< Genesis 39 >
1 Mwet Ishmael elos usalla Joseph nu Egypt ac kukakunulla nu sel Potiphar, sie sin mwet fulat lal tokosra, su sifen mwet topang su taran inkul sin tokosra.
Tsopano Yosefe anatengedwa kupita ku Igupto. Potifara Mwigupto amene anali mmodzi wa akuluakulu a Farao ndiponso mkulu wa asilikali olonda ku nyumba kwa Farao, anagula Yosefe kwa Aismaeli amene anapita naye kumeneko.
2 LEUM GOD El welul Joseph ac oru tuh ma nukewa el oru fahla wona ouiya. El muta yurin mwet kacto lal, sie mwet Egypt,
Koma Yehova anali ndi Yosefe ndipo zake zonse zimayenda bwino. Iye ankakhala mʼnyumba ya mbuye wake wa ku Igupto.
3 su liye tuh na LEUM GOD El welul Joseph, ac LEUM GOD El oru in wo ouiyal Joseph in ma nukewa el oru.
Mbuye wake anaona kuti Yehova anali naye Yosefe ndi kuti pa chilichonse chimene anachita Yehova ankaonetsetsa kuti achite bwino.
4 Potiphar el insewowo sel ac oru tuh elan mwet tutafpo lal. Ouinge el likilya elan leum fin lohm sel ac ma nukewa lal.
Potifara anakondwera ndi Yosefe chifukwa cha matumikiridwe ake. Choncho anamusandutsa woyangʼanira nyumba yake ndi zonse za mʼnyumba yake.
5 Tukun pacl sac lac, LEUM GOD El akinsewowoye sou lun mwet Egypt sac ac ma nukewa in lohm sel ac in ima lal, ke sripal Joseph.
Kuchokera pa nthawi imene anamuyika kukhala woyangʼanira wa nyumbayo ndi zonse za mʼnyumbamo, Yehova anadalitsa nyumba ya Mwiguptoyo chifukwa cha Yosefe. Madalitso a Yehova anali pa chilichonse chimene Potifara anali nacho, za mʼnyumba komanso za ku munda.
6 Potiphar el fuhleang ma nukewa lal nu ye karinginyuk lal Joseph, ac el tia elya ke kutena ma sayen in sulela ma nal sifacna. Joseph el arulana oasku ac wo lumahl,
Choncho anasiyira mʼmanja mwa Yosefe chilichonse chomwe anali nacho, kotero kuti samadandaula ndi chilichonse kupatula chakudya chimene ankadya. Tsopano Yosefe anali wa thupi labwino ndi wokongola.
7 ac tok kutu, mutan kien leum sac el mutawauk in lungseyak Joseph ac siyuk elan som oan yorol.
Patapita kanthawi, mkazi wa mbuye wake anayamba kusirira Yosefe nati, “Bwanji ugone nane!”
8 Joseph el srangesr, ac el fahk nu sin mutan sac, “Nge, wangin elya lun leum luk ke kutena ma in lohm sel, mweyen el lulalfongiyu. El se ngan karingin ma nukewa lal.
Koma iye anakana namuwuza kuti, “Inu mukuona kuti mbuye wanga sadandaula ndi kena kalikonse mʼnyumba muno, ndipo chawo chilichonse anachiyika mʼmanja mwanga.
9 Oasr ku luk in lohm se inge oana el, ac wangin kutena ma el sruok nu sik sayom. Fuka tuh ngan oru kain elahwet ingan ac orekma koluk lain God?”
Motero kuti palibe wina wamkulu kuposa ine mʼnyumba muno. Ndipo palibe chilichonse chimene mbuye wanga sanachipereke kwa ine kupatula inuyo, chifukwa ndinu mkazi wake. Tsono ndingachite bwanji choyipa choterechi ndi kuchimwira Mulungu?”
10 Mutan sac el ne kwafe nu sel Joseph pingana len elan oan yorol, a Joseph el tiana som welul oan.
Ndipo ngakhale kuti iye anayankhula mawu omwewa ndi Yosefe tsiku ndi tsiku, Yosefe sanalole kugona naye ngakhale kukhala naye pafupi.
11 Tusruktu sie len ah, ke Joseph el som in oru orekma lal in lohm sac, wangin mwet kulansap saya oasr we.
Tsiku lina Yosefe analowa mʼnyumbamo kukagwira ntchito zake, ndipo munalibe wina aliyense wantchito mʼnyumbamo.
12 Mutan sac sruokya nuknuk lal Joseph, ac fahk, “Fahsru oan yuruk.” A Joseph el kaingla nu likin lohm sac, sisla na nuknuk lal ah yurin mutan sac.
Mkazi uja anamugwira mkanjo Yosefe nati, “Tiye ugone nane!” Koma Yosefe anasiya mkanjo wake mʼmanja mwa mkaziyo nathawira kunja kwa nyumba.
13 Ke mutan sac el liye lah Joseph el sisla nuknuk lal ah ac kaingla nu lik ah,
Pamene mkazi uja anaona kuti Yosefe wamusiyira mkanjo wake mʼmanja mwake nathawira kunja kwa nyumba,
14 el pang nu sin mwet kulansap lal lohm sac, ac fahk, “Ngetma liye ma se nge! Mwet Hebrew se ma mukul tumuk ah use nu lohm uh el aklusrongtenye kut. El utyak nu infukil sik ah, ac srike in sruinkuiyu, tuh nga liksrenina wowoyak ke kuiyuk.
iye anayitana antchito ake a mʼnyumba nati, “Taonani mwamuna wanga anabwera ndi Mhebri uyu mʼnyumba muno kuti adzagone nane. Iyeyu analowa ku chipinda kwanga kuti adzagone nane ndipo ine ndinakuwa kwambiri.
15 Ke el lohng lah nga wowoyak, na el kaing nu likinuma, sisla nuknuk se lal inge siskuk.”
Atandimva ndikukuwa, anandisiyira mkanjo wakewu nʼkuthawira kunja.”
16 Mutan sac sruokya na nuknuk sac nwe ke na leum se lal Joseph ah tuku.
Tsono mkazi wa Potifara uja anasunga mkanjowo mpaka mbuye wake wa Yosefe atabwera ku nyumba.
17 Na el srumunang pac sramsram sac nu sel. El fahk, “Mwet kohs Hebrew sac, ma kom use nu inge ah, el utyak nu infukil sik uh ac nunku elan sruinkuiyu.
Tsono anamuwuza nkhaniyi nati: “Wantchito Wachihebri amene munatibweretsera uja anabwera kuti adzagone nane.
18 Tusruktu nga wowoyak, na el kaingla nu likinuma, sisla nuknuk lal ah siskuk.”
Koma pamene ndinakuwa, iye anandisiyira mkanjo wake nathawira kunja.”
19 Ke leum se lal Joseph el lohng ma mutan kial ac fahk inge, el foloyak,
Mbuye wake wa Yosefe atamva nkhani imene mkazi wake anamuwuza kuti, “Ndi zimene anandichitira wantchito wanu,” anapsa mtima kwambiri.
20 ac sap sruhu Joseph ac sisiyang el nu in presin, yen mwet kapir lun tokosra kapir we. Na el mutana we.
Tsono iye anatenga Yosefe namuyika mʼndende mmene ankasungiramo amʼndende a mfumu. Ndipo Yosefe anakhala mʼndendemo
21 Tusruktu LEUM GOD El welul Joseph ac akinsewowoyal, pwanang mwet liyaung presin el kulang nu sel.
koma Yehova anali naye, ndipo anamuonetsa kukoma mtima kwake, kotero kuti woyangʼanira ndende anakondwera ndi Yosefe.
22 El likilya Joseph elan sifen mwet kapir nukewa, ac sang elan fosrngakin ma nukewa ma orek in presin.
Choncho woyangʼanira ndende uja anamuyika Yosefe kukhala woyangʼanira onse amene anayikidwa mʼndende. Ndiponso anamupatsa udindo woyangʼanira zonse zochitika mʼndendemo.
23 Mwet liyaung presin el tia fosrngakin kutena ma su oan ye karinginyuk lal Joseph, mweyen LEUM GOD El welul Joseph ac oru in wo ouiyal ke ma nukewa el oru.
Woyangʼanira ndende uja sankayangʼaniranso china chilichonse chimene chinali mu ulamuliro wa Yosefe, chifukwa Yehova anali ndi Yosefe. Ndipo Yehova anaonetsetsa kuti chilichonse chimene Yosefe ankachita chimuyendere bwino.