< Ecclesiastes 9 >

1 Nga nunak yohk ke ma inge nukewa ke pacl na loeloes, ac nga liye lah God pa nununku mukuikui lun mwet lalmwetmet ac mwet suwoswos, finne nu ke lungse lalos ac srunga lalos. Wangin sie mwet etu lah mea oan meeto.
Ndinalingalira zonse ndanenazi ndipo ndinapeza kuti anthu olungama ndi anthu anzeru ali mʼmanja mwa Mulungu pamodzi ndi zimene amachita, koma palibe amene amadziwa zimene zikumudikira mʼtsogolo mwake, kaya chikondi kapena chidani.
2 Oana sie ma nukewa. Lumah sefanna ac tuku nu sin mwet suwoswos ac mwet sesuwos, nu sin mwet wo ac nu sin mwet koluk, nu sin mwet alu ac nu sin mwet tia alu, nu sin mwet orek kisa ac mwet tia orek kisa. Ma su sikyak nu sin sie mwet wo ac sikyak pacna nu sin sie mwet koluk. Sie mwet su orek wulela nu sin God el oapana mwet se ma tia orek wulela nu sin God.
Onsewa mathero awo ndi amodzi, anthu olungama ndi anthu oyipa, abwino ndi oyipa, oyera ndi odetsedwa, amene amapereka nsembe ndi amene sapereka nsembe. Zomwe zimachitikira munthu wabwino, zimachitikiranso munthu wochimwa, zomwe zimachitikira amene amalumbira, zimachitikiranso amene amaopa kulumbira.
3 Saflaiyen moul lun mwet nukewa ac oana sie, ac ma se inge tiana suwohs. Ke lusenna moul lun mwet uh, nunak lalos sessesla ke nunak koluk ac wel, na elos misa.
Choyipa chimene chili mʼzonse zochitika pansi ndi ichi: Mathero a zonse ndi amodzi. Ndithu, mitima ya anthu ndi yodzaza ndi zoyipa, ndipo mʼmitima mwawo muli zamisala pamene ali ndi moyo, potsiriza pake iwo amakakhala pamodzi ndi anthu akufa.
4 Tusruktu kutena mwet su moul inmasrlon ma moul uh, oasr finsrak yorolos. Soko kosro ngalngul ma moul, wo liki soko lion ma misa.
Aliyense amene ali ndi moyo amakhala ndi chiyembekezo, pajatu galu wamoyo aposa mkango wakufa!
5 Aok, mwet moul etu lah elos ac misa, a mwet misa wangin ma elos etu. Wangin mwe usru elos ac sifil eis. Mulkinyukla na pwaye elos.
Pakuti amoyo amadziwa kuti adzafa, koma akufa sadziwa kanthu; alibe mphotho ina yowonjezera, ndipo palibe amene amawakumbukira.
6 Lungse lalos, srunga lalos, kena lalos, nufonna welulos na misa. Ac fah tia sifilpa oasr ma kunalos ke kutena ma su sikyak fin faclu.
Chikondi chawo, chidani chawo ndiponso nsanje yawo, zonse zinatha kalekale; sadzakhalanso ndi gawo pa zonse zochitika pansi pano.
7 Ouinge kom in kang mongo nom ac engan. Nim wain nimom ke inse pwar. God El nuna oaki in ouinge.
Pita, kadye chakudya chako mokondwera ndi kumwa vinyo wako ndi mtima wosangalala, pakuti tsopano Mulungu akukondwera ndi zochita zako.
8 Pacl nukewa kom in naweyukla ac akmusrala in fal nu ke pacl in engan.
Uzivala zovala zoyera nthawi zonse, uzidzola mafuta mʼmutu mwako nthawi zonse.
9 Engankin moul lom yurin mutan kiom su kom lungse, ke lusenna moul lusrongten ma God El sot nu sum fin faclu. Engankin kais sie len lusrongten inge, mweyen pa na ingan ma kom ac eis ke orekma kemkatu nukewa lom.
Uzikondwerera moyo pamodzi ndi mkazi wako amene umamukonda, masiku onse a moyo uno wopanda phindu, amene Mulungu wakupatsa pansi pano. Pakuti mkaziyo ndiye gawo la moyo wako pa ntchito yako yolemetsa pansi pano.
10 Kutena ma kom oru, oru ke kuiyom mweyen ac fah wangin mukuikui, wangin nunak, wangin etauk, wangin lalmwetmet in facl sin mwet misa, tuh pa ingan acn se kom ac som nu we uh. (Sheol h7585)
Ntchito iliyonse imene ukuyigwira, uyigwire ndi mphamvu zako zonse, pakuti ku manda kumene ukupita kulibe kugwira ntchito, kulibe malingaliro, chidziwitso ndiponso nzeru. (Sheol h7585)
11 Oasr sie pac ma nga akilen ke moul lasr faclu: mwet mui uh tia eis kutangla pacl nukewa, ac mwet pulaik uh tia eis kutangla ke mweun pacl nukewa. Mwet lalmwetmet uh tia eis kasrpalos pacl nukewa, mwet usrnguk uh tia kasrup pacl nukewa, ac mwet ma fas ke orekma tia eis wal fulat pacl nukewa. Ma ongla ouiya uh sikyak nu sin mwet nukewa.
Ine ndinaonanso chinthu china pansi pano: opambana pa kuthamanga si aliwiro, kapena opambana pa nkhondo si amphamvu, ndiponso okhala ndi chakudya si anzeru, kapena okhala ndi chuma si odziwa zambiri, kapena okomeredwa mtima si ophunzira; koma mwayi umangowagwera onsewa pa nthawi yake.
12 Kom tia ku in etu lah pacl lom uh ac tuku ngac. Oana won ma sremla ke sruhf in kitin pacl na, ku oana ik ma sremla ke kwa, kut ac sremla pac ke sie pacl na koluk ma kut tiana etu kac.
Kungoti palibe munthu amene amadziwa kuti nthawi yake idzafika liti: monga momwe nsomba zimagwidwira mu ukonde, kapena mmene mbalame zimakodwera mu msampha, chimodzimodzinso anthu amakodwa mu msampha pa nthawi yoyipa, pamene tsoka limawagwera mosayembekezera.
13 Oasr pac sie ma nga liye, sie mwe srikasrak na wo ke nunkeyen lalmwetmet uh sin mwet faclu.
Ine ndinaonanso pansi pano chitsanzo ichi cha nzeru chimene chinandikhudza kwambiri:
14 Oasr sie siti srisrik ma mwet na pu muta we. Na sie tokosra na ku tuku mweuni acn sac. El kuhlusya ac akoo in fokolak pot uh ac utyak.
Panali mzinda waungʼono umene unali ndi anthu owerengeka. Ndipo mfumu yamphamvu inabwera kudzawuthira nkhondo, inawuzungulira ndi kumanga mitumbira yankhondo.
15 Oasr sie mukul wi muta in acn sac. El sukasrup, tuh el lalmwetmet, ac el ku na in molela siti sac. Tusruktu wanginna mwet lohang nu sel.
Tsono mu mzindamo munali munthu wosauka koma wanzeru, ndipo anapulumutsa mzindawo ndi nzeru zakezo. Koma palibe amene anakumbukira munthu wosaukayo.
16 Nga fahk pacl nukewa lah lalmwetmet uh wo liki ku, tusruktu wangin mwet nunku mu mwet sukasrup ku in lalmwetmet, pwanang elos tiana lohang nu ke ma mwet sukasrup uh fahk.
Choncho ine ndinati, “Nzeru ndi yopambana mphamvu.” Koma nzeru ya munthu wosauka imanyozedwa, ndipo palibe amene amalabadirako za mawu ake.
17 Wo in porongo pusra fisrasr lun sie mwet lalmwetmet, liki pusren wowoyak lun sie mwet kol inmasrlon mwet lalfon.
Mawu oyankhula mofatsa a munthu wanzeru, anthu amawasamalira kwambiri kupambana kufuwula kwa mfumu ya zitsiru.
18 Yohk ma wo tuku ke lalmwetmet liki na kufwen mwe mweun, tusruk sie mwet koluk el ku in forteya ma wo puspis.
Nzeru ndi yabwino kupambana zida zankhondo, koma wochimwa mmodzi amawononga zinthu zambiri zabwino.

< Ecclesiastes 9 >