< Ezekiel 8 >

1 Ke len aklimekosr in malem akonkosr ke yac akonkosr ma kut muta in sruoh, mwet kol lun mwet sruoh Judah elos wiyu muta in lohm sik. In kitin pacl ah, ku lun LEUM GOD Fulatlana tuku nu fuk.
Tsiku lachisanu la mwezi wachisanu ndi chimodzi, mʼchaka chachisanu ndi chimodzi, ndinakhala mʼnyumba mwanga pamodzi ndi akuluakulu a ku Yuda. Tsono mphamvu za Ambuye Yehova zinandifikira.
2 Nga ngetak ac liye sie aruruma oana luman mwet se. Infulwali nu ten oana luman e uh, ac infulwalyak nu lucng saromrom oana in bronze akmusrala.
Nditayangʼana ndinangoona chinthu chooneka ngati munthu. Kuchokera pamene pamaoneka ngati chiwuno chake kumatsika mʼmunsi anali ngati moto, ndipo kuchokera mʼchiwuno kukwera mmwamba amaoneka mowala ngati mkuwa wonyezimira.
3 El asroema luman pao se ac sruokya aunsifuk. Ke aruruma se inge, ngun lun God srukyuyak nu yen engyeng uh ac usyula nu Jerusalem. El usyula nu ke nien utyak layen nu epang ke kalkal se oan loac in Tempul, yen ma sruloala se oan we su akkasrkusrakye God.
Iye anatambasula chinthu chooneka ngati dzanja ndipo anagwira tsitsi la pamutu panga. Nthawi yomweyo Mzimu unandikweza mlengalenga. Tsono ndikumachita ngati ndikuona Mulungu kutulo, Mzimu uja unapita nane ku Yerusalemu nundiyika pa khomo la chipata chamʼkati choyangʼana kumpoto. Kumeneko kunali fano limene limaputa mkwiyo wa Mulungu.
4 Ac nga liye kalem saromrom se ma akkalemye lah God lun Israel oasr we, oana nga tuh liyauk ke nga tu pe Infacl Chebar.
Kumeneko ndinaona ulemerero wa Mulungu wa Israeli ngati momwe ndinaonera mʼmasomphenya mʼchigwa muja.
5 God El fahk nu sik, “Mwet sukawil moul la, ngetla nu epang.” Ke nga ngetla nga liyauk ma sruloala se su akkasrkusrakye God, oan apkuran nu ke loang se ke mutunoa in utyak ke mutunpot uh.
Tsono Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, tayangʼana kumpoto.” Choncho ndinayangʼana kumpoto ndipo ndinaona pa khomo la chipata pafupi ndi guwa lansembe ndinaona fano loputa mkwiyo wa Mulungu lija.
6 God El fahk nu sik, “Mwet sukawil, ku kom liye ma sikyak inge? Liye ma srungayuk mwet Israel elos oru in acn inge, pwanang nga som loes liki acn mutal sik. Kom ac fah liye kutu mwe mwekin yohk liki na ma inge.”
Ndipo Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi ukuona zimene akuchitazi, zonyansa zazikulu zimene Aisraeli akuchita kuno, zinthu zondichotsa Ine kumalo anga opatulika? Koma iwe udzaona zinthu zimene zili zonyansa kwambiri.”
7 El usyula nu ke mutunoa se lik ah, ac srisrngiya pat se ke pot uh.
Kenaka Iye anandipititsa ku khomo lolowera ku bwalo la Nyumba ya Mulungu. Nditayangʼanitsitsa ndinangoona dzenje pa khomapo.
8 El fahk, “Mwet sukawil, foklalik pat sacn, ac tilyak kac.” Na nga fukulya ac konauk srungul se.
Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, tsopano bowola pa khomapo.” Ndinabowoladi pa khomapo ndipo ndinapezapo khomo.
9 El fahk nu sik, “Utyak ac liye ouiya koluk elos oru we.”
Ndipo Yehova anandiwuza kuti, “Lowa, ndipo ona zinthu zonyansa zimene akuchita pamenepa.”
10 Na nga utyak ac liye pesinka ah sroalla ke wet ac kutu pac kain in kosro ma tia nasnas, oayapa kutu ma saya ma mwet Israel uh alu nu kac.
Motero Ine ndinalowa ndi kuyangʼana, ndipo ndinaona pa makoma onse zithunzi za zinthu zosiyanasiyana zokwawa pansi, za nyama zonyansa ndiponso za mafano onse amene Aisraeli ankapembedza.
11 Mwet kol itngoul lun mwet Israel uh muta we, ac Jaazaniah wen natul Shaphan el tu inmasrlolos. Kais sie selos sruok mwe akok mwe keng, ac kulasr uh fosryak liki mwe keng ah.
Patsogolo pa zimenezi panayima akuluakulu makumi asanu ndi awiri a Aisraeli, ndipo Yaazaniya mwana wa Safani anali atayima pakati pawo. Aliyense wa iwo anali ndi chofukizira lubani mʼdzanja lake ndipo utsi wa fungo lokoma la lubani unkafuka.
12 God El siyuk sik, “Mwet sukawil, kom liye ma mwet kol lun mwet Israel elos oru in lukma inge? Elos nukewa tukeni alu in sie fukil sessesla ke ma sruloala. In nunak tafongla lalos elos mu, ‘LEUM GOD El tia liye kut! El som liki facl se inge.’”
Tsono Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi waona zimene akuluakulu a Aisraeli akuchita mu mdima, aliyense akupembedza fano lakelake mʼnyumbamo? Iwo akuti, ‘Yehova sakutiona; Yehova walisiya dziko!’
13 Na LEUM GOD El fahk nu sik, “Kom ac liye ke elos ac oru ma koluk yohk liki na ma ingan.”
Iye anandiwuzanso kuti, ‘Iwe udzawaonanso akuchita zinthu zonyansa kwambiri.’”
14 Ouinge El usyula nu nien utyak layen epang in Tempul, ac fahkak nu sik kutu mutan su tungi misa lun god se pangpang Tammuz.
Kenaka anapita nane pa khomo la ku khomo la chipata cha Nyumba ya Mulungu choyangʼana kumpoto, ndipo kumeneko ndinaona akazi ena atakhala pansi, akulira mulungu wawo wotchedwa Tamuzi.
15 God El siyuk sik, “Mwet sukawil, ku kom liye ma inge? Kom ac liye pac kutu ma arulana koluk liki ma inge.”
Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi ukuziona zimenezi? Iwe udzaona zinthu zimene zili zonyansa kwambiri kuposa izi.”
16 Ac el usyula nu in kalkal se oan loac ke Tempul, nu ke acn se ma apkuran nu ke nien utyak lun acn mutal, inmasrlon loang sac ac sawalsrisr uh. Oasr mukul longoul limekosr we su totulikla liki acn mutal. Elos faksufi nu kutulap ac alu nu ke faht ke takak ah.
Kenaka Iye anapita nane mʼkati mwa bwalo la Nyumba ya Yehova. Kumeneko ku khomo lolowera ku Nyumba ya Yehova pakati pa khonde ndi guwa lansembe, panali amuna 25. Anafulatira Nyumba ya Mulungu wa Yehova ndipo nkhope zawo zinaloza kummawa, ndipo ankapembedza dzuwa choyangʼana kummawa.
17 LEUM GOD El fahk nu sik, “Mwet sukawil, ku kom liye ma ingan? Mwet Judah inge tiana falkin orekma koluk ac mwe mwekin ma kom liye inge, oayapa inkanek sulallal elos oru apunla facl se inge nufon, a elos tuku na nwe inkul lun Tempul ac oru, pwanang upala kasrkusrak luk uh. Liye ke elos orek pirakak nu sik ke lumah na koluk elos oru!
Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi waziona zimenezi? Kodi nʼchinthu chopepuka kuti anthu a ku Yuda azichita zonyansa zimene akuchitazi pano? Kodi afike mpaka pomafalitsa za ndewu mʼdziko lonse? Iwotu akuwutsa ukali wanga. Akundipsetsa mtima ndi zochita zawo!
18 Elos ac pula fulen kasrkusrak luk uh. Nga ac tiana molelosla ku pakomutalos. Elos ac pre nu sik ac wowoyak ke kuiyalos, a nga ac tiana lohng.”
Choncho Ine ndidzawalanga ndili wokwiya. Sindidzawamvera chisoni kapena kuwaleka. Ngakhale atandifuwulira mʼmakutu mwanga sindidzawamvera.”

< Ezekiel 8 >