< Isaiah 24 >

1 LEUM GOD El ac fah kunausla faclu ac filiya in wanginla ma oan fac. El ac furalik fin acn uh ac akfahsryelik mwet fac.
Taonani, Yehova adzawononga dziko lapansi ndi kulisandutsa chipululu; Iye adzasakaza maonekedwe ake ndi kumwaza anthu ake onse.
2 Mwet nukewa fah pulakin kain in ongoiya sefanna — mwet tol ac mwet uh, mwet kohs ac mwet kacto, mwet kuka ac mwet moli, mwet ngusr mani ac mwet sang mani, mwet kasrup ac mwet sukasrup.
Aliyense zidzamuchitikira mofanana: wansembe chimodzimodzi munthu wamba, antchito aamuna mofanananso ndi ambuye awo aamuna, antchito aakazi chimodzimodzi ambuye awo aakazi, wogula chimodzimodzi wogulitsa, wobwereka chimodzimodzi wobwereketsa, okongola chimodzimodzi okongoza.
3 Faclu ac fah sikiyukla ac mokutkuti. LEUM GOD pa fahk ouinge, na ac orek oana ma El fahk.
Dziko lapansi lidzawonongedwa kwathunthu ndi kusakazikiratu. Yehova wanena mawu awa.
4 Faclu pulamlamla ac uli; faclu nufon ac munasla. Kewana faclu ac yen engyeng uh ac mwesri.
Dziko lapansi likulira ndipo likufota, dziko lonse likuvutika ndipo likuwuma, anthu omveka a dziko lapansi akuvutika.
5 Mwet uh aktaekyala faclu ke elos kunausla ma sap lun God, ac ke elos siakos wuleang se su El orala in oan nwe tok.
Anthu ayipitsa dziko lapansi; posamvera malangizo ake; pophwanya mawu ake ndi pangano lake lamuyaya.
6 Ouinge God El selngawi faclu. Mwet faclu elos eis mwatan orekma lalos. Pueni na mwet moul lula.
Nʼchifukwa chake matemberero akuwononga dziko lapansi; anthu a mʼdzikomo akuzunzika chifukwa cha kulakwa kwawo, iwo asakazika ndipo atsala ochepa okha.
7 Ima in grape uh mwella, ac fahsr in lisr wain uh. Elos nukewa su engan meet, inge elos asor.
Vinyo watsopano watha ndipo mphesa zikufota; onse okonda zosangalatsa ali ndi chisoni.
8 Wanginla pusren on kato ke harp ac drum.
Kulira kokometsera kwa matambolini kwatha, phokoso la anthu osangalala latha, zeze wosangalatsa wati zii.
9 Wanginla on ac engan ke wain; emah uh mwen selos.
Anthu sadzayimbanso akumwa vinyo; akadzamwa zaukali zidzakhala zowawa mʼkamwa mwawo.
10 Ma nukewa fohsak in siti uh, ac lohm nukewa lakiyuki, mwet koluk in tia utyak.
Mzinda wachisokonezo uja wawonongeka; nyumba iliyonse yatsekedwa.
11 Mwet uh wowo fin inkanek uh ke sripen wanginla wain. Engan ac pwar wanginla na pwaye liki facl se inge.
Anthu akulira mʼmisewu kufuna vinyo; chimwemwe chonse chatheratu, palibenso chisangalalo pa dziko lapansi.
12 Siti uh musalla, ac mutunpot we kunausyukla.
Mzinda wasanduka bwinja zipata zake zagumuka.
13 Ac fah pa inge ma ac sikyak nu ke mutunfacl nukewa fin faclu. Ac fah oana ke safla pacl in kosrani — wanginla fahko ke sak olive, ac grape nukewa kinkinla.
Zimenezi ndizo zidzachitikire mitundu yonse ya dziko lapansi ndiponso pakati pa mitundu ya anthu. Zidzakhala ngati pamene mitengo ya olivi yayoyoledwa, kapena ngati nthawi ya kunkha la mphesa atatsiriza kukolola.
14 Elos su painmoulla ac fah alullul ke engan. Elos su muta in mutunfacl roto ac fah fahk lupan fulatlana lun LEUM GOD,
Koma otsala onse akufuwula ndi kuyimba mwachimwemwe; anthu akumadzulo akutamanda ukulu wa Yehova.
15 ac elos su muta in mutunfacl kutulap fah kaksakunul. Mwet su muta wekof uh fah kaksakin LEUM GOD lun Israel.
Nʼchifukwa chake inu akummawa, tamandani Yehova; ndi inu okhala mʼmphepete mwa nyanja kwezani dzina la Yehova, Mulungu wa Israeli.
16 Liki acn loessulana faclu kut lohng pusren on in kaksakin God lun suwoswos. Tusruktu wangin finsrak luk! Foroti insiuk! Mwet kutasrik tia tui in orek kutasrik, ac sulallal lalos uh koluk liki na meet ah.
Kuchokera kumalekezero a dziko lapansi tikumva kuyimba kotamanda “Wolungamayo.” Koma ine ndinati, “Ndatheratu, ndatheratu! Tsoka kwa ine! Anthu achinyengo akupitirizabe kuchita zachinyengo, inde chinyengo chawo chikunkerankera mʼtsogolo.”
17 Porongeyu, mwet nukewa! Mwe aksangeng, luf loal, ac sruhf oan soanekowos.
Inu anthu adziko lapansi, zoopsa, dzenje ndi msampha zikukudikirani.
18 Kutena mwet su srike in kaingla liki mwe aksangeng inge ac fah putatla nu in luf loal, ac kutena su kaingla liki luf sac ac fah sruoh ke sie sruhf. Af upa ac fah kahkla liki kusrao, ac pwelung lun faclu fah kusrusryak.
Aliyense wothawa phokoso la zoopsa adzagwa mʼdzenje; ndipo aliyense wotuluka mʼdzenjemo adzakodwa ndi msampha. Zitseko zakumwamba zatsekulidwa, ndipo maziko a dziko lapansi agwedezeka.
19 Faclu fah srasrelik ac muliplipi, ac ikakelik.
Dziko lapansi lathyokathyoka, ndipo lagawika pakati, dziko lapansi lagwedezeka kotheratu.
20 Faclu sifacna fah tukulkul oana mwet sruhi se, wactot wactma oana sie lac lohm in sie paka. Faclu sringelik ke koluk la; ac fah ikori ac tiana sifil tuyak.
Dziko lapansi likudzandira ngati munthu woledzera likugwedezeka ndi mphepo ngati chisimba; lalemedwa ndi machimo ake. Lidzagwa ndipo silidzadzukanso.
21 Pacl se ac tuku ke LEUM GOD El ac kalyei ku lun acn lucng, ac mwet kol lun faclu.
Tsiku limenelo Yehova adzalanga amphamvu a kumwamba ndiponso mafumu apansi pano.
22 God El fah orani tokosra uh nu sie in iktokeni oana mwet kapir in sie luf loal. El fah kalelosi in presin nwe ke sun pacl in kalya nu selos.
Mulungu adzawasonkhanitsa pamodzi ngati amʼndende amene ali mʼdzenje. Adzawatsekera mʼndende ndipo adzalangidwa patapita nthawi yayitali.
23 Malem ac fah lohsrla, ac faht ac fah tia sifil kalem, mweyen LEUM GOD Kulana El ac fah tokosra. El fah leum in Jerusalem fin Eol Zion, ac mwet kol lun mwet uh ac fah liye wolana lal.
Mwezi udzanyazitsidwa, dzuwa lidzachita manyazi; pakuti Yehova Wamphamvuzonse adzakhala mfumu ndipo adzalamulira; pa Phiri la Ziyoni ndi ku Yerusalemu, ndipo adzaonetsa ulemerero wake pamaso pa akuluakulu.

< Isaiah 24 >