< Esther 7 >

1 Ouinge tokosra ac Haman som in mongo yorol Esther
Choncho mfumu ndi Hamani anabwera kudzadya phwando la mfumukazi Estere.
2 ke pacl se akluo. Ke pacl eltal nim wain, tokosra el sifilpa siyuk, “Kasra Esther, fahk nu sik ma kom lungse, ac nga ac fah sot nu sum. Kom finne siyuk ke tafu tokosrai luk, ac fah itukot nu sum.”
Pa tsiku lachiwiri akumwa vinyo, mfumu inafunsanso kuti, “Kodi iwe mfumukazi Estere, chimene ufuna kupempha nʼchiyani? Chimene uti upemphe ndidzakupatsa. Choncho ukufuna chiyani? Ngakhale utafuna theka la ufumu ndidzakupatsa.”
3 Kasra Esther el topuk, “Fin oh lungse lun Tokosra, ac el fin insewowo in porongo mwe siyuk luk, pa inge ma nga kena kac, tuh nga in ku in moul, wi pac mwet srahk.
Kenaka mfumukazi Estere anayankha kuti, “Ngati mwandikomera mtima, inu mfumu, ndipo ngati chingakukomereni mfumu, pempho ndi chokhumba changa ndi ichi, mulole kuti ine ndi abale anga tisungidwe tonse ndi moyo.
4 Nga ac mwet srahk kukakinyukla tari in anwuki. Funu kukakinyukla kut nu ke mwet kohs, nga lukun misla na ac tia lusrong tokosra. Tusruktu akoeyuk in sikiyukla kut — kut nukewa ac wanginla!”
Popeza ine ndi anthu a mtundu wanga tagulitsidwa kuti atiwononge, atiphe ndi kutifafaniziratu. Akanangotigulitsa kokha tikanakhala chete, chifukwa chimene mdani wathuyo akanakupatsani mfumu sibwenzi mutasowa nacho mtendere.”
5 Na Tokosra Ahasuerus el siyuk sel Kasra Esther, “Su enum se ku in oru ouinge— Pia mwet sacn?”
Mfumu Ahasiwero anamufunsa mfumukazi Estere, “Kodi iyeyu ndi ndani ndipo ali kuti amene saopa kuchita chinthu chotere?”
6 Esther el topuk, “Mwet lokoalok lasr, su akola in kalyei kut, pa mwet koluk se inge Haman!” Haman el ngetang nu sel tokosra ac kasra, ac el rarrar ke sangeng.
Estere anati, “Wotizunza ndiponso mdani wathu! Munthu woyipayo ndi Hamani.” Kenaka Hamani anagwidwa ndi mantha pamaso pa mfumu ndi mfumukazi.
7 Tokosra el arulana foloyak ac tuyak som liki kufwa uh, ac illa nu likinuma nu ke ima ros lun inkul fulat. Haman el akilen lah tokosra el akola in sang kalya na yohk nu sel ke ma se inge, oru el mutana in kwafe sel Kasra Esther elan molella.
Mfumu itakwiya kwambiri inanyamuka pa phwando nipita ku munda wa maluwa wa nyumba yaufumu. Koma Hamani, pozindikira kuti mfumu yaganiza kale kumuchitira choyipa, anatsalira mʼnyumba kupempha Estere kuti apulumutse moyo wake.
8 El tufahna fungyang nu fin mwe oan se Esther el muta fac in kwafe elan nunak munas nu sel, ke pacl se tokosra el sifilpa utyak nu in lohm uh liki imae. Tokosra el wola, “Ya mwet se inge ac sruinkuel kasra ye mutuk in lohm uh?” Ke pacl se tokosra el fahkla kas inge, mwet eunuch uh afinya mutal Haman.
Mfumu itabwerera kuchokera ku munda wa maluwa wa nyumba yaufumu uja ndi kulowanso mʼchipinda chaphwando, anapeza Hamani atagona chafufumimba pa mpando wa khutagone pomwe Estere anakhalapo. Mfumu inayankhula mokweza kuti, “Kodi afunanso kuvula mfumukazi momukakamiza pamene ine ndili mʼnyumba?” Mfumu isanatsirize kuyankhula mawu awa, atumiki ake anaphimba nkhope ya Hamani.
9 Na sie sin mwet eunuch lal tokosra pangpang Harbona el fahk, “Sie pac ma Haman el oru pa el musaela sie nien loksak fit itngoul limekosr fulata pe lohm sel elan srupsrulak Mordecai kac, el su tuh molela moul lun tokosra!” Tokosra el sapkin, “Srupsrulak Haman olo!”
Haribona, mmodzi wa adindo ofulidwa amene ankatumikira mfumu anati, “Mtanda wotalika mamita 23 uli mʼnyumba ya Hamani. Mtandawu, Hamani anapangira Mordekai, uja amene anapulumutsa mfumu ku chiwembu.” Mfumu inati, “Mpachikeni pamenepo!”
10 Ouinge sripsripyak Haman ke nien loksak se su el musaela nu sel Mordecai. Na tufah ohula kasrkusrak lal tokosra.
Choncho anamupachika Hamani pa mtanda umene anakonzera Mordekai. Kenaka mkwiyo wa mfumu unatsika.

< Esther 7 >