< Genesis 25 >

1 Abraham el payukyak sin sie pac mutan, inel pa Keturah.
Abrahamu anakwatira mkazi wina dzina lake Ketura.
2 Keturah el oswela nu sel Abraham: Zimran, Jokshan, Medan, Midian, Ishbak, ac Shuah.
Iyeyu anamubalira Zimurani, Yokisani, Medani, Midiyani, Isibaki ndi Suwa.
3 Jokshan pa papa tumal Sheba ac Dedan, ac fwilin tulik natul Dedan pa mwet Asshurim, mwet Letushim ac mwet Leummim.
Yokisani anabereka Seba ndi Dedani ndipo zidzukulu za Dedani ndiwo Aasuri, Aletusi, ndi Aleumi.
4 Wen natul Midian pa Ephah, Epher, Hanoch, Abida, ac Eldaah. Elos inge nukewa ma tuku kacl Keturah.
Ana aamuna a Midiyani anali, Efai, Eferi, Hanoki, Abida ndi Elida. Onsewa anali zidzukulu za Ketura.
5 Abraham el filiya ma nukewa lal nu sel Isaac,
Abrahamu anasiyira Isake chilichonse anali nacho.
6 tusruktu ke el srakna moul, el sang pac mwe kite nu sin wen natul ma mutan kulansap kial elos oswela nu sel. Na el supwala wen natul inge nu in sie facl layen nu kutulap, tuh elos in muta loes lukel Isaac wen natul.
Koma pamene anali ndi moyo, Abrahamu anapereka mphatso kwa ana aakazi ake ena onse. Kenaka anawatumiza ku dziko la kummawa kuti akhale kutali ndi mwana wake Isake.
7 Pa inge lusen moul lal Abraham: yac siofok itngoul limekosr.
Abrahamu anakhala ndi moyo zaka 175.
8 Abraham el sisla mong safla lal ac misa ke el arulana matuoh.
Abrahamu anamwalira atakalamba kwambiri ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake.
9 Isaac ac Ishmael, wen luo natul, eltal piknilya in Luf Machpelah in acn mwesas kutulap in Mamre, su tuh ma lal Ephron wen natul Zohar, mwet Hit.
Ana ake, Isake ndi Ismaeli anamuyika mʼphanga la Makipela pafupi ndi Mamre, mʼmunda umene kale unali wa Efroni mwana wa Zohari Mhiti,
10 Pa inge ipin acn se ma Abraham el tuh molela sin mwet Hit ah. Abraham ac Sarah, mutan kial, eltal kewa pukpuki we.
uwu ndi munda umene Abrahamu anagula kwa Ahiti. Kumeneko Abrahamu anakayikidwa pamodzi ndi mkazi wake Sara.
11 Tukun Abraham el misa, God El akinsewowoyal Isaac wen natul, su muta fototo nu ke acn se pangpang “Lufin Kof Lun El Su Moul Ac Liyeyu.”
Atamwalira Abrahamu, Mulungu anadalitsa mwana wake Isake, amene ankakhala pafupi ndi Beeri-lahai-roi (chitsime cha Wamoyo Wondipenya).
12 Pa inge wen natul Ishmael, su Hagar, mutan kulansap Egypt lal Sarah, el tuh oswela nu sel Abraham.
Nazi zidzukulu za Ismaeli, mwana wa Abrahamu amene wantchito wa Sara, Hagara Mwigupto uja, anaberekera Abrahamu.
13 Takla inelos fal nu ke matwalos: Nebaioth, Kedar, Adbeel, Mibsam,
Awa ndi mayina a ana a Ismaeli monga mwa mndandanda wa mabadwidwe awo: Nebayoti ndiye anali mwana woyamba wa Ismaeli; kenaka Kedara, Adibeeli, Mibisamu,
14 Mishma, Dumah, Massa,
Misima, Duma, Masa,
15 Hadad, Tema, Jetur, Naphish, ac Kedemah.
Hadadi, Tema, Yeturi, Nafisi ndi Kedema;
16 Elos pa papa tumun sruf singoul luo, ac inelos itukyang nu ke inen acn elos muta we ac nien aktuktuk lalos.
Amenewa ndi ana a Ismaeli ndi mayina awo monga mwa midzi ndi misasa yawo. Anali olamulira mafuko khumi ndi awiri.
17 Ishmael el tuh yac siofok tolngoul itkosr ke el misa.
Ismaeli anakhala ndi moyo zaka 137. Iye anamwalira ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake.
18 Fwilin tulik natul Ishmael muta inmasrlon Havilah ac Shur, layen kutulap in acn Egypt, ke inkanek nu Assyria. Elos muta srengla liki tulik natul Abraham saya.
Zidzukulu za Ismaeli zinkakhala mʼdera la pakati pa Havila ndi Suri, kummwera kwa Igupto, mukamapita cha ku Asuri. Choncho anakhala kummawa kwa abale awo.
19 Pa inge sramsram kacl Isaac wen natul Abraham.
Iyi ndi mbiri ya Isake mwana wa Abrahamu. Abrahamu anabereka Isake
20 Isaac el yac angngaul ke el payukyak sel Rebecca, acn natul Bethuel (sie mwet Aram ke acn Mesopotamia), ac el ma lohl Laban.
ndipo Isake anali ndi zaka makumi anayi pamene anakwatira Rebeka mwana wa Betueli Mwaramu wa ku Padanaramu mlongo wa Labani Mwaramu.
21 Ke sripen wangin tulik natul Rebecca, Isaac el pre nu sin LEUM GOD kacl. LEUM GOD El topuk pre lal, ac Rebecca el pitutuyak.
Isake anapempherera mkazi wake kwa Yehova popeza iye anali wosabereka. Yehova anayankha pemphero lake ndipo mkazi wake Rebeka anatenga pathupi.
22 Fak se pa insial, ac meet liki eltal isusla eltal amei na insien nina kialtal. Rebecca el fahk, “Efu ku sikyak ange nu sik?” Ouinge el som siyuk sin LEUM GOD kac.
Koma pamene anawo amalimbana mʼmimba mwake, iye anati, “Bwanji zikundichitikira zoterezi?” Choncho anapita kukafunsa kwa Yehova.
23 LEUM GOD El fahk nu sel, “Mutunfacl luo oasr in kom. Kom ac oswela mutunfacl akwasui luo. Sie ac fah ku liki ma se ngia. El su matu ac fah kulansupu el su fusr.”
Yehova anati kwa iye, “Udzabala mafuko awiri a anthu olimbana, ndipo magulu awiri a anthu ochokera mwa iwe adzasiyana; fuko limodzi lidzakhala la mphamvu kuposa linzake, ndipo wamkulu adzatumikira wamngʼono.”
24 Ke sun pacl in isus lal ah, el oswela fak mukul se.
Pamene nthawi inakwana yakuti abeleke, Rebeka anaberekadi mapasa.
25 Tulik se meet ah srusra manol, ac kolol arulana unacna oana sie nuknuk manan, ke ma inge itukyang inel Esau.
Woyamba kubadwa anali wofiira, ndipo thupi lake lonse linali ngati chovala cha ubweya; choncho anamutcha Esau.
26 Tulik se akluo el isusla tuh na el sruokna kapinnial Esau. Ouinge itukyang inel Jacob. Isaac el yac onngoul ke eltal isusla.
Kenaka mʼbale wake anabadwa atagwira chidendene cha Esau; choncho anamutcha Yakobo. Isake anali ndi zaka 60 pamene Rebeka anabereka mapasawa.
27 Tulik mukul luo ah matula, ac Esau el mwet na etu sruh kosro se, ac el lungsena muta inimae, a Jacob el sukas ac el mutana in lohm uh.
Anyamatawo anakula ndipo Esau anakhala katswiri wosaka, munthu wamʼthengo, pamene Yakobo anali munthu wofatsa, wokonda kukhala pa nyumba.
28 Isaac el kuloel Esau, mweyen el lungse kang kosro inima ma Esau el muta sruok uh, a Rebecca el kuloel Jacob.
Isake ankakonda Esau chifukwa cha nyama za kutchire zomwe ankakonda kudya, koma Rebeka ankakonda Yakobo.
29 Sie len ah ke Jacob el orek sup nal, Esau el foloko liki sruh kosro lal. El masrinsralla
Tsiku lina pamene Yakobo ankaphika chakudya, Esau anabwera kuchokera kuthengo ali wolefuka ndi njala.
30 ac el fahk nu sel Jacob, “Nga ngulla na pwaye. Se nak kutu mongo srusra kom oru ingan.” (Pa ingan sripa se oru pangpang inel Edom.)
Iye anati kwa Yakobo, “Tandipatsako phala lofiiralo, ndimwe! Ndalefuka ndi njala.” (Nʼchifukwa chake amatchedwanso Edomu).
31 Jacob el topkol ac fahk, “Nga ac kite kom kom fin ase nu sik wal lun wounse lom.”
Yakobo anayankha, “Choyamba undigulitse ukulu wako.”
32 Esau el fahk, “Kwal aok. Nga akura misa — mwe mea wal sac nu sik?”
Esau anati, “Chabwino, ine ndatsala pangʼono kufa, ukulu undithandiza chiyani?”
33 Ac Jacob el fahk, “Fulahk nu sik lah kom ac se nu sik wal lom an.” Esau el fulahk ac kitala wal lal nu sel Jacob.
Koma Yakobo anati, “Lumbira kwa ine choyamba.” Kotero Esau analumbiradi, ndipo anagulitsa ukulu wake kwa Yakobo.
34 Na Jacob el sang kutu bread ac kutu sup uh nal. El mongoi tari na el tuyak som. Pa na ingan luman pilesreyen wal se lal Esau ah sel.
Choncho Yakobo anamupatsa Esau buledi ndi phala lofiira lija. Iye anadya ndi kumwa, nanyamuka kumapita. Motero Esau anapeputsa ukulu wake wachisamba uja.

< Genesis 25 >