< Genesis 27 >

1 In pacl se inge Isaac el matuoh ac mutawauk in sulonginla. El sapla solalma Esau, wen se ma matu natul, ac fahk nu sel, “Wen nutik!” Esau el topuk, “Nga inge.”
Isake atakalamba maso ake anachita khungu mwakuti sankatha kuona. Iye anayitana mwana wake wamkulu Esau nati kwa iye, “Mwana wanga.” Iye anayankha, “Ine abambo.”
2 Isaac el fahk, “Kom liye lah nga matuoh ac apkuran in misa.
Isake anati, “Tsopano ine ndakalamba, ndipo sindidziwa tsiku langa lakufa.
3 Us mwe pisr nutum an ac sruokma soko kosro inima an nak.
Tsono tenga zida zako, muvi wako ndi uta, pita kuthengo ukandiphere nyama.
4 Orauk kain in mongo yuyu se ma nga lungsena kang ah, ac use nu yuruk. Nga ac mongo tari, na nga fah akinsewowoyekomla meet liki nga misa.”
Undikonzere chakudya chabwino monga muja ndimakonderamu ndipo ubwere nacho kwa ine kuti ndidye ndi kuti ndikudalitse ndisanamwalire.”
5 Ke pacl se Isaac el kaskas nu sel Esau inge, Rebecca el lohng na. Ouinge ke Esau el illa som in sruh kosro,
Koma Rebeka amamvetsera pamene Isake amayankhula ndi mwana wake Esau. Esau atanyamuka kupita kuthengo kukaphera abambo ake nyama,
6 Rebecca el fahk nu sel Jacob, “Nga lohng lah ingena papa tomom fahk nu sel Esau ange:
Rebeka anati kwa mwana wake Yakobo, “Taona ndamva abambo ako akuwuza mʼbale wako Esau kuti,
7 ‘Use soko kosro inima an ac akmolyela nak. Tukun nga ac mongo tari, na nga ac akinsewowoye kom ye mutun LEUM GOD meet liki nga misa.’”
‘Bweretsere nyama yakutchire ndipo undikonzere chakudya chokoma kuti ndidye; kuti ndikudalitse pamaso pa Yehova ndisanamwalire.’
8 Rebecca el tafwela ac fahk, “Wen nutik, porongo akwoye ac oru ma nga fahk uh.
Tsopano mwana wanga, mvetsetsa ndipo uchite zimene ndikuwuze:
9 Fahla nu ke un kosro uh, ac srela lukwa nani fusr na fact an. Use ngan tuh akmolyela ac orala kain mongo se ma papa tomom el arulana lungse yohk ah.
Pita ku khola, ukatenge ana ambuzi abwino awiri, kuti ndikonzere abambo ako chakudya chokoma monga amakondera.
10 Kom ku in usla nu yorol elan kang, elan mau akinsewowoyekomla meet liki el misa.”
Kenaka upite nacho chakudyacho kwa abambo ako kuti adye ndi kukudalitsa asanafe.”
11 Tusruktu Jacob el fahk nu sin nina kial, “Kom etu na lah manol Esau unacna, a monuk fwel.
Koma Yakobo anati kwa Rebeka amayi ake, “Komatu mʼbale wanga Esau ndi munthu wa khungu la ubweya zedi, ndipo ine ndine munthu wa khungu losalala.
12 Papa el ac tuh kahl monuk ac konauk lah nga kiapwel. Ac fin ange, ac tia akinsewowoyeyuk nga, a el ac selngaiyuwi.”
Mwina abambo anga adzandikhudza, ndipo ndidzaoneka kuti ndawapusitsa. Tsono ndizadzitengera temberero mʼmalo mwa madalitso.”
13 Nina kial ah fahk, “Wen nutik, lela kutena selnga nu sum an in oan fuk. Oru na ma nga fahk uh. Fahla use nani an.”
Amayi ake anati kwa iye, “Mwana wanga, temberero limenelo ligwere ine. Iwe ungochita zimene ine ndikukuwuza; pita kanditengere timbuzito.”
14 Ouinge el som sruokya nani uh, ac use nu yurin nina kial, ac el orala kain mongo se ma papa sac arulana lungse ah.
Choncho anapita nakatenga timbuzito ndi kubwera nato kwa amayi ake. Choncho Rebeka anaphika chakudya chokoma monga momwe Isake amakondera.
15 Na Rebecca el srukak nuknuk se ma wo emeet lal Esau su oan yorol in lohm uh, ac sang nokmulang Jacob.
Tsono Rebeka anatenga zovala zabwino kwambiri za Esau mwana wake wamkulu zimene zinali mʼnyumba namuveka Yakobo.
16 El sang kulun nani uh nu fin paol Jacob, oayapa nu fin acn ma tia unacna ke kawal.
Anamuvekanso manja ake ndi khosi lake ndi zikopa za mwana wambuzi.
17 Na el sang mwe mongo yuyu sac, ac bread ma el munanla nu sel.
Kenaka, anamupatsa Yakobo chakudya chokoma chija chimene anaphika pamodzi ndi buledi.
18 Na Jacob el som nu yurin papa tumal ah, ac fahk, “Papa!” El topuk, “Nga inge. Su kac sumtal ingan?”
Yakobo anapita kwa abambo ake ndipo anati, “Abambo anga.” Ndipo anayankha, “Eya, kodi ndiwe mwana wanga uti?”
19 Jacob el fahk, “Nga Esau, wen matu nutum. Ma kom sap ngan orala nom ah pa inge. Tukakek mongoi, kom in tari akinsewowoyeyula.”
Yakobo anati kwa abambo ake, “Ndine Esau mwana wanu woyamba. Ndachita monga munandiwuzira. Chonde dzukani ndi kukhala tsonga kuti mudyeko nyama ndakukonzeraniyi kuti tsono mundidalitse.”
20 Isaac el fahk nu sin wen natul, “Ku kom oru fuka tuh kom arulana sa konauk?” Jacob el fahk, LEUM GOD lom El kasreyu konauk.”
Isake anafunsa mwana wake, “Wayipeza msanga chotere bwanji mwana wanga?” Iye anayankha, “Yehova Mulungu wanu anandithandiza kuti ndiyipeze.”
21 Isaac el fahk nu sel Jacob, “Kaluku ngan kahlkomi. Pwayena lah kom pa Esau?”
Pamenepo Isake anati kwa Yakobo, “Tabwera pafupi ndikukhudze mwana wanga, kuti ndidziwedi ngati uli mwana wanga Esau kapena ayi.”
22 Jacob el kalukyang nu yurin papa tumal ah, na Isaac el kahlilya ac fahk, “Pusrem oana pusracl Jacob, a poum paol Esau.”
Yakobo anasendera kufupi ndi abambo ake Isake ndipo anamukhudza nati, “Mawuwa ndi mawu a Yakobo koma mikonoyi ndi mikono ya Esau.”
23 El tiana akilenul Jacob, mweyen paol oana paol Esau. El akola elan akinsewowoyal,
Sanamuzindikire, popeza mikono yake inali ndi ubweya ngati ya mʼbale wake Esau; choncho anamudalitsa.
24 na el sifilpa siyuk, “Ku pwayena kom pa Esau?” Ac el topuk, “Aok, pwaye.”
Isake anafunsa, “Kodi ndiwedi mwana wanga Esau?” Yakobo anayankha, “Inde ndine.”
25 Isaac el fahk, “Kolma mongo an nu yuruk ngan kang. Nga ac mongo tari, na nga fah akinsewowoyekomla.” Jacob el kolang nu yorol, ac el oayapa sang wain nimal.
Ndipo iye anati, “Mwana wanga, patseko nyama yakoyo ndidye kuti ndikudalitse.” Yakobo anabwera ndi nyama ija kwa Isake ndipo anadya. Kenaka anamupatsanso vinyo ndipo anamwa.
26 Na papa tumal ah fahk nu sel, “Kaluku, wen nutik, ac ngokya mutuk.”
Tsono Isake anati kwa Yakobo, “Bwera kuno mwana wanga undipsompsone.”
27 Ac ke el kalukyang in ngok mutal, Isaac el ngokak nuknuk lal, ouinge el akinsewowoyalla. Ac el fahk, “Foulin wen nutik uh loslos oana foulin ima ma LEUM GOD El akinsewowoye.
Choncho anapita namupsompsona. Apa Isake anamva fungo la zovala zake, ndipo anamudalitsa nati, “Haa, fungo la mwana wanga lili ngati fungo la munda umene Yehova waudalitsa.
28 God Elan asot nu sum aunfong inkusrao me, ac akkasrupye fohkon acn in ima lom! Ac lela Elan akpusye wheat ac wain lom!
Mulungu akugwetsere mame akumwamba ndipo minda yako ibale tirigu wambiri ndi vinyo watsopano.
29 Mutunfacl puspis in kulansap nu sum, ac mwet uh in faksufi ye motom. Lela kom in leum fin sou lom nukewa, ac fwilin tulik nutin nina kiom in akfulatye kom. Lela elos su selngawi kom in selngawiyuk, ac elos su akinsewowoye kom in akinsewowoyeyuk.”
Mitundu ya anthu ikutumikire iwe ndipo anthu akugwadire iwe. Ukhale wolamula abale ako, ndipo ana aamuna a amayi ako akugwadire. Amene akutemberera iwe atembereredwe ndipo amene adalitsa iwe adalitsike.”
30 Isaac el akinsewowoyela Jacob tari, na Jacob el tuyak som. Tia paht na Esau, tamulel lal, el foloko liki sruh kosro lal.
Isake atatsiriza kudalitsa Yakobo, atangochoka pamaso pa abambo akewo, Esau anabwera kuchokera kosaka kuja.
31 El oayapa akmolyela mwe mongo na yuyu ac usla nu yurin papa tumal. Ac el fahk, “Papa, tukakek kang kutu ikwen kosro nga us tuku nom inge, kom in tari akinsewowoyeyula.”
Nayenso anakonza chakudya chokoma nabwera nacho kwa abambo ake. Ndipo anati kwa iye, “Chonde abambo, dzukani mukhale tsonga kuti mudye nyamayi ndi kuti mundidalitse.”
32 Ac Isaac el siyuk, “Ku su kom an?” Ac Esau el fahk, “Nga Esau, wounse mukul nutum.”
Abambo ake, Isake, anamufunsa kuti, “Ndiwe yani?” Iye anayankha, “Ndine mwana wanu woyamba Esau.”
33 Manol Isaac nufon rarrarak, ac el siyuk, “Fin angan, ac su sruhk uniya kosro soko use nak ah? Nga mongo tufahna tari na pa kom utyak. Nga sang nufon mwe insewowo luk nu sel, ac inge ac ma na lal nwe tok.”
Isake ananjenjemera kwambiri nati, “Nanga ndani uja anakapha nyama kutchire nʼkudzandipatsa? Ine ndadya kale, ndadya nyamayo iwe utangotsala pangʼono kubwera ndipo ndamudalitsa ndipo adzakhaladi wodalitsika.”
34 Ke Esau el lohng ma inge, el liksreni tung ac wowoyak, ac fahk, “Papa, akinsewowoyeyu pac!”
Esau atamva mawu a abambo ake, analira mokweza ndi mowawidwa mtima nati kwa abambo ake, “Inenso dalitseni abambo anga!”
35 Isaac el fahk, “Tamulel lom el tuku ac kiapweyula. El eisla tari mwe insewowo lom.”
Koma iye anati, “Mʼbale wako anabwera mwachinyengo ndipo watenga madalitso ako.”
36 Esau el fahk, “Pacl luola el aklalfonyeyu. Fal in pangpang inel Jacob. El eisla wal lun wounse luk, ac inge el eisla pac mwe insewowo luk. Ya wangin na pwaye mwe insewowo lula kom filiya luk?”
Esau anati, “Kodi nʼchifukwa chake iyeyu dzina lake lili Yakobo eti? Aka nʼkachiwiri kundinyenga: Anatenga ukulu wanga, pano watenga madalitso anga!” Kenaka anafunsa, “Kodi simunandisungireko ena madalitsowo?”
37 Isaac el topuk, “Nga orala tari elan leum fom, ac tuh mwet wial nukewa fah mwet kulansap lal. Nga sang nu sel wheat ac wain. Inge, wen nutik, wangin ma nga ku in oru nu sum!”
Koma Isake anamuyankha nati, “Ndamudalitsa iye kuti akhale wokulamulira iwe. Ndaperekanso abale ake onse kuti akhale omutumikira iye, ndipo ndamudalitsa ndi tirigu wambiri, ndi vinyo watsopano. Ndiye ndingakuchitirenso chiyani mwana wanga?”
38 Esau el sifil pacna kwafe nu sin papa tumal ah, ac fahk, “Ya mwe insewowo sefanna lom, papa? Akinsewowoyeyu pac!” Na el sifilpa tung.
Esau anati kwa abambo ake, “Kodi muli ndi dalitso limodzi lokhali, abambo anga? Inenso mundidalitse chonde abambo anga!” Pomwepo Esau analira mokuwa.
39 Na Isaac el fahk nu sel, “Wangin aunfong nu sum inkusrao me, Wangin acn wo ke ima uh lom.
Tsono Isake abambo ake anamuyankha kuti, “Malo ako okhalapo sadzabala dzinthu, ndipo mvula sidzagwa pa minda yako.
40 Cutlass nutum pa ac sot enenu lom, Ac kom fah kulansupu tamulel lom. Tusruktu kom fin tuyak lainul, Kom ac fah pisrla liki ye nununku lal.”
Udzakhala ndi moyo podalira lupanga ndipo udzatumikira mʼbale wako. Koma idzafika nthawi pamene udzakhala mfulu udzachotsa goli lake mʼkhosi mwako.”
41 Esau el arulana srungalla Jacob, mweyen papa tumal ah tuh sang mwe insewowo ah nu sel. Ac el nunku sel sifacna, “Akuranna sun pacl in eoksra ke misa lal papa. Fin safla, na nga ac unilya Jacob.”
Ndipo Esau anamusungira chiwembu Yakobo chifukwa cha madalitso amene abambo ake anamupatsa. Esau anati kwa iye yekha, “Masiku olira abambo anga ayandikira; pambuyo pake ndidzamupha mʼbale wangayu Yakobo.”
42 Tusruktu ke Rebecca el lohng ke akoo lal Esau ah, el sapla solalma Jacob ac fahk nu sel, “Esau tamulel lom, el akoo in foloksak nu sum ac unikomi.
Pamene Rebeka anamva zimene mwana wake wamkulu Esau ankaganiza, anayitanitsa Yakobo nati kwa iye, “Mʼbale wako Esau akulingalira zakuti akuphe kuti akulipsire.
43 Wen nutik, inge kom oru ma nga fahk uh. Fahla ingena nwe yorol Laban tamulel luk in acn Haran,
Tsopano mwana wanga, chita zimene ndinene: Nyamuka tsopano, uthawire kwa mlongo wanga Labani ku Harani.
44 ac muta yorol nwe ke na kasrkusrak lun tamulel lom ohula
Ukakhale naye kwa kanthawi mpaka mkwiyo wa mʼbale wako utatsika.
45 ac el mulkunla ma kom oru nu sel inge. Tok nga ac fah supwaot sie mwet in folokinkomme. Mwe mea wen luo nutik in tukenina wanginla ke len sefanna?”
Tsono mkwiyo wa mʼbale wakoyo ukadzatsika ndi kuyiwala zonse wamuchitirazi, ndidzatuma munthu kuti adzakutenge. Nanga nditayirenji nonse awiri nthawi imodzi?”
46 Rebecca el fahk nu sel Isaac, “Nga keokla sin mutan Hit kial Esau inge. Jacob el fin payukyak pac sin sie mutan Hit, ac mansis pacna ngan tari misa.”
Tsono Rebeka anati kwa Isake, “Ine sindikukondwera nawo anamwali a Chihiti. Ndipo ngati Yakobo angapeze mbeta kuno mwa anamwali a Chihitiwa, ndiye kuli bwino kungofa.”

< Genesis 27 >