOD El fahk mu kom in akoela ma nukewa in wo, mweyen kom ac tia kwela. Kom ac misa.”
Nthawi imeneyo Mfumu Hezekiya anadwala ndipo anali pafupi kufa. Mneneri Yesaya mwana wa Amozi anapita kukamuona ndipo anati “Yehova akuti: Konza bwino nyumba yako, pakuti ukufa; suchira.”
2 Hezekiah el forang nu pe sinka uh ac pre:
Hezekiya anatembenuka nayangʼana kukhoma, napemphera kwa Yehova kuti,
3 “LEUM GOD, esam lah nga kulansupwekom ke inse pwaye ac suwohs, ac pacl nukewa nga srike na nga in oru ma lungse lom.” Na el mutawauk in tung arulana upa.
“Inu Yehova, kumbukirani momwe ndayendera pamaso panu mokhulupirika ndi modzipereka ndipo ndakhala ndikuchita zabwino pamaso panu.” Ndipo Hezekiya analira mosweka mtima.
4 Na LEUM GOD El sap Isaiah elan
Ndipo Yehova analamula Yesaya kuti:
5 folokla nu yorol Hezekiah ac fahk nu sel, “Nga, LEUM GOD lal David, papa matu tomom, lohng pre lom ac liye sroninmotom. Nga ac fah lela nu sum in sifilpa moul ke yac singoul limekosr.
“Pita kwa Hezekiya ndipo ukamuwuze kuti, ‘Yehova, Mulungu wa kholo lake Davide akuti: Ndamva pemphero lako ndipo misozi yako ndayiona; ndidzakuwonjezera zaka 15 pa moyo wako.
6 Nga fah molikomla ac siti Jerusalem lukel Tokosra Fulat lun Assyria, ac nga fah karinganangna siti se inge.”
Ndipo ndidzakupulumutsa, iwe pamodzi ndi mzindawu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya, Ine ndidzawuteteza mzindawu.
7 Isaiah el topuk ac fahk, “LEUM GOD El ac sot sie akul nu sum in akpwayei lah El ac liyaung wulela lal.
“‘Ichi ndi chizindikiro cha Yehova kwa iwe kutsimikiza kuti Yehova adzachita zimene walonjeza:
8 Ke nien fan se ma musaiyukla sel Tokosra Ahaz, LEUM GOD El ac oru lulin faht uh in foloki fahluk singoul.” Na lul sac foloki ke fahluk singoul.
Chithunzithunzi chimene dzuwa likuchititsa pa makwerero a Ahazi ndidzachibweza mʼmbuyo makwerero khumi.’” Ndipo chithunzithunzi chinabwerera mʼmbuyo makwerero khumi.
9 Tukun Hezekiah el kwela liki mas lal, el simusla on in kaksak soko inge:
Ndakatulo ya Hezekiya mfumu ya ku Yuda imene analemba atadwala ndi kuchira:
10 Nga pangon mu nga ac som nu in facl sin mwet misa Ke pacl se nga sun kuiyen moul luk, Ac tiana aksafyela moul luk. (Sheol h7585)
Ine ndinaganiza kuti ndidzapita ku dziko la akufa pamene moyo ukukoma. (Sheol h7585)
11 Nga tuh nunku mu in facl sin mwet moul inge Nga fah tiana sifilpa liye LEUM GOD Ku kutena mwet moul.
Ndinaganiza kuti, “Sindidzaonanso Yehova, mʼdziko la anthu amoyo, sindidzaonanso mtundu wa anthu kapena kukhala pamodzi ndi amene amakhala pa dziko lapansi lino.
12 Moul luk uh utukla likiyu, Oana sie lohm nuknuk ma tuleyuki, Oana sie nuknuk ma laslasla liki mwe tol nuknuk. Nga nunku mu God El aksafyela moul luk.
Nyumba yanga yasasuka ndipo yachotsedwa. Ngati tenti ya mʼbusa mwapindapinda moyo wanga, ngati munthu wowomba nsalu; kuyambira usana mpaka usiku mwakhala mukundisiya.
13 Nga tung fong nufon se ke ngal, Oana lion soko in koteya sri keik. Nga nunku mu God El aksafyela moul luk.
Ndinkalira kupempha chithandizo usiku wonse mpaka mmawa; koma Inu Yehova munaphwanya mafupa anga ngati mkango, ndipo mwakhala mukundisiya.
14 Pusrek munasla ac srikeni, Ac nga sasao oana sie wule. Atronmutuk totola ke nga nget nu inkusrao. LEUM GOD, moliyula liki mwe lokoalok inge nukewa.
Ndinkalira ngati namzeze kapena chumba, ndinkabuwula ngati nkhunda yodandaula. Maso anga anatopa nʼkuyangʼana mlengalenga. Inu Ambuye, ine ndili mʼmavuto bwerani mudzandithandize!”
15 Mea nga ku in fahk? LEUM GOD pa oru ma inge. Insiuk keoklana, ac nga tia ku in motul.
Koma ine ndinganene chiyani? Yehova wayankhula nane, ndipo Iye ndiye wachita zimenezi. Chifukwa cha kuwawa kwa mtima wanga, ine ndidzayenda modzichepetsa masiku amoyo wanga onse.
16 LEUM GOD, nga ac moul nu sum, nu sum mukena; Akeyeyula ac lela nu sik in moul.
Ambuye, masiku anga ali mʼmanja mwanu. Mzimu wanga upeza moyo mwa Inu. Munandichiritsa ndi kundikhalitsa ndi moyo.
17 Keok luk fah ekla nu ke inse misla. Kom molela moul luk liki mwe sensen nukewa; Kom sisla ma koluk luk nukewa.
Ndithudi, ine ndinamva zowawa zotere kuti ndikhale ndi moyo; Inu munandisunga kuti ndisapite ku dzenje la chiwonongeko chifukwa mwakhululukira machimo anga onse.
18 Wangin sie mwet in facl sin mwet misa ku in kaksakin kom; Mwet misa tia ku in lulalfongi ke oaru lom. (Sheol h7585)
Pakuti akumanda sangathe kukutamandani, akufa sangayimbe nyimbo yokutamandani. Iwo amene akutsikira ku dzenje sangakukhulupirireni. (Sheol h7585)
19 Mwet moul pa kaksakin kom, Oana ke nga kaksakin kom inge. Papa uh fahk nu sin tulik natulos lupan oaru lom.
Amoyo, amoyo okha ndiwo amakutamandani, monga mmene ndikuchitira ine lero lino; abambo amawuza ana awo za kukhulupirika kwanu.
20 LEUM GOD, kom akkeyeyula. Kut fah srital ke harp ac onkakin kom; Kut fah alullul ke on in kaksak in Tempul lom ke lusen moul lasr.
Yehova watipulumutsa. Tiyeni tiyimbe ndi zoyimbira za zingwe masiku onse a moyo wathu mʼNyumba ya Yehova.
21 Na Isaiah el fahk nu sel tokosra elan apisya ono se orekla ke fokinsak fig nu ke faf kacl ah, na el ac fah kwela.
Yesaya anati, “Anthu atenge mʼbulu wankhunyu ndipo apake pa chithupsacho ndipo Hezekiya adzachira.”
22 Na Tokosra Hezekiah el siyuk, “Akul fuka se ac akpwayei lah nga ac ku in sifilpa som nu in Tempul?”
Hezekiya nʼkuti atafunsa kuti, “Kodi chizindikiro chako nʼchiyani chotsimikiza kuti ndidzapita ku Nyumba ya Yehova?”

< Isaiah 38 >