< Ezekiel 10 >

1 Nga ngetla liye ma raun se ma oan lucng liki sifen cherub akosr uh, na lucng liki ma inge nga liye ma se oana in tron se orekla ke eot sapphire.
Ine nditayangʼana ku thambo limene lili pamwamba pa mitu ya akerubi ndinangoona chinthu chooneka ngati mpando waufumu wa mwala wa safiro.
2 God El fahk nu sin mukul se ma nukum nuknuk linen, “Fahsrot inmasrlon wheel ye cherub uh, ac nwakla inpoum ke mulut firir, ac sisalik mulut ingan nu in siti uh.” Nga liyal ke el fahla.
Tsono Yehova anawuza munthu wovala chovala chabafuta uja kuti, “Pita pakati pa mikombero kunsi kwa akerubi. Udzaze manja ako ndi makala oyaka amene ali pakati pa akerubiwo ndipo uwawaze mu mzinda.” Iye anachita zimenezi ine ndikuona.
3 Ac cherub uh tu layen nu eir in Tempul ke el utyak, na sie pukunyeng nwakla luin kalkal se oan loac ke Tempul.
Apa akerubiwo anali atayima mbali ya kummwera kwa Nyumba ya Mulungu pamene munthuyo ankalowa. Tsono mtambo unadzaza bwalo lamʼkati.
4 Kalem saromrom se, ma akkalemye lah LEUM GOD El oasr, sowak liki fin cherub uh ac mukuila nu ke nien utyak nu in Tempul. Pukunyeng sac nwakla luin Tempul, ac in kalkal sac arulana saromrom ke kalem wolana lun LEUM GOD.
Ndipo ulemerero wa Yehova unachoka pamwamba pa akerubi ndipo unafika ku chiwundo cha Nyumba ya Mulungu. Mtambo unadzaza Nyumba ya Mulungu, ndipo kuwala kwa ulemerero wa Yehova kunadzaza bwalolo.
5 Kusen pikpik ke posohksok lun cherub uh, su oana pusren God Kulana, lohngyuk e likin kalkal ah.
Phokoso la mapiko a akerubi limamveka mpaka ku bwalo lakunja, monga momwe linamvekera liwu la Mulungu Wamphamvuzonse akamayankhula.
6 Ke LEUM GOD El sapkin nu sin mukul se ma nukum nuknuk linen elan eis kutu mulut firir su oan inmasrlon wheel ye cherub uh, na mwet sac utyak ac tu pe sie wheel inge.
Kenaka Yehova analamula munthu wovala chovala chabafuta uja kuti, “Pala moto pakati pa mikombero, pakati pa akerubi.” Munthu uja anapitadi nakayima pa mbali pa mkombero umodzi.
7 Sie sin cherub uh el saplakla nu ke e se ma oan inmasrlolos, ac lafusak kutu mulut firir ac filiya inpoun mukul se su nukum nuknuk linen. Na el eis ac som.
Ndipo mmodzi wa akerubi anatambalitsa dzanja lake mpaka pa moto umene unali pakati pawo. Iye anapalako motowo ndipo anapatsa munthu wovala chovala chabafuta uja. Tsono iye anawulandira natuluka.
8 Nga liye tuh kais sie cherub inge oasr pao se oana poun mwet uh oan ye kais sie posohksok lalos.
Ndiye kuti kunsi kwa mapiko akerubi kumaoneka zinthu zooneka ngati manja a munthu.
9 Nga liye pac lah oasr wheel akosr ingo, kewana oana sie — kais sie wheel oan sisken kais sie cherub.
Ine nditayangʼanitsitsa ndinaona mikombero inayi pambali pa akerubi. Pambali pa kerubi aliyense panali mkombero umodzi; mikomberoyo inkanyezimira ngati miyala yokongola ya krizoliti.
10 Wheel inge saromrom oana wek saok uh, ac kais sie wheel oasr pac sie wheel pitukelik loac.
Maonekedwe a mikombero inayi ija anali ofanana. Mkombero uliwonse umaoneka ngati mkombero wolowana ndi unzake.
11 Ke pacl cherub inge ac mukuiyak elos ku in fahsr nu meet, nu tok, nu lasa ku nu layot ac tiana forla. Elos ac tukenina mukui nu ke acn elos lungse som nu we, ac tia enenu in forla.
Poyenda akerubiwo, amapita mbali iliyonse ya mbali zinayizo kumene akerubiwo amayangʼana. Mikomberoyo simatembenuka pamene akerubiwo ankayenda. Kulikonse kumene mutu walunjika nʼkumene ankapita popanda kutembenuka.
12 Manolos, fintokolos, paolos, posohksok lalos, ac wheel kaclos, afyufla ke atronmuta.
Matupi awo onse, misana yawo, manja awo ndi mapiko awo zinali ndi maso okhaokha, monganso mʼmene inalili mikombero yawo inayi ija.
13 Nga lohng ke pusra se pangon wheel inge, “Wheel for.”
Ine ndinamva mikombero ikutchedwa kuti, “mikombero yakamvuluvulu.”
14 Kais sie cherub inge oasr muta akosr kac. Ma se meet mutun cow mukul, ma se akluo mutun mwet, ma se aktolu mutun lion, ac ma se akakosr mutun eagle.
Kerubi aliyense anali ndi nkhope zinayi. Nkhope yoyamba inali ya Kerubi, nkhope yachiwiri inali ya munthu, nkhope yachitatu inali ya mkango ndipo nkhope yachinayi inali ya chiwombankhanga.
15 (Nuna ma orekla moul ma nga tuh liye pe Infacl Chebar ah pa inge.) Ke pacl se cherub inge sohkak nu yen engyeng uh
Tsono akerubi aja anawuluka. Izi zinali zamoyo zija zimene ndinaziona ku mtsinje wa Kebara.
16 ac mukuila, na wheel inge ac welulos. Pacl nukewa ma elos ac asroelik posohksok lalos in sohkak, wheel inge ac welulos pac.
Pamene akerubi ankayenda, nayonso mikombero ya mʼmbali mwawo inkayenda. Akerubiwo ankati akatambasula mapiko awo kuti auluke mikombero sinkachoka mʼmbali mwawo.
17 Ke pacl elos ac tui uh, na wheel uh ac tui pac. Ac ke elos ac sohkla, wheel inge welulos pac, mweyen ma moul inge pa nununkalos.
Akerubiwo ankati akayima, mikombero inkayimanso. Ngati akerubiwo auluka, mikomberoyo inkapita nawo chifukwa mzimu wa zamoyozo ndiwo unkayendetsa mikomberoyo.
18 Ouinge kalem wolana lun LEUM GOD som liki nien utyak nu ke Tempul, ac mukuila nu ke sie acn lucng liki cherub uh.
Pamenepo ulemerero wa Yehova unachoka pa chiwundo cha Nyumba ya Mulungu ndi kukakhala pamwamba pa akerubi.
19 Elos asroelik posohksok lalos ac sohkak liki faclu ke nga liye ah, ac wheel uh welulos pac. Elos tui ke mutunpot layen kutulap ke Tempul, ac kalem saromrom sac oan faclos.
Ine ndikuona akerubi, anatambasula mapiko awo ndi kuwuluka. Pamene ankapita, mikombero inapita nawo pamodzi. Akerubi anakayima pa khomo la chipata cha kummawa cha Nyumba ya Yehova. Tsono ulemerero wowala wa Mulungu wa Israeli unali pamwamba pawo.
20 Na nga akilen lah cherub inge nuna ma orekla moul ma nga tuh liye ye God lun Israel e pe Infacl Chebar ah.
Izi ndizo zamoyo ndinaziona pansi pa Mulungu wa Israeli ku mtsinje wa Kebara, ndipo ndinazindikira kuti anali akerubi.
21 Kais sie selos oasr muta akosr la ac posohksok akosr, ac ye kais sie posohksok oasr ma se oana luman poun mwet.
Kerubi aliyense anali ndi nkhope zinayi ndi mapiko anayi, ndipo kunsi kwa mapiko awo kunali chinthu chimene chimaoneka ngati manja a munthu.
22 Mutalos luman na muta nga tuh liye pe Infacl Chebar. Kais sie cherub inge ac mukuila suwosna nu meet.
Nkhope zawo zinali zofanana ndi zomwe ndinaziona ku mtsinje wa Kebara. Kerubi aliyense amayenda molunjika.

< Ezekiel 10 >