< Isaiah 17 >

1 LEUM GOD El fahk, “Siti Damascus ac fah kunausyukla, ac ekla yol in na ma musalla.
Uthenga wonena za Damasiko: “Taonani, mzinda wa Damasiko sudzakhalanso mzinda, koma udzasanduka bwinja.
2 Ac fah wanginla mwet muta in siti nukewa lun acn Syria nwe tok. Ac fah ekla acn mahma nien mongo lun sheep ac cow, ac wangin mwet ac luselosyak.
Mizinda ya Aroeri idzakhala yopanda anthu ndipo idzakhala ya ziweto, zimene zidzagona pansi popanda wina woziopseza.
3 Ac fah wanginla ma loangeyen Israel, ac siti Damascus ac fah tia sifil sifacna nununkal. Mwet Syria su painmoulla ac fah akmwekinyeyuk oana mwet Israel. Nga, LEUM GOD Kulana, pa fahk ma inge.”
Ku Efereimu sikudzakhalanso linga, ndipo ku Damasiko sikudzakhalanso ufumu; Otsalira a ku Siriya adzachotsedwa ulemu monga anthu a ku Israeli,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
4 LEUM GOD El fahk, “Sie len ac tuku ke wolana lun Israel ac fah wanginla, ac pacl mut lal ac fah ekla nu ke pacl sracl.
“Tsiku limenelo ulemerero wa Yakobo udzazimirira; ndipo chuma chake chidzasanduka umphawi.
5 Israel ac fah oana sie ima in wheat ma kosrkosrla tari, ac filfilla oana sie ima Infahlfal Rephaim ke kinkinla lisr fahko.
Israeli adzakhala ngati munda wa tirigu umene anatsiriza kukolola. Adzakhalanso ngati munda wa mʼchigwa cha Refaimu anthu atatha kukunkha ngala za tirigu.
6 Mwet na pu fah moulla, na acn Israel ac fah oana soko sak olive ma fahko nukewa sifeyukeni sayen ma luo na ku tolu ke lah oelucng, ku kais kutu na lula ke lah ten ah. Nga, LEUM GOD lun Israel, pa fahk ma inge.”
Komabe Aisraeli ochepa okha ndiwo ati adzatsale monga mʼmene zimatsalira zipatso ziwiri kapena zitatu pa nthambi ya pamwamba penipeni kapena zipatso zisanu pa nthambi za mʼmunsi mwa mtengo wa olivi akawugwedeza,” akutero Yehova, Mulungu wa Israeli.
7 Ke len sac, mwet uh ac fah forla in suk kasru sin El Su oralosla, God mutal lun Israel.
Tsiku limenelo anthu adzayangʼana Mlengi wawo ndipo adzatembenukira kwa Woyerayo wa Israeli.
8 Elos ac tia sifil alu ke loang ma elos orala ke paolos sifacna in kisakin mwe keng fac, ku lulalfongi sru ma elos tulokunak nu sin god mutan Asherah.
Iwo sadzakhulupiriranso maguwa ansembe, ntchito ya manja awo, ndipo sadzadaliranso mitengo ya mafano a Asera, ndiponso maguwa ofukizirapo lubani amene manja awo anapanga.
9 Ke len sac, siti ma potyak ku ac fah sisila ac filfilla in kulawi, oana siti ma mwet Hiv ac mwet Amor tuh kaingkunla ke elos kaingkin mwet Israel.
Tsiku limenelo mizinda yawo yamphamvu, imene anasiya chifukwa cha Aisraeli, idzakhala ngati malo osiyidwa kuti awirire ndi kumera ziyangoyango. Ndipo yonse idzakhala mabwinja.
10 Israel, kom mulkunla God su molikomla ac karingin kom oana sie eot kulana. Ac kom yukwiya sie ima oal nu sin sie god sac.
Inu mwayiwalatu Mulungu Mpulumutsi wanu; simunakumbukire Thanthwe, linga lanu. Choncho, ngakhale munadzala mbewu zabwino, ndi kuyitanitsa kunja mitengo ya mpesa,
11 Tusruktu ma inge finne srunak ac farengla ke lotutang se na kom yukwiya ah, a ac fah wangin fahko in kosrani. Ac fah oasr lokoalok mukena, ac waiok su koflana tui.
nimuyembekeza kuti zikule tsiku lomwelo ndi kuphukira maluwa mmawa mwake, komabe zimenezi sizidzakupindulirani pa tsiku la mavuto.
12 Mutunfacl kulana puspis ngisyak ke sie pusra oana ngirngir lun meoa, oana toki lun noa lulap weacn uh.
Aa, mkokomo wa anthu a mitundu yambiri, akusokosa ngati kukokoma kwa nyanja! Aa, phokoso la anthu a mitundu ina, akusokosa ngati mkokomo wa madzi amphamvu!
13 Mutunfacl uh ac rirme oana noa toki, tusruktu God El ac kaelos na elos foloki, pahleyukla oana kutkut pe eol uh, ku oana ke eng fohru uh pokak mah pao uh.
Ngakhale ankhondo a mitundu ina akubwera ndi mkokomo ngati wa madzi ambiri, koma adzathawira kutali Mulungu akadzawadzudzula. Yehova adzawapirikitsa ngati mankhusu owuluka ndi mphepo pa phiri, ndi ngati fumbi la kamvuluvulu asanayambe.
14 Ke eku uh elos aktuninfongye mwet uh, a ke lotutang elos wanginla. Pa ingan ma ac sikyak nu selos nukewa su utyak kunausla ac pisre ma in facl sesr uh.
Pofika nthawi yamadzulo zoopsa zidzayamba kuchitika, ndipo zidzakhala zitatha pofika mmawa. Izi ndizo zidzachitikire anthu otilanda zinthu, gawo la amene amatibera zinthu zathu.

< Isaiah 17 >