< Exodus 9 >

1 LEUM GOD El fahk nu sel Moses, “Utyak nu ye mutal tokosra ac fahk nu sel lah LEUM GOD lun mwet Hebrew El fahk, ‘Lela mwet luk in som, tuh elos in ku in alu nu sik.
Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Pita kwa Farao ndipo ukamuwuze kuti Yehova, Mulungu wa Ahebri akuti alole anthu anga apite kuti akandipembedze.
2 Kom fin sifilpa srunga fuhlela elos in som,
Koma ngati ukana kuti apite ndi kupitiriza kuwaletsa,
3 nga ac kai kom, ac supwaot sie mas na upa nu fin kosro nukewa — horse nutum, donkey nutum, camel, cow, sheep ac nani.
dzanja la Yehova lidzakantha ziweto zako zimene zili ku munda, pamodzi ndi akavalo, abulu, ngamira, ngʼombe, nkhosa ndi mbuzi ndi mliri woopsa kwambiri.
4 Nga fah sraclik kosro nutin mwet Israel liki kosro nutin mwet Egypt, na ac fah wangin kosro nutin mwet Israel misa.
Koma Yehova adzasiyanitsa pakati pa ziweto za Israeli ndi ziweto za Igupto, kotero kuti palibe chiweto nʼchimodzi chomwe cha Aisraeli chimene chidzafe.”
5 Nga, LEUM GOD, oakiya tuh lutu nga fah oru ma inge.’”
Yehova anayika nthawi ndipo anati, “Yehova adzachita zimenezi mmawa mʼdziko muno.”
6 Len se toko, LEUM GOD El oru oana El fahk, ac kosro nukewa nutin mwet Egypt ah misa, a tia soko kosro nutin mwet Israel misa.
Ndipo mmawa mwake Yehova anachitadi zimenezi. Ziweto zonse za Aigupto zinafa, koma palibe chiweto ndi chimodzi chomwe cha Aisraeli chomwe chinafa.
7 Tokosra el sapla siyuk lah mea sikyak, na fwackyang nu sel lah wangin sokofanna kosro nutin mwet Israel misa. Tusruktu upa na nankal ac el tia lela mwet ah in som.
Farao anatuma anthu kuti akafufuze ndipo anapeza kuti palibe chiweto chilichonse cha Aisraeli chomwe chinafa. Komabe mtima wake sunagonje ndipo iye sanalole kuti anthu apite.
8 Na LEUM GOD El fahk nu sel Moses ac Aaron, “Eis kutu apat an inpoumtal liki funyu uh, na Moses elan sisak nu lucng ye mutal tokosra.
Kenaka Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni, “Tapani phulusa la pa moto lodzaza dzanja ndipo Mose aliwaze mmwamba pamaso pa Farao.
9 Ac fah sokelik oana fofosr lun fohkfok fin acn nukewa lun Egypt, ac yen nukewa ac sikyak faf su ac orala ruf aryur fin mwet ac fin kosro.”
Phulusalo lidzasanduka fumbi pa dziko lonse la Igupto. Tsono fumbilo lidzasanduka zithupsa zomaphulika nʼkukhala zilonda pa munthu aliyense ndi pa nyama zomwe mʼdziko lonse la Igupto.”
10 Ouinge eltal eis kutu apat ac tu ye mutal tokosra. Moses el sisak nu lucng, ac apat uh ekla faf su orala ruf aryur ke monin mwet ac kosro uh.
Kotero anatenga phulusa la pa moto ndi kuyima pamaso pa Farao. Mose analiwaza mmwamba, ndipo panabuka zotupa zophulika zokha pa munthu aliyense ndi pa ziweto.
11 Mwet orek inutnut uh koflana tuku nu ye mutal Moses, mweyen manolos wi afla ke faf, oana mwet Egypt nukewa ngia.
Amatsenga sanathe kumuyandikira Mose chifukwa nawonso anali ndi zithupsa monga mmene analili Aigupto ena onse.
12 Na LEUM GOD El akupaye nankal tokosra, tuh elan tia lungse lohngol Moses ac Aaron, oana ke LEUM GOD El tuh fahk nu sel Moses meet ah.
Koma Yehova anawumitsa mtima wa Farao ndipo iye sanamvere Mose ndi Aaroni monga momwe Yehova anamuwuzira Mose.
13 Na LEUM GOD El fahk nu sel Moses, “Toangna lutu, kom in som tu ye mutal tokosra ac fahkang nu sel lah LEUM GOD lun mwet Hebrew El fahk, ‘Fuhlela mwet luk in som, tuh elos in ku in alu nu sik.
Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Mawa mmawa upite ukakumane ndi Farao maso ndi maso ndipo ukamuwuze kuti Yehova Mulungu wa Ahebri akuti ulole anthu anga apite kuti akandipembedze.
14 Pacl se inge nga ac supwaot mwe ongoiya upa nukewa luk nu fom ac nu fin mwet fulat lom ac mwet lom, tuh kom fah etu lah wangin sie oana nga fin faclu nufon.
Ngati suwalola, tsopano ndidzagwetsa miliri yanga yonse pa iwe ndi nduna zako ndiponso pa anthu ako, kuti udziwe kuti palibe wina wofanana nane pa dziko lonse lapansi.
15 Nga funu srukak pouk in lain kom ac mwet lom ke mas, kowos lukun wanginla na pwaye.
Pakuti ndikanakhala nditatukula kale dzanja langa ndikupheratu iwe pamodzi ndi anthu ako onse pa dziko lapansi.
16 Tusruktu sripa se sis nga lela kom in moulna, tuh in fahkak ku luk nu sum, ac inek in pwengelik nu fin faclu nufon.
Koma ndakuyika kukhala mfumu ndi cholinga choti ndionetse mphamvu zanga kwa iwe ndiponso kuti dzina langa litchuke pa dziko lonse lapansi.
17 Ne ouinge, kom srakna inse fulat ac tia lungse lela mwet luk uh in som.
Komabe iwe ukudzitukumula pa anthu anga osawalola kuti atuluke.
18 Ke pacl se na inge lutu, nga fah oru sie af na matol ac af yohk kosra, su tia liyeyuk oemeet me in acn Egypt.
Nʼchifukwa chake mawa, nthawi ngati ino, ndidzagwetsa matalala amphamvu amene sanagwepo pa Igupto, kuyambira pachiyambi mpaka lero.
19 Inge sapkin tuh kosro nutum ac ma nukewa saya ma muta in imah uh in utukyak nu in lohm uh. Af yohk kosra ac fah kahki nu fin mwet ac kosro ma mutana in imae ac tia utukyak nu in lohm ah, ac elos nukewa fah misa.’”
Tsopano lamula kuti ziweto zanu zonse ndi zinthu zonse zomwe zili ku minda kuti zilowetsedwe mʼkhola, chifukwa matalala adzagwera munthu aliyense ndi chiweto chilichonse chimene sichidzalowetsedwa mʼkhola ndipo zimene zidzakhala zili ku munda zidzafa.”
20 Kutu sin mwet fulat lal tokosra elos sangeng ke ma LEUM GOD El fahk inge, oru elos usak mwet kohs lalos ac kosro natulos nu in lohm ah.
Nduna za Farao zinachita mantha ndi mawu a Yehova, ndipo zinalowetsa antchito awo ndi ziweto zawo mʼnyumba.
21 A kutu mwet uh tia lohang nu ke ma LEUM GOD fahk, ac fuhlelana mwet kohs lalos ac kosro natulos in mutana in imae.
Koma iwo amene ananyozera mawu a Yehova anasiya akapolo ndi ziweto zawo panja.
22 Na LEUM GOD El fahk nu sel Moses, “Sralak poum nu lucng, ac af yohk kosra fah kahki nu fin mutunfacl Egypt nufon — nu fin mwet, kosro, ac mwe yok in imae nukewa.”
Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Kweza dzanja lako kumwamba kuti matalala agwe pa dziko lonse la Igupto, pa munthu aliyense, pa ziweto ndi pa zonse zomera mʼminda ya Igupto.”
23 Ouinge Moses el srukak sikal lal ac kolak nu lucng, ac LEUM GOD El supweya pulahl ac af yohk kosra, ac sarom kasri nu in fohk uh. LEUM GOD El supweya
Mose ataloza ndodo yake kumwamba, Yehova anatumiza mabingu ndi matalala ndi ziphaliwali zongʼanima pa nthaka. Kotero Yehova anagwetsa matalala pa dziko la Igupto.
24 af na matol ac yohk kosra, ac oasr sarom yen nukewa. Paka se inge upa liki kutena paka ma sikyak meet in acn Egypt.
Matalala anagwa ndipo ziphaliwali zinangʼanima. Inali mphepo ya mkuntho yoopsa kwambiri imene sinakhaleponso mʼdziko lonse la Igupto chiyambire pamene Aigupto anakhala mtundu woyima pa okha.
25 Fin acn Egypt nufon, af upa se inge kunausla ma nukewa ma oan likinum ac in imae, weang mwet ac kosro — kunausla mahsrik nukewa ac koteya sak nukewa.
Matalala anawononga dziko lonse la Igupto, munthu aliyense pamodzi ndi ziweto. Matalala aja anawononga zomera zonse za mʼmunda ndi kukhadzula mtengo uliwonse.
26 Acn Goshen mukena, yen mwet Israel muta we, pa wangin af upa we.
Ku malo kokhako kumene matalala sanafikeko ndi dera la Goseni kumene kunali Aisraeli.
27 Tokosra el sapla solalma Moses ac Aaron, ac fahk nu seltal, “Nga sifacna fahkyuyak inge lah oasr ma koluk luk. LEUM GOD pa suwohs, ac nga ac mwet luk uh pa tafongla.
Kenaka Farao anayitanitsa Mose ndi Aaroni nati kwa iwo, “Tsopano ndachimwa, Yehova ndi wolungama, ine ndi anthu anga ndife olakwa.
28 Pre nu sin LEUM GOD, mweyen pulahl ac af yohk kosra inge arulana upala nu sesr! Nga wuleot in filikowosla in som. Kowos tia enenu in sifilpa muta yenu.”
Upemphere kwa Mulungu chifukwa mabingu ndi matalala atikwana. Ine ndidzakulolani kuti mupite. Simuyenera kukhalabe kuno.”
29 Moses el fahk nu sel, “Pacl se na nga illa liki siti uh, nga fah sralak pouk in pre nu sin LEUM GOD. Pulahl ac fah tui, ac ac fah wanginla af upa, tuh kom fah ku in etu lah faclu ma lun LEUM GOD.
Mose anayankha, “Ndikangotuluka mu mzinda muno, ine ndidzakweza manja anga kwa Yehova ndi kupemphera. Mabingu ndi matalalawa adzaleka ndipo inu mudzadziwa kuti Yehova ndiye akulamulira dziko lapansi.
30 Tusruktu nga etu lah kom ac mwet fulat lom srakna tia sangeng sin LEUM GOD.”
Koma ine ndikudziwa kuti inu ndi nduna zanu simukuopabe Yehova Mulungu.”
31 Flax ac barley kunausyukla ke af upa sac, mweyen barley ah mwesrla ac flax ah tufacna fokla.
Thonje ndi barele zinawonongeka, popeza barele anali atakhwima ndi thonje linali ndi maluwa.
32 Tusruktu wangin wheat musalla, mweyen soenna kapak.
Koma tirigu ndi mchewere sizinawonongeke chifukwa zimakhwima mochedwa.
33 Moses el som lukel tokosra, illa liki siti uh, ac sralak paol nu lucng ac pre nu sin LEUM GOD. Na pulahl wi af yohk kosra ah tui, ac tiana sifilpa af.
Mose anasiyana ndi Farao natuluka mu mzindawo. Iye anakweza manja ake kwa Yehova. Mabingu ndi matalala zinaleka, ndipo mvula inalekeratu kugwa mʼdzikolo.
34 Ke tokosra el liye ma sikyak uh, el sifilpa orekma koluk. El ac mwet fulat lal ah sifilpa akupaye nankalos.
Farao ataona kuti mvula, matalala ndi mabingu zaleka, anachimwanso. Iye ndi nduna zake anawumitsanso mitima yawo.
35 Na in oana ke LEUM GOD El tuh fahk nu sel Moses meet mu tokosra el ac mau tia lela mwet Israel in som, ouinge el tiana lela.
Choncho Farao sanalole kuti Aisraeli apite monga momwe Yehova anamuwuzira Mose.

< Exodus 9 >