< Isaiah 25 >

1 LEUM GOD, kom God luk; Nga fah akfulatye kom ac kaksakin Inem. Kom orala ma usrnguk; Ac kom oaru na in akfahsrye Ma kom lumahla in pacl oemeet ah.
Yehova ndinu Mulungu wanga; ine ndidzakukwezani ndi kutamanda dzina lanu, pakuti mwachita zodabwitsa zimene munakonzekeratu kalekale mokhulupirika kwambiri.
2 Kom ekulla siti uh in oanna sruala, Ac kom kunausla pot ku we. Inkul fulat sin tokosra ma mwet lokoalok lasr musaela Wanginla. Ac fah tia sifil musaiyuk.
Inu mwasandutsa mzinda uja kukhala mulu wamiyala. Ndipo mzinda wamalinga wasanduka bwinja, linga la anthu achilendo lero si mzindanso ndipo sidzamangidwanso.
3 Mwet in mutunfacl kulana fah kaksakin kom; Mutunfacl sulallal nukewa ac fah sangeng sum.
Nʼchifukwa chake anthu amphamvu adzakulemekezani; mizinda ya mitundu ya anthu ankhanza idzakuopani.
4 Mwet sukasrup ac mwet mukaimtal elos kaing nu yurum Ac elos moulla in pacl in ongoiya. Kom sang nu selos acn in wikla ke pacl in paka, Ac acn lul ke pacl fol. Mwet sulallal elos anwuk oana ke eng upa uh fungulya pesinka,
Inu mwakhala ngati populumukira pa anthu osauka, mwakhala ngati kobisalirako munthu wovutika pa nthawi ya masautso ake. Mwakhala ngati pobisalirapo pa nthawi ya mphepo yamkuntho ndi mthunzi pa nthawi ya dzuwa. Pakuti anthu ankhanza ali ngati mphepo yamkuntho yowomba pa khoma,
5 Oana fol upa lun faht yen mwesis. A Kom, LEUM GOD, kom akmisyela wohwon lun mwet lokoalok lasr; Kom sikulya sasa lun mwet sulallal, Oana ke sie pukunyeng akoyohuye sie len fol.
ndiponso ngati kutentha mʼdziko lowuma. Inu mumaletsa phokoso la anthu achilendo. Monga momwe mthunzi wa mtambo umachepetsa kutentha, inu munaletsa nyimbo za anthu ankhanza.
6 In acn se inge, fin Eol Zion, LEUM GOD Kulana El fah akola sie kufwa nu sin mutanfahl nukewa faclu — sie kufwa ke mwe mongo na yuyu ac wain na wowo.
Pa phiri ili Yehova Wamphamvuzonse adzakonzera anthu a mitundu yonse madyerero a zakudya zokoma ndi vinyo wabwino. Phwando la nyama yonona ndi vinyo wabwino kwambiri.
7 El fah sa na moklela pukunyeng in asor su sunya mutunfacl nukewa.
Iye adzachotsa kulira kumene kwaphimba anthu ngati nsalu. Adzachotsa chinsalu chimene chakuta mitundu yonse ya anthu.
8 LEUM GOD Fulatlana El fah kunausla misa nwe tok! El ac fah eela sroninmuta liki mutun mwet nukewa, ac usla mwe mwekin ma mwet lal keok kac yen nukewa faclu. LEUM GOD sifacna pa fahk ma inge.
Yehova adzathetsa imfa mpaka muyaya, Ambuye Yehova adzapukuta misozi mʼmaso mwa munthu aliyense; adzachotsa manyazi a anthu ake pa dziko lonse lapansi, Yehova wayankhula.
9 Pacl se ma inge ac sikyak uh, mwet nukewa fah fahk, “El inge God lasr! Kut filiya lulalfongi lasr in El, ac El molikutla. El pa LEUM GOD! Kut filiya lulalfongi lasr in El, ac inge kut engan ac insewowo mweyen El molikutla.”
Tsiku limenelo iwo adzati, “Ndithudi, uyu ndiye Mulungu wathu; ife tinamudalira ndipo anatipulumutsa. Uyu ndiye Yehova, ife tinamudalira; tiyeni tikondwe ndi kusangalala chifukwa watipulumutsa.”
10 LEUM GOD El fah loangela Eol Zion, tusruktu mwet Moab ac fah futungyuki oana ke mah pao uh lolongyuki ke fohkon cow uh.
Yehova adzateteza phiri limeneli ndi dzanja lake; ndipo Amowabu adzawapondereza pomwe alilipo, ngati mmene amapondera manyowa mʼdzenje.
11 Elos ac fah asroela paolos oana elos in srike in kofkof, tusruktu God El ac akmwekinyalos, na paolos ac totola ac tili, tia ku in oru kutena ma.
Amowabuwo adzatambasula manja awo mʼmenemo, ngati mmene amachitira munthu wosambira. Koma Mulungu adzathetsa kunyada kwawo ngakhale luso la manja awo.
12 El ac fah kunausla pot ku ac fulat lun Moab ac rakinya nu infohk uh.
Iye adzagumula malinga awo ataliatali ndipo adzawagwetsa ndi kuwaponya pansi, pa fumbi penipeni.

< Isaiah 25 >