< Genesis 9 >

1 God El akinsewowoyal Noah ac wen tolu natul, ac fahk, “Kowos isusi, tuh fwilin tulik nutuwos fah puseni ac nwakla faclu nufon.
Ndipo Mulungu anadalitsa Nowa ndi ana ake aamuna nati kwa iwo, “Berekanani ndipo muchulukane ndi kudzaza dziko lapansi.
2 Kosro ac won ac ik nukewa ac fah moul in sangeng suwos. Ma inge nukewa ac fah oan ye ku lowos.
Nyama zonse za dziko lapansi, ndi mbalame zonse za mlengalenga, ndi chamoyo chilichonse chokwawa, ndiponso nsomba zonse za ku nyanja; zidzakuopani ndipo ndazipereka kuti muzilamulire.
3 Inge kowos ku in kang ma inge, oapana fokin ma kapak inima uh. Nga sot ma inge nukewa nu suwos kowos in mongo kac.
Tsopano chamoyo chilichonse chidzakhala chakudya chanu. Monga momwe ndinakupatsirani ndiwo zamasamba, tsopano ndikupatsaninso nyama iliyonse.
4 Ma se na ma kowos fah tia kang uh pa ikwa ma srakna oasr srah kac, mweyen moul uh oasr ke srah uh.
“Koma musamadye nyama imene ikanali ndi magazi oyenda.
5 Kutena mwet su eisla moul lun sie pac mwet, ac fah anwuki el. Kutena kosro ma eisla moul lun sie mwet, kalya nu sel pa misa.
Aliyense wopha munthu adzaphedwa, nyama iliyonse yopha munthu idzaphedwa, munthu aliyense wopha munthu mnzake, adzaphedwa.
6 Mwet uh orekla in luman God, ke ma inge kutena mwet su akmuseya sie mwet fah anwuki pac sin mwet.
“Aliyense wopha munthu, adzaphedwanso ndi munthu; pakuti Mulungu analenga munthu mʼchifanizo chake.
7 “Enenu in pukanten tulik nutuwos, tuh fwilin tulik nutuwos fah apunla fin faclu.”
Inu muberekane ndi kuchulukana kuti mudzaze dziko lonse lapansi ndi kuligonjetsa.”
8 God El fahk nu sel Noah ac wen tolu natul,
Mulungu anawuza Nowa ndi ana ake kuti,
9 “Inge nga oru sie wulela inmasrlosr, ac oayapa yurin fwilin tulik nutuwos,
“Tsopano Ine ndapangana ndi iwe ndi zidzukulu zako zamʼtsogolomo,
10 ac yurin won nukewa ac kosro nukewa — ma nukewa ma wi kowos tufoki liki oak uh.
pamodzi ndi zamoyo zonse, mbalame, ziweto ndi nyama zonse za kuthengo, ndi zonse zimene zinatuluka mʼchombo pamodzi ndi iwe.
11 Ke kas inge nga ac oru wulela luk yuruwos: nga wulela mu wangin sie pacl nga ac sifilpa kunausla ma su oasr moul la ke sronot. Faclu ac fah tia sifilpa kunausyukla ke sronot.
Pangano langa ndi ili: Ine ndilonjeza kuti sindidzawononganso zamoyo ndi madzi a chigumula. Chigumula sichidzawononganso dziko lapansi.”
12 Pa inge mwe akpwaye nu ke wuleang kawil se su nga oru yuruwos ac yurin ma moul nukewa inge,
Ndipo Mulungu anati, “Ine ndikupereka chizindikiro ichi cha pangano langa la pakati pa Ine ndi iwe, ana ako, zamoyo zonse, pamodzi ndi mibado ya mʼtsogolo.
13 nga filiya lelakem luk in pukunyeng uh. Ac fah mwe akul ke wuleang se inmasrlok ac faclu nufon nwe tok.
Ndayika utawaleza wanga mʼmitambo, ndipo chidzakhala chizindikiro cha pangano langa ndi dziko lapansi.
14 Kutena pacl ma nga afinya kusrao ke pukunyeng ac lelakem uh sikyak,
Nthawi zonse pakakhala mitambo mu mlengalenga ndipo utawaleza uwoneka,
15 nga fah esam wuleang luk nu suwos ac nu sin kosro nukewa, lah sronot ac fah tia sifil kunausla ma nukewa ma oasr moul la.
ndizikumbukira pangano langa pakati pa Ine ndi inu ndi zolengedwa zonse. Madzi sadzakhalanso chigumula chowononga dziko lapansi.
16 Pacl se lelakem uh sikyak in pukunyeng uh, nga ac fah liye ac esam wuleang kawil inmasrlok ac ma moul nukewa faclu.
Utawaleza ukamadzaoneka mʼmitambo, ndidzawuona ndi kukumbukira pangano losatha pakati pa Mulungu ndi zamoyo zonse pa dziko lapansi.”
17 Pa ingan akil lun wulela su nga oru nu sin ma oasr moul la nukewa.”
Choncho Mulungu anati kwa Nowa, “Ichi ndiye chizindikiro cha pangano limene ndalichita pakati pa Ine ndi zamoyo zonse pa dziko lapansi.”
18 Wen tolu natul Noah su tufoki liki oak uh pa Shem, Ham, ac Japheth. (Ham pa papa tumal Canaan.)
Ana aamuna a Nowa amene anatuluka mʼchombo muja anali Semu, Hamu ndi Yafeti. Hamu anali abambo ake a Kanaani.
19 Wen tolu natul Noah inge pa papa tumun mwet faclu nufon.
Ana aamuna a Nowa amenewa ndiwo anali makolo a anthu onse pa dziko lapansi.
20 Noah, su tuh sie mwet ima, pa mwet se oemeet ma tuh yukwiya ima in grape uh.
Nowa anali munthu woyamba kulima munda wamphesa.
21 Tukun el numla kutu wain uh, el sruhila, sarukla nuknuk lal, ac oan koflufolla in lohm nuknuk sel.
Tsiku lina pamene Nowa anamwako vinyo wa zipatso za mʼmundawo analedzera ndipo anavula zovala zake zonse ndi kugona mu tenti yake ali maliseche.
22 Ke Ham, papa tumal Canaan, el liyauk lah papa tumal el koflufolla oan, el illa ac fahkang nu sin tamulel luo wiel.
Hamu, abambo ake a Kanaani ataona kuti abambo ake ali maliseche anakawuza abale ake awiri aja omwe anali panja.
23 Na Shem ac Japheth eis nuknuk loeloes se ac filiya finpisaltal. Eltal kohloli nu in lohm nuknuk sac ac afinya papa tumaltal. Mutaltal ngetla lukel tuh eltal in tia liye koflufol lal.
Koma Semu ndi Yafeti anatenga chofunda nachiyika pa mapewa awo; ndipo anayenda chamʼmbuyo naphimba umaliseche wa abambo awo. Anafulatira kuti asaone umaliseche wa abambo awo.
24 Ke sruhi lal Noah uh sarla lukel ac el etauk ke ma wen se ma fusr natul el oru nu sel,
Nowa atadzuka, kuledzera kutatha, ndikudziwa zimene mwana wake wamngʼono wamwamuna uja anamuchitira,
25 el fahk, “Sie selnga nu facl Canaan! El ac fah sie mwet kohs nu sin tamulel lal.
anati, “Atembereredwe Kanaani! Adzakhala kapolo wa pansi kwenikweni kwa abale ake.”
26 Kaksakin LEUM GOD, God lal Shem! Canaan el ac fah mwet kohs lal Shem.
Anatinso, “Atamandike Yehova, Mulungu wa Semu! Kanaani akhale kapolo wa Semu.
27 God Elan akyokyelik acn lal Japheth! Lela fwilin tulik natul in puseni ac muta yurin mwet lal Shem. Canaan el ac fah mwet kohs lal Japheth.”
Mulungu akulitse dziko la Yafeti; Yafeti alandire madalitso pamodzi ndi Semu, ndipo Kanaani akhale kapolo wawo.”
28 Tukun sronot sac, Noah el moul yac tolfoko lumngaul,
Chitatha chigumula, Nowa anakhala ndi moyo zaka 350.
29 ac misa ke el yac eufoko lumngaul matwal.
Anamwalira ali ndi zaka 950.

< Genesis 9 >