< Ecclesiastes 6 >

1 Nga liye pac lah fin facl se inge oasr sie ma koluk na yohk sikyak, ac mwet puspis wi pulakin.
Ine ndinaona choyipa china pansi pano, ndipo chimasautsa anthu kwambiri:
2 God El ac sang mwe kasrup, sunak, ac acn nu sin sie mwet, aok el fas ke ma lungse lal nukewa. Na tok God El tia lela nu sel in engan kac. Siena mwet pa ac insewowokin, ac tia el. Tiana suwohs in ouinge. Arulana wangin sripa.
Mulungu amapereka chuma, zinthu ndi ulemu kwa munthu, kotero kuti munthuyo sasowa kanthu kalikonse kamene akukalakalaka, koma Mulungu samulola kuti adyerere zinthuzo, ndipo mʼmalo mwake amadyerera ndi mlendo. Izi ndi zopandapake, ndi zoyipa kwambiri.
3 Mwet se fin oasr foko tulik natul ac loes moul lal, tusruktu tu el finne moul paht a el tia insewowo in moul lal, ku fin tia pukpuki el in wo, na nga ku in fahk mu wo nu sin tulik fusr se ma misa na osweyukla, liki mwet sac.
Ngakhale munthu atabereka ana 100 ndi kukhala ndi moyo zaka zambiri; komatu ngakhale atakhala zaka zambiri chotani, ngati iye sangadyerere chuma chake ndi kuyikidwa mʼmanda mwaulemu, ine ndikuti mtayo umamuposa iyeyo.
4 Wangin sripa in osweyukla tulik sac — el wanginla nu in lohsr, yen mulkinyukla el we.
Mtayo umangopita pachabe ndipo umapita mu mdima, ndipo mu mdimamo dzina lake limayiwalika.
5 El tiana liye kalem lun len uh, ku etu kutena ma ke luman moul uh, tusruktu el konauk mongla —
Ngakhale kuti mtayowo sunaone dzuwa kapena kudziwa kanthu kalikonse, koma umapumula kuposa munthu uja,
6 yohk liki na mwet se ma tiana insewowokin moul lal uh el finne moul yac luo tausin. Kalem lah eltal kewa ac som nu yen sefanna.
ngakhale munthuyo atakhala ndi moyo zaka 2,000, koma ndi kulephera kudyerera chuma chake. Kodi onsewa sapita malo amodzi?
7 Sie mwet el oru orekma lal nukewa ma na in konauk mwe mongo nal, tusruktu wangin pacl el muti kac.
Ntchito yonse ya munthu imathera pakamwa pake, komatu iye sakhutitsidwa ndi pangʼono pomwe.
8 Mea ac wo nu sin mwet lalmwetmet se liki mwet lalfon se? Oayapa wangin ma ac wo nu sin sie mwet sukasrup el finne moulkin moul wo inmasrlon mwet uh.
Kodi munthu wanzeru amaposa motani chitsiru? Kodi munthu wosauka amapindula chiyani podziwa kukhala bwino pamaso pa anthu ena?
9 Ma inge ma lusrongten — oana ukweyen eng uh. Wo kom in falkin ma oasr yurum, liki kom in mwel kutu pacna ma saya pacl nukewa.
Kuli bwino kumangoona zinthu ndi maso kusiyana ndi kumangozilakalaka mu mtima. Izinso ndi zopandapake, nʼkungodzivuta chabe.
10 Ma nukewa ma sikyak uh nuna oakwuki oemeet me, ac kut nukewa etu lah sie mwet el tia ku in akukuin nu sin sie su ku lukel.
Chilichonse chimene chilipo anachitchula kale dzina, za mmene munthu alili nʼzodziwika; sangathe kutsutsana ndi munthu amene ali wamphamvu kupambana iyeyo.
11 Kom finne kaskas pusla ke akukuin, ac nuna wangin sripa wo ac tuku kac, ac kom tia pac eis wo kac.
Mawu akachuluka zopandapake zimachulukanso, nanga munthu zimamupindulira chiyani?
12 Su ku in etu lah mea ac wo emeet nu sin sie mwet ke lusen moul fototo ac lusrongten se inge — sie moul su ac wanginla oana lul in pukunyeng? Su ku in etu ma ac sikyak fin faclu tukun kut misa?
Pakuti ndani amene amadziwa chomwe ndi chabwino pa moyo wa munthu, pakuti moyo wake ndi wa masiku ochepa ndi opandapake, umangopitira ngati mthunzi. Ndani amene angamufotokozere zimene zidzachitika pansi pano iye atapita?

< Ecclesiastes 6 >