< Ecclesiastes 2 >

1 Nga sulela ngan suk mwe akpwaryeyu tuh ngan ku in etu kalmen engan. Tusruktu nga konauk lah ma se inge wangin pac sripa.
Ine ndinaganiza mu mtima mwanga, “Tsopano ndiyese zosangalatsa kuti ndipeze zomwe ndi zabwino.” Koma izi zinaonekanso kuti ndi zopandapake.
2 Nga konauk lah israsr uh ma lusrongten, ac mwe akpwar uh wangin pac sripa.
“Kuseka,” ndinati, “imeneyo ndi misala. Ndipo kodi chisangalalo chimabweretsa phindu lanji?”
3 Ke nga suk in akyokye lalmwetmet luk, nga sulela in akpwarye ikok ke wain, ngan sifacna pulakin lah mea lalfon. Nga tuh nunku mu ouiya se inge pa wo mwet uh in oru ke moul fototo lalos fin faclu.
Ndinayesa kudzisangalatsa ndi vinyo, koma umenewu unali uchitsiru, pamenepo nʼkuti maganizo anga akutsogozedwa ndi nzeru. Ine ndinkati mwina kapena njira yotero nʼkukhala yopambana, imene anthu amatsata pofuna kusangalala pa masiku owerengeka a moyo wawo.
4 Orekma na yohk nga orala tari. Nga musaela lohm puspis nu sik, ac yukwiya ima in grape sunuk.
Ndinagwira ntchito zikuluzikulu: Ndinadzimangira nyumba ndi kuwoka mipesa.
5 Nga yukwiya ima mwe intoe, oayapa ima in sak nukewa ma ku in mongo fahko kac.
Ndinalima madimba ndi minda yamitengo; ndipo ndinadzalamo mitengo ya zipatso za mitundu yonse.
6 Nga pukanak lulu in kof in akoyohuye ima uh.
Ndinakumba mayiwe osungiramo madzi woti ndizithirira minda ya mitengo yodzalidwa ija.
7 Nga moli mwet kohs puspis, mukul ac mutan, ac tulik natulos ma isusla inkul sik uh ma pac luk. Pisen cow ac sheep nutik pus liki kutena mwet saya su muta Jerusalem oemeet me.
Ndinagula akapolo aamuna ndi akapolo aakazi, ndiponso ndinali ndi akapolo ena omwe anabadwira mʼnyumba mwanga. Ndinalinso ndi ngʼombe ndi nkhosa zambiri kupambana aliyense mu Yerusalemu amene analipo ndisanabadwe.
8 Tokosra lun mutunfacl nga leumi uh elos use silver ac gold ac ma saok puspis nu in nien fil ma saok luk. Mukul ac mutan elos on in akpwaryeyu, ac oasr mutan kulansap puspis kiuk fal nu ke lungse luk.
Ndinadzikundikira siliva ndi golide, ndiponso chuma chochokera kwa mafumu ndi madera awo. Ndinali ndi amuna ndi akazi oyimba ndiponso azikazi; zinthu zokondweretsa mtima wa munthu.
9 Pwaye, nga fulat ac pwengpeng liki kutena mwet su muta Jerusalem emeet me, ac lalmwetmet luk kolyu pacl nukewa.
Ndinali munthu wotchuka kupambana wina aliyense mu Yerusalemu amene analipo ndisanabadwe. Mu zonsezi nzeru zanga zinali nane.
10 Kutena ma su nga lungse, nga eis. Nga tia sifacna ikolyuwi nu ke kutena mwe pwar. Nga konkin ke ma nukewa nga orala, ac insewowo luk kac uh pa molo nu sik.
Sindinadzimane chilichonse chimene maso anga anachifuna; mtima wanga sindinawumane zokondweretsa. Mtima wanga unakondwera ndi ntchito yanga yonse, ndipo iyi ndiyo inali mphotho ya ntchito zanga zonse zolemetsa.
11 Na nga nunku ke ma nukewa nga orala, ac ke lupan kemkatu luk in orala, ac nga akilen lah wanginna sripa — ma nukewa ma lusrongten, oana ukweyen eng uh.
Koma pamene ndinayamba kuyangʼanayangʼana zonse zimene ndinachita ndi manja anga, ndi zimene ndinazivutikira kuti ndizipeze, zonsezi zinali zopandapake; kungodzivuta chabe, palibe chomwe ndinapindula pansi pano.
12 Pwayeiya uh, sie tokosra el ac oru na ma tokosra meet lukel ah oru. Ouinge nga mutawauk nunku lah mea kalmac tuh sie mwet in lalmwetmet, ku in sununta, ku in lalfon.
Kenaka maganizo anga anayamba kulingalira zakuti nzeru nʼchiyani, komanso kuti misala ndi uchitsiru nʼchiyani. Kodi munthu wodzalowa ufumu tsopanoyo angachite chiyani choposa chimene chinachitidwa kale?
13 Na inge nga etu lah, “Lalmwetmet wo liki na lalfon, oana ke kalem uh wo liki lohsr.
Ndinaona kuti nzeru ndi yopambana uchitsiru, monga momwe kuwala kumapambanira mdima.
14 Mwet lalmwetmet elos ku in liye acn elos fahsr nu we, a mwet lalfon uh tia ku.” Tusruktu nga etu pac lah ouiya sefanna pa soanekut kewa.
Munthu wanzeru amayenda maso ali patsogolo, pamene chitsiru chimayenda mʼchimbulimbuli; koma ndinazindikira kuti chomwe chimawachitikira onsewo ndi chimodzi.
15 Nga sifacna nunku, “Ma ac sikyak nu sin mwet lalfon uh ac sikyak pacna nu sik. Ouinge mwe mea ngan lalmwetmet?” Na nga sifacna topuk, “Wangi — nwanginna pwaye sripa.”
Pamenepo ndinalingalira mu mtima mwanga, “Zochitikira chitsiru zidzandichitikiranso ine. Nanga tsono phindu langa nʼchiyani pakukhala wanzeru?” Ndinati mu mtima mwanga, “Ichinso ndi chopandapake.”
16 Wangin mwet esam mwet lalmwetmet uh, ac wangin mwet esam mwet lalfon. In len fahsru uh, kut nukewa ac fah mulkinyukla. Kut nukewa ac fah misa, mwet lalmwetmet ac mwet lalfon oana sie.
Pakuti munthu wanzeru, pamodzinso ndi chitsiru sadzakumbukiridwa nthawi yayitali; mʼmasiku amʼtsogolo awiriwo adzayiwalika. Mmene chimafera chitsiru ndi mmenenso amafera wanzeru!
17 Ke ma inge wanginna kalmen moul nu sik, mweyen wanginna ma nga eis kac sayen mwe lokoalok mukena. Ma nukewa ma lusrongten. Oana ngan ukwe na eng uh.
Kotero ndinadana nawo moyo chifukwa ntchito zimene zimagwiridwa pansi pano ndi zosautsa kwa ine. Ntchito zonsezo ndi zopandapake, nʼkungodzivuta chabe.
18 Orekma nukewa ma nga orala wanginna kalmeya nu sik, mweyen nga etu lah ac ma na lun mwet se ma aolyula,
Ine ndinadana nazo ntchito zonse zimene ndinazigwira pansi pano, chifukwa ndinayenera kudzazisiyira wina amene adzalowa mʼmalo mwanga.
19 na el ac ku in lalmwetmet, ku el ac ku in lalfon, su etu? Tusruktu el pa ac la ma nukewa ma nga kemkatu kac — ma nukewa ma lalmwetmet luk uh ase nu sik fin faclu. Ma inge nukewa ma lusrongten.
Ndipo ndani amadziwa kuti munthu ameneyo adzakhala wanzeru kapena chitsiru? Komabe munthuyo adzakhala wolamulira zonse zimene ndinazichita pansi pano mwa nzeru zanga. Izinso ndi zopandapake.
20 Ouinge nga auli lah nga arulana kemkatu kac.
Motero ndinayamba kutaya mtima chifukwa cha ntchito zonse zimene ndinazivutikira pansi pano.
21 Kom orekmakin lalmwetmet, etauk, ac pisrla lom nufon in orala sie ma, na kom ac filiya nu sin sie su tia wi orekma kac. Wanginna sripa, ac tia pac suwohs!
Pakuti munthu atha kugwira ntchito yake mwanzeru, chidziwitso ndi luntha, ndipo kenaka nʼkusiyira wina amene sanakhetserepo thukuta. Izinso ndi zopandapake ndiponso tsoka lalikulu.
22 Kom orekma ac fosrnga ke lusen moul lom nufon, ac mea nu sum kac?
Kodi munthu amapindulanji pa ntchito zonse zolemetsa ndi zodetsa nkhawa zimene amazichita pansi pano?
23 Ke lusen na moul lom, ma nukewa kom oru use na inse fosrnga ac inse toasr. Finne ke fong, nunak lom koflana mongla ke nunkeya. Ma inge nukewa ma lusrongten.
Masiku ake onse amakhala achisoni, ntchito yake imakhala yovuta; ngakhale usiku womwe, mtima wake supumula. Izinso ndi zopandapake.
24 Ma se wo emeet mwet se in oru pa elan mongo ac nim ac insewowokin ma el kosrani. Ac nga akilen lah finne ma inge, ma tuku sin God me.
Kwa munthu palibe chabwino china kuposa kudya, kumwa ndi kukondwerera ntchito zake. Izinso ndaona kuti ndi zochokera kwa Mulungu,
25 Su ku in mongo ku insewowokin moul lal God El fin tia sang nu sel?
pakuti popanda Iye, ndani angadye ndi kupeza chisangalalo?
26 God El sang lalmwetmet, etauk, ac insewowo nu selos su oru lungse lal, a El oru tuh mwet koluk uh in orekma, kosrani, ac karinganang, tuh ma elos eis in ku in itukyang nu selos su oru ma lungse lal. Ma inge nukewa ma lusrongten. Oana ukweyen eng uh.
Munthu amene amakondweretsa Mulungu, Mulunguyo amamusandutsa wanzeru, wozindikira ndi wachisangalalo, koma wochimwa, Mulungu amamupatsa ntchito yosonkhanitsa ndi kusunga chuma kuti adzachipereke kwa amene Mulunguyo amakondwera naye. Izinso ndi zopandapake, nʼkungodzivuta chabe.

< Ecclesiastes 2 >